< Mui 11 >

1 Amo esoga, osobo bagade dunu fi da sia: hisu hisu hame galu. Ilia huluane da sia: afadafa fawane galu.
Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
2 Dunu fi huluane da eso maba gusudili ahoanu, umi soge ea dio amo Ba: bilone ba: i. Amo ganodini ilia fi dialu.
Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
3 Ilia da amane gilisili sia: dasu, “Defea! Ninia osobo ganumugini, gobele, igi agoai ‘baligi’ hamone, diasu gagumu.’ Amola amo liligi ‘baligi’ ilia da edele amoga madelagisu.
Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
4 Amalalu, ilia da amane sia: i, “Ninia moilai bai bagade hamomu. Amo ganodini ninia da diasu sedade gagagula heda: i amo da Hebene amoga doaga: mu liligi gagumu. Ninia dio bagade hamomu. Ninia fi da osobo bagade soge huluane amoga afafasa: besa: le agoane hamomu.
Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
5 Be Hina Gode da moilai bai bagade amola diasu gado gagagula heda: i amo dunu da hamonanu, amo ba: la gudu sa: i.
Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
6 E amane sia: i, “Ilia da fi afadafa amola sia: afadafa gala. Amo ilia da muni hamobeba: le, hobea huluane ilia hanaiga hamomusa: dawa: mu.
Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
7 Defea! Ninia da gudu sa: ili, ilia sia: ededenagia: mu. Amasea, ilia sia: hisu hisu amoga sia: sea, nabimu gogolemu.”
Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
8 Amaiba: le, Gode da dunu fi afagogole, osobo bagade dedeboma: ne asunasi. Ilia amo diasu gagagula heda: i gagumu yolesi dagoi.
Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
9 Amaiba: le, amo diasu ilia da Ba: ibele dio asuli. Bai amoga Hina Gode da ilia sia: hisu hisu hamoi, amola ili afagogole, osobo bagade soge huluane fima: ne asunasi.
Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
10 Sieme ea mano da hagudu dedei. Hano bagade da yolesili, ode aduna asili, Sieme da ode 100 esalu, ea dunu mano amo Aba: sa: de da lalelegei.
Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
11 Amalalu, Sieme da ode 500 eno esalu. Amoga e da manolali eno lalelelegei.
Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
12 Aba: sa: de da ode 35 esalu, dunu mano amo ea dio Sila amo lai.
Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
13 Fa: no e da ode 403 eno esalu amola amoga manolali eno lalelelegei.
Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
14 Sila da ode 30 esalu, dunu mano ea dio Ibe amo lai.
Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
15 Fa: no e da ode 430 eno esalu. Amoga e da manolali eno lalelelegei.
Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
16 Ibe da ode 34 esalu, dunu mano amo ea dio Bilege lai.
Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
17 Fa: no Ibe da ode 430 eno esalu. Amo odega e da egefelali eno lalelelegei amola uda manolali eno lalelelegei.
Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
18 Bilege da ode 30 esalu, dunu mano ea dio amo Liu lai.
Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
19 Bilege da Liu lai amalu ode 209 eno esalu. Amoga e da egefelali eno lalelelegei amola uda manolali eno lalelelegei.
Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
20 Liu da ode 32 esalu, dunu mano ea dio amo Silage lai.
Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
21 Liu da Silage lai amalu fa: no e da ode 207 esalu. Amoga e da dunu manolali eno lalelelegei amola uda manolali eno lalelelegei.
Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
22 Silage da ode 30 esalu, dunu mano ea dio amo Na: iho lai.
Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
23 Silage da Na: iho lai amalu fa: no e da ode 200 eno esalu. Amoga e da dunu manolali eno lalelelegei amola uda manolali eno lalelelegei.
Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
24 Na: iho da ode 29 esalu, dunu mano ea dio amo Dila lai.
Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
25 E da Dila lai amalu fa: no ode 119 esalu. Amoga, e da dunu manolali eno lalelelegei amola uda manolali eno lalelelegei.
Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 Dila da ode 70 esalu, dunu mano udiana lai amo A: ibala: me, Na: iho amola Ha: ila: ne.
Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
27 Dila egaga fi da agoane. Ea mano da A: ibala: me, Na: iho amola Halane. Halane ea mano da Lode.
Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
28 Halane da ea moilaidafa (moilai dio da E, Ba: bilone soge ganodini dialu) amoga bogoi. E bogoloba, ea ada Dila da esalebe ba: i.
Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
29 A: ibala: me da Selai lai amola Na: iho da Miliga lai. Miliga ea ada da Halane. Halane idiwi eno da Isiga.
Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
30 Selai da aligime esalu. Mano lamu hamedei ba: i.
Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 Dila da egefe A: ibala: me, eaowa Lode (Halane ea mano) amola ea nawi Selai (A: ibala: me idua) amo oule asili, Ba: bilone soge moilai amo E yolesili, Ga: ina: ne sogega doaga: musa: asi. Be ilia da Halane sogega doaga: le, fi galu.
Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 Dila da amogawi bogoi. Ea esalu ode idi da 205 ba: i.
Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

< Mui 11 >