< varumi 1 >

1 uPaulo unsung'ua ghwa Yesu Kilisite, juno akemhelilue kuva nsung'ua, na kubaghulua vwimila ilivangili lya Nguluve.
Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
2 ili lwe livangili lino akalifingile pakali kukilila avavili vaake mu malembe amimike.
umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
3 sa nswambe, juno akaholilue kuhuma mu kikolo kya Davidi mu lwa m'bili.
Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
4 umwene akapulisivue kwa mwana ghwa Nguluve ku nguu ja Mhepo uMwimike ku vusyukue vwa vafue, uYesu Kilisite Mutwa ghwitu.
Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
5 kukilila umwene twupile uvumosi nu vusung'ua kwa kwitikila ulwitiko mu luhala lwoni, vwimila ilitavua lyake.
ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
6 mu luhala ulu, najumue kanga mukemhelilue kuva va Yesu Kilisite.
Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
7 ikalata iji ja kuvoni vano vali ku Rumi, vaghanike va Nguluve, vano vakemhelilue kuva vimike. uvumosi nu lutengano fivisaghe numuekuhuma kwa Nguluve Nhaata ghwitu nu Mutwa Yesu Kilisite.
Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
8 muvwandilo, nikumuhongesia uNguluve ghwango mwa Yesu Kilisite vwimila jinu mweni. ulwakuva ulwitiko lwinu ludalikivue mu iisi jooni.
Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
9 ulwakuva uNguluve nsaidi ghwango, juno nikumwuvila mu numbula jango mu livangili lya Nswambe, ndavule nikukala na kukuvakemhela.
Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
10 jaatu nikuvasumila mu nyifunyo sango kuuti, ku sila jojoni nikave uvusililo kuva lughinio ku lughano lwa Nguluve kukwisa kulyumue.
Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
11 lwa kuva nonoghelua kukuvagha, neke nikave kukuvapela ifipelua ifya munumbula, nikave kukuvakangasia.
Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
12 ni lolelela kukuvakangasia inumbula ku sila ija lwitiko kwa muunhu ghweni. ijinu ni jango.
ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
13 lino vanyalukolo nanilonda muleka kukagula kuuti, ke kinga nihuvila kukwisa kulyumue neke kuhanga lino nisighilie. nilonda ndiki neke kuva ni mheke kulyumue ndavule lulivua kuvapanji.
Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
14 nidajivua na vaYunani navaghesi kange, averefu na vajaasu.
Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
15 lino ku lubale lwango, une nili tayale kupulisia ilivangili kulyumue na kuvano vali ku Rumi.
Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
16 ulwakuva nanikulivonela soni ilivangili, ulwakuva se ngufu sa Nguluve uvuvangi ku vano vikumwitika, kwa muYahudi taasi neke kwa muYunani kange.
Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
17 ulwakuva ikyang'hani ja Nguluve jivonike kuhuma ulwitiko nu lwitiko, ndavule jilembilue,” inya lwitiko ikukala mu lwitiko.
Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
18 ulwakuva ing'alasi ja Nguluve jivonike kuhuma kukyanya kulutila uvuhosi vwoni vwa vaanhu, vano kusila ja vuhosi vikujifisa ikyang'haani.
Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
19 ulu lwe lukuva, sooni sino ndepoonu sikagulika kwa Nguluve sesa vuvalafu kuveene. ulwakuva uNguluve avamamnyisie.
Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
20 ulwakuva imbombo sake sino nasivoneka vunono sili pavuvalafu kuhuma muvutengulilo vwa iisi. sivoneka kukilila ifinu finofivumbilue. imbombo isi se vuwesia vwake vwa kusila na kusila nu vutengulilo vwa vunguluve. amahumile ghake avaanhu ava vasila vutavulilua (aïdios g126)
Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios g126)
21 . ulu lwe lyakuva nave valyakagwile isa Nguluve, vakampaala umwene ndavule uNguluve nambe navamuhongisie. pe pano valyale vajaasu mu musaghe ghave na moojo ghave agha vujaasu ghakaponesivue ing'iisi.
Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
22 vajikemelagha vanyaluhala neke vakava vajaasu.
Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
23 valyavwandwile uvwimike vwa Nguluve juno nsila vunangifu vwa kihwanikisio kya muunhu juno ali nuvunangifu, nagha fijuni, nagha fidimua ifinya maghulu ghane, na fifing'onyo fino fikwafuala.
Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24 pe uNguluve akavaleka vasivingilile inogheluo indamafu sa moojo ghave, ku mavili ghave kusukunalua vavuo ku vavuo.
Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
25 vope vano vandwile ilweli ja Nguluve kuuva vudesi, na vano vakifunyilagha na kufivombela ifidimua na kukumuleka juno afivumbile juno ighinilua ifighono ifisila na kusila. Amina. (aiōn g165)
Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
26 mu ulu uNguluve alyavelekile vavingilile inoghelua saave isa soni, ulwakuva avadala vaave vakandwile kutumila amavili ghave ndavule lulyamunoghile uNguluve. na
Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
27 vavaghosi vakaleka kutumila amavili ku vadala vaave looli vavuo ku vavuo. ava valyale ve vaghosi vano vavombagha na vaghosi vajanave sino nasinoghile, valyupile uluhombo luno lunoghile ku vusofi vwave.
Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
28 ulwakuva navakighanile kuuva nu Nguluve mu luhala lwavo, akavaleka valuvingililaghe uluhala lu vanave luno nalunoghile, vavombe sino nasinoghile.
Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
29 vamemilue ni nuvuhosi, uvunoghelua nu vuvivi. vamemilue nu vwifu, ilibaatu, uvusyangi nu vufumbue vuvivi,
Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
30 avene kange vajova fivi, vahomeleng'ani kange vanya kun'kalalia unguluve. avanya vulugu, imbedo, na vanya lughinio. aveene vanya kusagha imbivi, navikuvitika avapafi vaave.
osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
31 aveene vasila vukagusi; navikwitikika, vasila lughano kange vasila ikisa.
alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
32 vikwelevua uvutavike vwa Nguluve, lwa kuuti avaanhu vano vivomba mu isio vanoghile kufua. neke nakwekuti vano vivomba aghuo vene, looli avene vikwiting'ana na vala vano vivomba aghuo.
Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.

< varumi 1 >