< Левит 21 >
1 Господ рече още на Моисея: Говори на свещениците, Аароновите синове, и кажи им: Никой от вас да се не оскверни между людете си, заради мъртвец,
Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
2 освен за близък сродник, сиреч, за майка си, за баща си, за сина си, за дъщеря си, или за брата си;
Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
3 също и за сестра си девица, която е близка нему, и която не е била омъжена, заради нея може да се оскверни.
kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
4 Като началник на людете си да се не оскверни така щото да стане мръсен.
Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
5 Да не оплешат главата си, нито да бръснат краищата на брадата си, нито да правят порязвания по месата си.
“‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
6 Свети да бъдат на Бога си, и да не осквернят Името на Бога си; защото те принасят Господните чрез огън приноси, хляба на Бога си; затова, да бъдат свети.
Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
7 Да не вземат жена, която е блудница или осквернена, нито да вземат жена напусната от мъжа си; защото свещеникът е свет на Бога си.
“‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
8 Прочее, да го накараш да бъде свет, защото той принася хляба на твоя Бог; свет да ти бъде; защото Аз Господ, Който ви освещавам, съм свет.
Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
9 И ако дъщерята на някой свещеник се омърси с блудство, тя омърсява баща си; с огън да се изгори.
“‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
10 Но оня, който между братята си е велик свещеник, на чиято глава се е изляло мирото за помазване, и който се е посветил, за да облича свещените одежди, да не ткрива главата си, нито да раздира дрехите си,
“‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
11 нито да влиза при някой умрял, нито да се осквернява за баща си или за майка си;
Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
12 нито да излиза от светилището или да осквернява светилището на Бога си; защото посвещаването чрез помазване с мирото на Бога му е станало на него. Аз съм Господ.
Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
13 И той да вземе за жена девица;
“‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
14 вдовица, или напусната, или осквернена, или блудница да не взема; но девица от людете си да вземе за жена.
Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
15 И тъй, да не осквернява потомството си между людете си; защото Аз съм Господ, Който го освещавам.
kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
16 Господ говори още на Моисея, казвайки:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Говори на Аарона, като му речеш: Който от твоето потомство, във всичките им поколения, има недостатък, той да не пристъпва да принася хляб на Бога си.
“Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
18 Защото никой, който има недостатък, не бива да пристъпва: човек сляп, или куц, или със сплескан нос, или с нещо излишно,
Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
19 или човек със строшена нога, или строшена ръка,
munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
20 или гърбав, или завързляк, или с повредени очи, или със суха краста, или с лишаи, или килав.
kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
21 Ни един човек от потомството на свещеника Аарона, който има недостатък, да не пристъпва за да принесе Господните чрез огън приноси; понеже има недостатък, ни бива да пристъпи да принесе хляба на Бога си.
Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
22 От пресветите и от светите приноси нека яде хляба на Бога си;
Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
23 но да не влиза до завесата нито да се приближава при олтара, понеже има недостатък, за да не омърсява светилищата Ми; защото Аз съм Господ, Който ги освещавам.
Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
24 И тъй, Моисей каза това на Аарона и на синовете му, и на всичките израилтяни.
Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.