< Ulusetulilo 17 >
1 Jumo ughwa vanyamola lekela lubale alyale ni fitasa fiila lekela lubale akisa na pikum'bula, “Isa, nikukusona uluhighilo lwa mbwafu u m'baha juno ikukala mumalenga minga,
Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja amene anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri anadza nati kwa ine, “Bwera ndikuonetse chilango cha mkazi wadama wotchuka uja amene akukhala pambali pa madzi ambiri.
2 juno ava tua va iisi vavombile naghwoope isa vuvwafu na muluhuje lwa muvuvwafu vwa mweene vano vikukala mu iisi vaghalile.”
Mafumu a dziko lapansi amachita naye chigololo ndipo okhala pa dziko lapansi analedzera ndi vinyo wa zigololo zake.”
3 Umunyamola akanoola mu mepo mpaaka kulukuve, nilya m'bwene u mwana mama ikalile pakyanya pa ng'anu indangali juno amemile amatavua agha nyamaligho. Ing'anu jilyale na maatu lekela lubale namapembe kijigho.
Kenaka mngeloyo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku chipululu. Kumeneko ndinaona mkazi atakhala pa chirombo chofiira chokutidwa ndi mayina a chipongwe ndipo chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi.
4 Umwana mama alyafwasivue amenda gha sambalau ni ndangali apambilue ni sahabu amavue gha lutogo, ni lulu. Alyakolelile muluvoko lwa mweene ulwa sahabukino kimemile ifiinu fino fikalasia nhu vunyali vwa vuvwafu vwa mweene.
Mkaziyo anavala zovala za pepo ndi zofiira nadzikongoletsa ndi golide, miyala yapamwamba ndi ngale. Ananyamula chikho chagolide mʼdzanja lake, chodzaza ndi zinthu zonyansa ndi fungo loyipa la zigololo zake.
5 Pavweni vwa mwene lilembilue ilitavua lya vusyefu: “BABELI UM'BAHa, GHWE NG'INA GHWA VAMALAYA NI FINU FINO FIKARASI MU IISI.”
Pa mphumi pake panalembedwa dzina lodabwitsa: BABULONI WAMKULU MAYI WA AKAZI ADAMA NDI WAZOYIPITSA ZA DZIKO LAPANSI.
6 Nikalula kuuti umwanamama uju akaghalile idanda ja vitiki ni danda javano valyafwile vwimila u Yesu. Unsiki ghuno nilyam'bwene, nikadeghile kyongo.
Ndinaona kuti mkaziyo anali ataledzera ndi magazi a oyera mtima, magazi a amene anachitira umboni Yesu. Nditamuona mkaziyo ndinadabwa kwambiri.
7 Looli umunyamola akam'bula, “Kiki ghudegha? Nikukwolelela uvu mama kye kiinu kiki nu ng'aanu ikuntokla (ing'aanu ijio jinyamaatu lekela lubale namapembe ghala kijigho).
Kenaka mngelo uja anati kwa ine, “Bwanji ukudabwa? Ndikufotokozera chinsinsi cha mkaziyu ndi chinsinsi cha chirombo chimene wakwerapochi chokhala ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi.
8 Ing'anu jino ukajivwene pwejikale, nakwejili kange lino, looli jiling'anisie kuhuma mu lina linlo lisila vusililo. Kange jighendelelaghe kuvomba uvunangi. Kuvala vano vikukala mu iisi, vala vano amatavua gha vanave naghalembilue mukitabu ikya vwuumi kuhuma livikua ulwalo lwa iisi - vilidegha pano vikujivona ing'anu jino pwiili, kuuti na pe jiili lino, looli alipipi pikwisa. (Abyssos )
Chirombo chimene wachionachi chinalipo kale koma tsopano kulibe ndipo chidzatuluka ku chidzenje chakuya ndi kupita kukawonongedwa. Anthu okhala pa dziko lapansi amene mayina awo sanalembedwe mʼbuku lamoyo kuyambira pa kulengedwa kwa dziko lapansi adzadabwa pamene adzaona chirombocho, chifukwa chinalipo kale, tsopano kulibe, komabe chidzabwera. (Abyssos )
9 Ing'emelo iiji vwimila vwa haala sino sivungike. Amaatu lekela lubale ni fidunda lekela lubale pano umwana mama alikalile lakyanya pa fyeene.
“Zimenezi zikufunika kuganizira mwanzeru. Mitu isanu ndi iwiriyo ndi mapiri asanu ndi awiri pomwe mkazi uja amakhalirapo. Yomweyonso ndi mafumu asanu ndi awiri.
10 Joope kange ve vaatua lekela lubale. Ava tua vahano vaghwile, jumo kwale, jumo akyale na isile; unsiki ghuno ikwisa, ikukala unsiki n'debe.
Mafumu asanu anagwa, imodzi ilipo ndipo ina sinabwere; koma pamene idzafika, idzayenera kukhala kwa kanthawi kochepa.
11 Ing'anu jino kwejilyale, looli lino napwiili, kange ghwe ntua ghwa lekela kwooni, looli ghwe jumo na vutua lekela lubale, kange iluta kuvunangi.
Chirombo chomwe chinalipo kale ndipo tsopano kulibe ndiyo mfumu yachisanu ndi chitatu. Iyo ndi ya mʼgulu la asanu ndi awiriwo ndipo ikupita kukawonongedwa.
12 Amapembe ghala kijigho ghano akaghavweene ve vatua kijigho vano navupiile uvutua, looli vikwupila uvutavulilua hwene vatua ku kivalilo kimo palikimo ni ng'anu.
“Nyanga khumi unaziona zija ndi mafumu khumi amene sanapatsidwe ulamuliro, koma adzapatsidwa ulamuliro pamodzi ndi chirombo kwa ora limodzi.
13 Ava vali nu n'kolo ghumo pevikupela ingufu sa vanave nuvutavulilua vwa ng'aanu jiila.
Mafumuwo ali ndi cholinga chimodzi ndipo adzapereka mphamvu ndi ulamuliro wawo kwa chirombocho.
14 Vilua ililugu avene nu mwana ng'olo. Looli umwanang'olo ikuvalefia ulwakuva Mutwa ghwa vatua Ntua ghwa vatua - mwamwene tukemelilue, tusalulivue, vapesie.”
Iwo adzachita nkhondo ndi Mwana Wankhosa, koma Mwana Wankhosayo adzawagonjetsa chifukwa Iye ndi Mbuye wa ambuye ndi Mfumu ya mafumu, ndipo amene adzakhala ndi Iye ndi oyitanidwa ake, osankhidwa ndi otsatira ake okhulupirika.”
15 Umunyamola akam'bula, “Amalenga ghala ghano akaghavwene, pala pano akikalileumalaya jula ve vaanhu, fupugha, fisina ni njovele.
Kenaka mngeloyo anati kwa ine, “Madzi amene unawaona pamene mkazi wadamayo anakhalapo ndiwo anthu ochuluka, mitundu ndi ziyankhulo.
16 Amapembe ghala kijigho ghano aka ghavwene - ni ng'aanu jila vikusulagha u malaya juula. Voope vikum'bikagha mwene kange vufula, vilisagha um'biili ghwa mwene, pe vinyanyilila nu mwooto.
Nyanga khumi ndi chirombo unazionazo zidzadya mkazi wadamayo. Zidzamufwifwitsa ndi kumusiya wamaliseche; zidzadya nyama yake ndi kumutentha ndi moto.
17 Ulwakuva u Nguluve avikile mu mojo gha vanave kum'pinda uluhuvilo lwa mwene ku lwiting'ano ulwakujipela ing'ano ingufu sivanave pikun'ema m'paka amasio gha Nguluve ghiiliva ghikwilana.
Pakuti Mulungu wayika ichi mʼmitima mwawo kuti akwaniritse cholinga chake povomerezana kupereka mphamvu zawo zolamulira kwa chirombo, kufikira Mawu a Mulungu atakwaniritsidwa.
18 Umwanamama jula juno alyam'bwene lye likaja lila ilivaha lino litemile uvutua vwa iisi.”
Mkazi unamuonayo ndi mzinda waukulu umene ulamulira mafumu a dziko lapansi.”