< Matiwos Dooshishiyo 18 >

1 Manoor b́ danifuwots Iyesusok t'int, «Dari mengstotse jamoniyere bogo kone?» ett bo aati.
Pa nthawi imeneyo ophunzira anabwera kwa Yesu ndipo anamufunsa kuti, “Wamkulu woposa onse ndani mu ufumu wakumwamba?”
2 Iyesuswere na'í marmat' iko s'eegdek't bo taalots ned'ib́k'r,
Iye anayitana kamwana kakangʼono ndi kukayimiritsa pakati pawo.
3 Hank'owo bíeti, «Arikone itsh ti etiri, woneyar nana'í marmat'uwotskok'o woto it k'azal b́ jamon dari mangstots kindratste.
Ndipo Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati simusintha ndi kukhala ngati tiana tatingʼono, simudzalowa konse mu ufumu wakumwamba.
4 Na'i marmat'ankok'o b́ tooko dashan detsetwo dari mengstotse eene b́wotiti.
Chifukwa chake, aliyense amene adzichepetsa yekha ngati kamwana aka, ameneyo ndiye wamkulu koposa onse mu ufumu wakumwamba.
5 Hank'o wotts na'o t shúútsosha err dek'etwo taan dek'etwe.» bíet.
Ndipo aliyense amene alandira kamwana kakangʼono ngati aka mu dzina langa, alandira Ine.
6 «Konwor wotowa asho taan amaniru muk'nana'anotsitse iko b́ dariyoniyere mangts dí'́i shútso b́ bimbats tifde'er ayide dashan gop'ts aatsi k'arotse juweyar k'ot'eeb́wtsink'eree bísh k'aniyank'e.»
“Koma ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana awa, amene akhulupirira Ine, kuti achimwe, kukanakhala bwino kuti iye amangiriridwe chimwala chachikulu mʼkhosi mwake ndi kumizidwa pansi pa nyanja.
7 Manats dabt Iyesus hank'o bíet, «Ash ashuwotssh t'ug wotiru ashuwots jangatse tuutson indowe datsusha! wottso b́ wotiyalor t'ug wotit keewwots bowowo ooreratse, ernmó t'ugo wotitwo b́weetwok'o k'alitumansh indowe bísha!
Tsoka dziko lapansi chifukwa cha zinthu zimene ziyenera kubwera, koma tsoka kwa munthu amene abweretsa zotere!
8 Mansh eshe n kisho wee n tufo morro n finitwok'o neen b́daritkawotiyal k'ut'de' juk'rowe! git kisho wee git tufo deshfetsr dúre dúri tawots njuwewoniree kish k'ut'o wee duro wotarr dúre dúri kashomaats kindo neesh k'anefe. (aiōnios g166)
Ngati dzanja lako kapena phazi lako likuchimwitsa, lidule ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kulowa mʼmoyo wosatha wolumala kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri kapena mapazi awiri ndi kukaponyedwa ku moto wosatha. (aiōnios g166)
9 Ni ááwonúwere morro nfinitwok'o neen b́dariyal kishde okaan juk'rowe! git ááwo deshfetsŕ gahanem taw gop'ots njuwewoniyere ááw iketso wotaarr kasho maants kindo neesh k'anefe. (Geenna g1067)
Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Ndi bwino kwa iwe kuti ukalowe ku moyo wosatha ndi diso limodzi kuposa ndi kukhala ndi maso awiri ndi kukaponyedwa ku moto wa gehena.” (Geenna g1067)
10 Darotse fa'a bo melakiwots jam aawo darotse fa'o tnih shiitso bos'iilirwotse, k'ac'in nana'anotsitse dab́ ikonor it gac'erawok'o it tooko korde'ere. [
“Onetsetsani kuti musanyoze mmodzi wa anawa. Pakuti ndikuwuzani kuti angelo awo kumwamba amakhala pamaso pa Atate anga akumwamba nthawi zonse.”
11 Ash na'onúwor b́waa t'aftso kashiyoshe.»]
(Mwana wa Munthu anabwera kudzapulumutsa chimene chinatayika).
12 Ando aaniy Iyesus hank'o bíeti, «Aab eeg arefa itsha? Bal mereer detsts ash iko boyitse iko b́k'aleyal balosh ik shapwotsi guri abaatse k'ayk'rar t'aftsman geyo amaalkeya?
“Kodi mukuganiza bwanji? Ngati munthu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi nʼkusowa, kodi sasiya 99 zija mʼmapiri ndi kupita kukafuna imodzi yosocherayo?
13 Ariko itsh keewirwe, bín b́daatsor fa'a balosh ik shapwotsiyere t'aft daatsets ikmansh b́gene'úwiti.
Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti akayipeza amasangalala kwambiri chifukwa cha nkhosa imodziyo kuposa nkhosa 99 zimene sizinasochere.
14 Mank'o darotse fa'o itnih nana'a k'ac'nanotsitse ikonwore b́t'fitwok'o geyeratsee.
Chimodzimodzinso Atate anu akumwamba safuna kuti mmodzi wa anawa atayike.
15 «Nieshu neen b́dadiyal neenat bín ikn wotde neesh b́t'afitso keewwe, n keewo b́ shishetka wotiyal aani nik woshdek'etuune,
“Ngati mʼbale wako akuchimwira, pita kamuwuze cholakwa chake pa awiri. Ngati akumvera, wamubweza mʼbale wakoyo.
16 N keewo shisho b́k'azalmo wee git wee keez ashuwots gawts gawo b́s'eenetwok'o neenton wee iko wee git asho de'er biyok amee.
Koma ngati sakumvera, katenge wina mmodzi kapena ena awiri, ‘kuti nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.’
17 Boon k'ewatse bíetalmó Ik' moosh keewwe, Ik'i moonowere k'ewatse bí'etetka wotiyalowere Ik' danawok'o wee morretsok'o taawk'rowe.
Ngati iye akana kuwamvera iwo, kaneneni ku mpingo; ndipo ngati sakamvera ngakhale mpingo, muchite naye monga mukanachitira ndi wakunja kapena wolandira msonkho.
18 «Arikoniyere itsh tietiri, datsatse it tiptetwoniye darotse tipekee b́wotiti, datsatse it biitsetwo daaratse bishke b́wotiti.
“Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti chilichonse chimene muchimanga pa dziko lapansi, chidzamangidwanso kumwamba, ndipo chilichonse chimene muchimasula pa dziko chidzamasulidwanso kumwamba.
19 Andoor aaniy itsh keewirwe, ititse gitetswots datsatse eegonor k'onosh ikwotar Ik'o bok'oniyal darotse fa'o t nih itsh s'eentsitwe.
“Komanso ndikukuwuzani inu kuti ngati awiri a inu pa dziko lapansi avomerezana kanthu kalikonse kamene mukapempha, Atate anga akumwamba adzakuchitirani.
20 Gito wee keezo wotar tshúútson bokakwet beyokoke taa bo dagotse daatsetwe.»
Pakuti pamene awiri kapena atatu asonkhana pamodzi mʼdzina langa, Ine ndili nawo pomwepo.”
21 Manoor P'et'ros Iyesus maants t'int́, «Doonzono! tíeshuu taan b́dadiyal ambtsoto bísh oorowe erta? Shawatoto b́borfetsoneya?» ett bíaati.
Kenaka Petro anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Ambuye, kodi mʼbale wanga akandichimwira ndimukhululukire kokwanira kangati? Mpaka kasanu nʼkawiri?”
22 Iyesuswere bísh hank'o bíet, «Shawatoti sheba bako shawatot mec'ra eraatse neesha,
Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuza iwe kuti osati kasanu nʼkawiri, koma ka 70 kuchulukitsa ndi kasanu nʼkawiri.
23 Mansh daritsi mengstu guutswotsnton tanoosh geyiru nugúsoniye bíari,
“Nʼchifukwa chake, ufumu wakumwamba ukufanana ndi mfumu imene inafuna kuti antchito ake abweze ngongole.
24 Nugusonwere taano dek't b́tuutsok'on ay miliyeniyon meklityo bíatse fa'a guuts iko detseyat b́weyi.
Atangoyamba kulandira, anamubweretsa munthu kwa iye amene anakongola ndalama 10,000.
25 Guuts man bíatse fa'a k'awntso dasho b́mááwtsotse bíwere b́ máátsunowere b́nan'úwotsnat b́ detsts jamonowere kemde'er bíats fa'a k'awntso b́dashetwok'o b́ doonz bíazazi.
Popeza sakanatha kubweza, bwanayo analamula kuti iye, mkazi wake, ana ake ndi zonse anali nazo zigulitsidwe kuti zibweze ngongoleyo.
26 Guutsonmo b́ doonz shirots tuk'maldek't ‹Doonzono! oona neea! muk'i taash s'iilde'e, b́ jamonor neesh dashetwe!› ett bín b́ k'oni.
“Wantchitoyo anagwada pamaso pake namupempha iye kuti, ‘Lezereni mtima ndipo ndidzabweza zonse.’
27 B́ doonzwere bísh maac'o k'ewat bín faksh b́k'ri, bíatsi k'awntsonoweree k'azb́k'ri.
Bwana wakeyo anamuchitira chifundo, namukhululukira ngongoleyo ndipo anamulola apite.
28 «Ernmó guutsman manoke kesht amoke b́befere bal dinariyo gusho bíatse b́detstso b́ tooho daatsdek't b́ bimbo gúk'dek't, ‹Neesh t gushits gizo taash daye!› bí et.
“Koma wantchito uja atatuluka, anakumana ndi wantchito mnzake amene anakongola kwa iye madinari 100. Anamugwira, nayamba kumukanyanga pa khosi, namuwumiriza nati, ‘Bwezere zimene unakongola kwa ine!’
29 Guuts b́ toohmanwere b́tufishirotse diht́ ‹Oona neesha! taash muk'i k'amowee, neesh dashetwe!› ett b́ k'oni.
“Wantchito mnzakeyo anagwada namupempha iye kuti, ‘Lezere mtima ine, ndipo ndidzakubwezera.’
30 Ashmanmó k'aze bíet. Iki dabnwor detsdek't amt́ b́ k'awntso b́dashfetsosh tipi moots tipi b́k'ri.
“Koma iye anakana. Mʼmalo mwake, anachoka nakamumangitsa kufikira atabweza ngongoleyo.
31 Bínk'ó wotts guuts guutswots man bobek'tsok'on ayidek't shiyanbowts, amtinwere wotts jamo bodoonzsh keewbok'ri.
Pamene antchito ena anaona zomwe zinachitikazo, anamva chisoni kwambiri ndipo anapita nakawuza bwana wawo zonse zimene zinachitika.
32 doononwere guutsman s'eegidek't bísh hank'o bíet, ‹Nee gond guutsono! taan nk'onree jam k'awntsman neesh k'azre,
“Pamenepo bwanayo anayitana wantchitoyo nati, ‘Iwe wantchito woyipa mtima, ndinakukhululukira ngongole yako yonse chifukwa unandipempha.
33 Eshe, taa niatsi k'awntso neesh k'aztk'rok'o, nee ntooh wotts guutsosh k'azo neesh geyiyank'oshna b́teshi?›
Kodi iwe sukanamuchitira chifundo wantchito mnzako monga momwe ine ndinakuchitira iwe?’
34 Mansh doonzo fayat bíatsi k'awnts jamo b́dashfetsosh tipi maa naashosh beshidek't b́ ími.
Ndi mkwiyo, bwana wakeyo anamupereka kwa oyangʼanira ndende kuti amuzuze mpaka atabweza zonse zimene anakongola.
35 «Eshe itwere ik ikon it eshuwi itnibotse kishde neesh orowe eto itk'azal darotse fa'o tnihwor mank'o it aats k'alitwe.»
“Umu ndi mmene Atate anga akumwamba adzachitira ndi aliyense wa inu ngati simukhululukira mʼbale wanu ndi mtima wonse.”

< Matiwos Dooshishiyo 18 >