< Mui 18 >

1 A: ibalaha: me da Ma: melei soge amo sema ifa bagade lelebe sogebi esalu. Eso gia: beba: le, e da ea abula diasu logo holei gadenene filasa: i esalu. Amalalu, Hina Gode da ema doaga: i.
Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
2 A: ibalaha: me da ba: legadole, dunu udiana gadenene lelebe ba: i. Ba: loba, e da hedolowane ili yosia: musa: asi, amola ilima begudui.
Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
3 E amane sia: i, “Hina! Dilia da na hahawane ba: i galea, mae baligili masa.
“Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
4 Na da hano gaguli misa: ne sia: mu. Amoga dilia emo dodofelalu, amo ifa ea ougiga helefima.
Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
5 Na da dilia hawa: hamosu dunu defele esala. Dilia gasa bu lama: ne, na da dilima ha: i manu imunu da defeala: ?” Ilia da bu adole i, “Defea! Dia sia: i defele hamoma!”
Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
6 Amaiba: le, A:ibalaha: me da hedolowane ea abula diasua golili sa: i. E da Selama amane sia: i, “Hedolo! Falaua 22 lida amo lale, bibiagole amola gobele agi ga: gi hamoma.”
Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
7 Amalalu, A:ibalaha: me da ea lai gebo gilisisu amoga hehenane, bulamagau mano gasono ida: iwane lale, ea hawa: hamosu dunuma i. Amo da hedolowane hahamoi.
Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
8 Amalalu, e da dodo maga: me haei, dodo maga: me amola bulamagau mano gobei, amo gaguli misini, sofe misi dunu ili amo moma: ne ligisi. Ilia da ha: i nanoba, e da ifa ea ougiga ilima gadenene lelu.
Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
9 Ilia da ema amane adole ba: i, “Dia uda Sela da habila: ?” A: ibalaha: me da bu adole i, “E da abula diasu ganodini esala.”
Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
10 Amalalu, Hina Gode da amane sia: i, “Na da waha oubi sesegeyale uduli, dafawane dima misunu. Dia uda Sela da dunu mano lalelegemu.” Sela da abula diasu holei amo Hina Gode Ea baligiga galu amoga sia: lalabolalu.
Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
11 A: ibalaha: me amola Sela da da: i hamoi dagoiba: le, Sela da mano lamu ode defei amo baligi dagoi ba: i.
Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
12 Amaiba: le, Sela da ea dogo ganodini ousu. Ea asigi dawa: su ganodini, e amane dawa: i, “Na da: i da wadela: lesi dagoi amola nagoa da da: i hamoi. Na da habodane amo hahawane hou ba: ma: bela: ?”
Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
13 Amalalu, Hina Gode da A: ibalaha: mema amane sia: i, “Sela da abuliba: le oune amane sia: i, ‘Na da da: i hamoiba: le, habodane mano lalelegema: bela: ?’
Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
14 Gasa bagade liligi hamomu da Godema hamedebela: ? Na da oubi sesegeyale uduli, eso ilegei defele na dima olelei, bu misunu. Amola Sela da dunu mano lalelegemu.”
Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
15 Sela da beda: iba: le, ogogoi. E amane sia: i, “Na da hame oui.” Be Hina Gode da amane sia: i, “Be di da oui dagoi.”
Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
16 Sofe misi dunu da masusa: wa: legadoloba, ilia da ba: le gaidi Sodame ba: i. Ilia da logoga ahoanoba, A:ibalaha: me da ili sigi asi.
Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
17 Amalalu, Hina Gode da Hima amane sia: i, “Na da waha hou hamomu amo A: ibalaha: mema wamolegema: bela: ?
Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
18 A: ibalaha: me ea fi da fi bagade amola gasa bagade hamomu. Ea houba: le, osobo bagade fifi asi gala huluane da hahawane dogolegele ilegesu ba: mu.
Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
19 Bai Na da e ilegei dagoi. E da ea mano noga: le olelema: ne amola ea fi dunu da hou moloidafa amola dafawanedafa amo olelema: ne, Na da e ilegei. Amai galea, Na da Na hahawane ilegele sia: i liligi huluane ema imunu.”
Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
20 Amalalu, Hina Gode da amane sia: i, “Na da Sodame amola Goumola ela fi wadela: idafa hou amo nabi.
Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
21 Amaiba: le, Na da ilia hou ba: ma: ne amo da nabi liligi defele ganabela: ? Amo Na da ba: la masunu. Hame galea Na da dawa: mu.”
choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
22 Sofe misi dunu da sinidigili, Sodame moilaiga doaga: musa: asi. Be A: ibalaha: me da mae fisili Hina Gode Ea midadi lelu.
Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
23 Amalalu, e da Hina Godema misini, amane sia: i, “Di da dafawane gilisili ida: iwane dunu amola wadela: i hamosu dunu ili fane legema: bela: ?
Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
24 Amabela: ? Dunu ida: iwane 50 agoane amo moilai bai bagade ganodini esalabala? Amai galea, Di da amo dunu ilia hou dawa: beba: le, amo moilai bai bagade fadegale fasima: bela: ?
Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
25 Na da agoane dawa: Di da dunu ida: iwane amola wadela: i hamosu dunu gilisili hou afadafa fawane hamomu da hamedei gala. Amo hou da Dima hame gala. Osobo bagade fifi asi gala ilima Fofada: su Dunudafa, E da hou moloidafa fawane hamoma: bela: ? Na agoane dawa: E da moloidafa hou fawane hamomu.”
Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
26 Hina Gode da bu amane sia: i, “Na da Sodame moilai bai bagade ganodini dunu ida: iwane gala 50 agoane ba: sea, Na da ilia hou dawa: beba: le, Sodame huluane hame gugunufinisimu.”
Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
27 Amalalu, A:ibalaha: me da bu sia: i, “Na da osobo amola nasubu, amo fawane. Be na da mae beda: iwane, Hina Godema sia: i dagoiba: le, na da bu sia: mu.
Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
28 Di da Sodame moilai bai bagade ganodini, dunu ida: iwane 45 fawane ba: sea, Di da 50 defei amo ganodini wadela: i hamosu dunu biyale fawane ba: sea, moilai wadela: ma: bela: ?” E bu adole i, “Na da dunu ida: iwane 45 fawane ba: sea, moilai hame gugunufinisimu.”
bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
29 A: ibalaha: me da eno amane sia: i, “Be 40 fawane ba: sea, adi hamoma: bela: ?” E amane sia: i, “Amo 40 ilia hou dawa: beba: le, Na da moilai bai bagade hame wadela: mu.”
Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
30 Amalalu, A:ibalaha: me da amane sia: i, “Hina Gode! Nama mae ougima, be na da Dima bu sia: mu. Dunu 30 fawane ida: iwane esalea adi hamoma: bela: ?” E bu adole i, “Na da 30 ba: sea, moilai hame gugunufinisimu.”
Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
31 A: ibalaha: me da amane sia: i, “Defea! Na da wali mae beda: iwane Hina Gode Ema sia: i dagoi. Be 20 fawane ba: sea?” E bu adole i, “Moloi dunu 20 ba: sea, Na da hame wadela: mu.”
Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
32 A: ibalaha: me da amane sia: i, “Hina Gode! Nama mae ougima, be na da afadafa fawane eno Dima sia: mu. Dunu 10 ida: iwane fawane ba: sea, adi hamoma: bela: ?” Hina Gode da bu adole i, “Dunu 10 ilia hou ida: iwane ba: sea, Na da amo moilai hame gugunufinisimu.”
Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
33 Hina Gode amola A: ibalaha: me, ela gilisili sia: dasu da dagoloba, Hina Gode da fisili asi amola A: ibalaha: me da hi diasuga buhagi.
Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.

< Mui 18 >