< Левит 20 >

1 Господ говори още на Моисея, казвайки:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Да речеш на израилтяните: Който от израилтяните, или от заселените в Израиля чужденци, даде от семето си на Молоха, непременно да се умъртви; людете на земята да го убият с камъни.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
3 Също Аз ще насоча лицето Си против оня човек и ще го изтребя изсред людете му, защото е дал от семето си на Молоха, та е омърсил светилището Ми и е осквернил светото Ми Име.
Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
4 И ако по какъв да е начин людете на земята затворят очите си, за да не видят тоя човек, когато дава от семето си на Молоха, и не го погубят,
Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
5 тогава Аз ще насоча лицето Си против тоя човек и против семейството му, и ще изтребя изсред людете им него и всички, които го последват в блудството, за да блудствуват след Молоха.
Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
6 И човек, който се отнесе към запитвачите на зли духове и към врачовете за да блудствува след тях, против оня човек Аз ще насоча лицето Си и ще го изтребя изсред людете му.
“‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
7 И тъй, осветете се и бъдете свети, защото Аз съм Господ вашият Бог;
“‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
8 и да пазите повеленията Ми и да ги вършите. Аз съм Господ, Който ви освещавам.
Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
9 Всеки, който прокълне баща си или майка си, непременно да се умъртви; баща си или майка си е проклел; кръвта му да бъде върху него.
“‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
10 Ако прелюбодействува някой с чужда жена, тоест, ако прелюбодействува някой с жената на ближния си, непременно да се умъртви и прелюбодеецът и прелюбодейката.
“‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
11 Който легне с жената на баща си, бащината голота е открил; непременно и двамата да се умъртвят; кръвта им да бъде върху тях.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
12 И ако някой легне със снаха си, непременно и двамата да се умъртвят; мърсота са извършили; кръвта им да бъде върху тях.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
13 Ако някой легне с мъжко, като с женско, и двамата са извършили гнусота; непременно да се умъртвят; кръвта им да бъде върху тях.
“‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
14 Ако някой вземе жена и майка й, това е беззаконие; с огън да се изгорят и той и те, за да няма беззаконие между вас.
“‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
15 Ако някой се съвъкупи с животно, той непременно да се умъртви, и животното да убиете.
“‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
16 И ако се приближи жена при какво да е животно, за да се съвъкупи с него, да убиеш и жената и животното; непременно да се умъртвят; кръвта им да бъде върху тях.
“‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
17 Ако някой вземе сестра си, дъщеря на баща си, или дъщеря на майка си, и види голотата й, и тя види неговата голота, това е нечестие, да се изтребят пред очите на людете си; голотата на сестра си е открил; ще носи беззаконието си.
“‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
18 И който легне с жена, която е в нечистотата си, и открие голотата й, той е открил течението й, и тя е открила течението на кръвта си; за това, да се изтребят и двамата изсред людете си.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
19 Голотата на майчината си сестра или на бащината си сестра да не откриеш; защото, който е сторил това, открил е голотата на близките си роднини; те ще носят беззаконието си.
“‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
20 И ако някой легне със стрина си, голотата на стрина си е открил; те ще носят греха си; бездетни ще умрат.
“‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
21 И ако някой вземе братовата си жена, това е нечистота; братовата си голота е открил; баздетни ще останат.
“‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
22 Пазете, прочее, всичките Ми повеления и всичките Ми съдби та ги извършвайте, за да не ви избълва земята, гдето Аз ви завеждам да живеете в нея.
“‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
23 И да не ходите по обичаите на населението, което Аз изпъждам отпред вас; защото те извършиха всички тия гнусоти, и затова Аз се погнусих от тях.
Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
24 А на вас съм казал: Вие ще наследите земята им, и Аз ще я дам на вас за притежание, земя гдето текат мляко и мед. Аз съм Господ вашият Бог, който ви отделих от племената.
Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
25 За това, правете разлика между чистите животни и нечистите, и между нечистите птици и чистите; и да не осквернявате себе си с животно, или с птица, или с какво да е що пълзи на земята, които Аз ви отделих като нечисти.
“‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
26 И бъдете свети на Мене; защото Аз, Иеова съм свет, и ви отделих от племената за да бъдете Мои.
Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
27 Също мъж или жена, която запитва зли духове, или е врач, непременно да се умъртви; с камъни да ги убият; кръвта им да бъде върху тях.
“‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”

< Левит 20 >