< Изход 12 >

1 Тогава Господ говори на Моисея и Аарона в Египетската земя, казвайки:
Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti,
2 Тоя месец ще ви бъде началният месец; ще ви бъде първият месец на годината.
“Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka.
3 Говорете на цялото Израилево общество, като им кажете да си вземат, на десетия ден от тоя месец, всеки по едно агне, според бащините си домове, по едно агне за всеки дом.
Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi.
4 Но ако домашните са малцина, за агнето, тогава домакинът и най-ближният до къщата му съсед нека вземат, според числото на човеците в тях; смятайте за агнето според онова, което всеки може да изяде.
Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere.
5 Агнето или ярето ви нека бъде без недостатък, едногодишно мъжко; от овците или от козите да го вземете.
Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi.
6 И да го пазите до четиринадесетия ден от същия месец; тогава цялото общество на израилтяните, събрани в домовете си да го заколят привечер.
Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo.
7 После нека вземат от кръвта и турят на двата стълба и на горния праг на вратата на къщите, гдето ще го ядат.
Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo.
8 През същата нощ нека ядат месото, печено на огън; с безквасен хляб и с горчиви треви да го ядат.
Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa.
9 Да не ядат от него сурово нито варено във вода, но изпечено на огън, с главата му, краката му и дреболиите му.
Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba.
10 И да не оставите нищо от него до утринта; ако остане нещо до утринта, изгорете го в огън.
Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe.
11 И така да го ядете; препасани през кръста си, с обущата на нозете си и тоягите в ръцете си; и да го ядете набързо, понеже е време на Господното минаване.
Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.
12 Защото в оная нощ ще мина през Египетската земя, и ще поразя всяко първородно в Египетската земя, и човек и животно; и ще извърша съдби против всичките египетски богове; Аз съм Иеова.
“Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova.
13 И кръвта на къщите, гдето сте, ще ви служи за белег, така че, като видя кръвта, ще ви отмина, и когато поразя Египетската земя, няма да нападна върху вас, погубителна язва.
Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.
14 Оня ден ще ви бъде за спомен, и ще го пазите като празник на Господа във всичките си поколения; вечен закон ще ви бъде, да го празнувате.
“Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova.
15 Седем дни да ядете безквасен хляб; още на първия ден ще дигнете кваса от къщите си; защото, който яде квасно от първия ден до седмия ден, оня човек ще се изтреби от Израиля.
Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli.
16 На първия ден ще имате свет събор, и на седмия ден свет събор; никаква работа да не се върши в тях, освен около онова, което е нужно за ядене на всеки; само това може да вършите.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.
17 Да пазите, прочее, празника на безквасните, защото в същия тоя ден изведох войнствата ви из Египетската земя; заради което ще ви бъде вечен закон да пазите тоя ден във всичките си поколения.
“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya.
18 От вечерта на четиринадесетия ден от първия месец до вечерта на двадесет и първия ден от месеца ще ядете безквасни хлябове.
Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo.
19 Седем дена да се не намира квас в къщите ви; защото който яде квасно, оня човек ще се изтреби отсред обществото на израилтяните, бил той пришелец или туземец.
Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa.
20 Нищо квасно да не ядете; във всичките си жилища безквасни хлябове да ядете.
Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”
21 Тогава на четиринадесетия ден от месеца, Моисей повика всичките Израилеви старейшини и рече им: Идете та си вземете по едно агне според челядите си и заколете пасхата.
Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska.
22 После да вземете китка от исоп и да я потопите в кръвта, която ще приемете в леген, и с кръвта, що е в легена, да ударите по горния праг и двата стълба на къщната врата; и никой от вас да не излиза от къщната си врата до утринта.
Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa.
23 Защото Господ ще мине, за да порази египтяните, и когато види кръвта на горния праг и на двата стълба на вратата, Господ ще отмини вратата, и не ще остави погубителят да влезе в къщите ви, за да ви порази.
Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.
24 И ще пазите това като вечен закон за себе си и за синовете си.
“Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu.
25 Когато влезете в земята, която Господ ще ви даде според обещанието си, ще пазите тая служба.
Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu.
26 И когато чадата ви попитат: Какво искате да кажете с тая служба?
Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’
27 Ще отговорите: Това е жертва в спомен на минаването на Господа, който отмина къщите на израилтяните в Египет, когато поразяваше египтяните, а избави нашите къщи. Тогава людете се наведоха и се поклониха.
Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’” Kenaka anthu anawerama napembedza.
28 И израилтяните отидоха та сториха, според както Господ заповяда на Моисея и Аарона; така направиха.
Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
29 И по среднощ Господ порази всяко първородно в Египетската земя, от първородния на Фараона, който седеше на престола си, до първородния на пленника, който бе в затвора, както и всяко първородно от добитък.
Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo.
30 И Фараон стана през нощта, той и всичките му слуги, и всичките египтяни; и нададе се голям писък в Египет, защото нямаше къща без мъртвец.
Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.
31 И повика Моисея и Аарона още през нощта та рече: Станете и вие и израилтяните, излезте, изсред людете ми и идете, послужете на Иеова, както рекохте;
Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha.
32 подкарайте и овците си и стадата си, както рекохте, та идете; па благословете и мене.
Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”
33 Тоже египтяните принуждаваха людете, за да ги отпратят по-скоро от земята си, защото си рекоха: Ние всички измираме.
Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.”
34 И людете дигнаха тестото си преди да вкисне, като носеха на рамена нощвите обвити в дрехите си.
Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu.
35 А израилтяните бяха постъпили както Моисей беше казал, като бяха поискали от египтяните сребърни и златни вещи и дрехи;
Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala.
36 и Господ беше дал на людете да придобият благоволението на египтяните, тъй щото те бяха им дали колкото искаха. Така те обраха египтяните.
Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.
37 Прочее, израилтяните се дигнаха от Рамесий за Сокхот, на брой около шестстотин хиляди мъже пешаци, освен челядите.
Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana.
38 Още с тях излезе и голямо разноплеменно множество, както и твърде много добитък - овци и говеда.
Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe.
39 А от тестото, което носеха из Египет, изпекоха безквасни пити; защото не беше вкиснало, понеже ги изпъдиха из Египет, и те не можаха да се бавят, нито да си приготвят ястие.
Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.
40 А времето, което израилтяните прекараха като пришълци в Египет, беше четиристотин и тридесет години.
Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430.
41 И в края на четиристотин и тридесетте години, дори в същия ден, всички войнства Господни излязоха из Египетската земя.
Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto.
42 Това е нощ, която е за особено опазване за Господа, загдето ги изведе из Египетската земя; това е оная нощ, която всичките израилтяни, във всичките си поколения, трябва особено да пазят за Господа.
Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.
43 И Господ рече на Моисея и Аарона: Ето законът за пасхата: никой чужденец да не яде от нея;
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa: “Mlendo asadye Paska.
44 обаче всеки роб купен с пари да яде от нея тогава, когато се обреже.
Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe.
45 Никой пришелец или наемник да не яде от нея.
Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.
46 В една къща да се изяде; от месото да не изнасяте вън от къщи и кост от нея да не строшите.
“Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse.
47 Цялото общество израилтяни ще я пазят.
Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.
48 И ако би някой чужденец да живее като пришелец между тебе и да иска да пази пасхата Господу, нека се обрежат всичките му мъжки, и тогава нека да пристъпи да я пази; той ще бъде като туземец. Но никой необрязан не бива да яде от нея.
“Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska.
49 Един закон ще има за туземеца и за чужденеца, който е пришелец между вас.
Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.
50 И всичките израилтяни сториха според както Господ заповяда на Моисея и Аарона; така направиха.
“Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
51 И тъй, в същия оня ден Господ изведе израилтяните из Египетската земя според устроените им войнства.
Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”

< Изход 12 >