< Изход 11 >
1 (А Господ беше казал на Моисея: Още една язва ще нанеса на Фараона и на Египет, подир което ще ви пусне от тука; когато ви пусне, съвсем ще ви изпъди от тука.
Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani.
2 Кажи, прочее, в ушите на людете, и нека поиска всеки мъж от съседа си, и всяка жена от съседката си, сребърни и златни вещи.
Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.”
3 И Господ беше дал на людете да продибият благоволението на египтяните. При това, Моисей беше станал твърде велик човек в Египетската земя пред Фараоновите слуги и пред людете).
Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.
4 Моисей каза на Фараона: Така казва Господ: Около средата на една нощ Аз ще мина през Египет;
Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto.
5 и всички първороден в Египетската земя ще умре, от първородните на Фараона, който седи на престола си, до първородния на слугинята, която е зад воденицата, и до всяко първородно от добитъка.
Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto.
6 И по цялата Египетска земя ще се нададе голям писък, какъвто никога не е имало, нито ще има вече такъв.
Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso.
7 А против израилтяните, против човек или животно, нито куче няма да поклати езика си, за да познаете, че Господ прави разлика между египтяните и израилтяните.
Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli.
8 И всички тия твои слуги ще дойдат при мене и ще ми припаднат и рекат: Излез ти с всичките люде, които те следват. И подир това ще изляза. И Моисей излезе от Фараоновото присъствие с голям гняв.
Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.
9 (А Господ беше казал на Моисея: Фараон няма да ви послуша, за да се умножат Моите чудеса в Египетската земя.
Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.”
10 И Моисей и Аарон бяха извършили всички тия чудеса пред Фараона, и той не беше пуснал израилтяните из земята си).
Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.