< Luuka 21 >

1 uYesu akalila akavagha avakinhaata vamofu valyale vivika amatekelo ghave muvutile
Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
2 akamwagha unfwile jumonga nkotofu ivika isenti sake ivili. pe
Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
3 akati,”kyang'haani nikuvavula unfwile uju unkotofu ivikile indalama nyinga kukila avange voooni.
Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
4 ava vooni vahumisie ilitekelo ili kuhuma mufinga fino valinafyo. neke unfwile uju mu vukotofu vwake ahumisie indalamasooni sino avele naso vwimila uvwumi vwake”
Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
5 ye avange valyale vijova isa nyumba inyimike ja kufunyila, ndavule jilyavikilue na mavue amanono na matekelo, akati,
Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
6 mu mhola isa mbombo sino mukusagha, ifighono fikwisa fino nakwekuliva nilivue limo lino lililekua nkyanya ja livue ilinge lino nalilighua.
“Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
7 pe vakamposia vakati, Mbulanisi isi sooni silihumila lighi? kwe kiliku kino kiliva kye kivalilo kuuti agha ghalipipi kuhumila?
Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
8 uYesu akamwamula, “muvisaghe maaso kuuti namungasyanguaghe. ulwakuva vingi vikwisa ku litavua lyango viti,”une nene, nu nsiki ghulipipi. namungavavingililaghe.
Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
9 mungapulike ivuluguvulugu namungoghwopaghe, ulwakuva isi sooni sinoghile sihumile taasi. neke uvusililo navulihimila ng'hani ng'hani”
Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
10 pe pano akavavula,” iisi jilikwima na kutovana ni jinge, uvutwa ku vutwa uvunge.
Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
11 kuliva ni finsenyena ifikome, injala ni nhamu isa kwambukila siliva papinga. kwe kuliva ni finu fya kwoghofia ni fivalilo fya kwoghofia kuhuma kukyanya.
Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
12 neke isio sooni ye sikyale kuhumila, tiko avaanhu vilikuvakoola umue na kukuvapumusia. vilikuvawala kukuahigha mu nyumba isa kufunyila, na kukuvadindila mu ndinde. kange mulitwalua ku vatwa na ku vanya vutavulilua kuuti muhighue ulwakuva umue muli vavvulanisivua vango.
“Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
13 neke kulyumue aghuo ghuva ghwe nsiki ghwa kwoleka ulwitiko lwinu.
Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
14 pe lino mwamulaghe mu moojo ghinu ku ling'ania avimilisi viinu ye lukyale.
Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
15 ulwakuva nikuvapela amasio agha vukoola vuno avalugu viinu voni vikunuagha kusigha na kukujikana.
Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
16 neke mulikanwa na vapafi vinu, avanyalukolo vinu, avapipi vinu na vamanyani vinu, kange vilikuvabuda vamonga mu lyumue,
Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
17 vilikunkalalila umuunu ghweni ku litavua lyango.
Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
18 neke nakwelule nambe ulunyele lumo lwa matu ghinu luno lulisova.
Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
19 ku lugudo mukusisosia inumbula sinu.
Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
20 kyale muvoona ilikaaja lya Yelusalemu lisyungutilue navalua lilugu pe mukagulaghe kuuti unsiki ughwa kutipulua ghuli pipi.
“Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
21 apuo vano vali ku Yudea vakimbililaghe ku fidunda, na vala vano vali pakate pa mpulo vavukaghe, kange namungavalekaghe vano vali kufikaaja kukwingila.
Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
22 ulwakuva ifi fye fighono fya kuhombekesia, neke kuuti ghooni ghano ghalembilue ghiise kuvombeka.
Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
23 iga ku vala vano vali nuvukunue na vala vano vikwong'esia ku fighono ifio! ulwakuva kuliiva nulupumuko lukome mu iisi, ni ng'halasi ku vaaanhu ava.
Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
24 avaanhu avange vilibudua ni bambaavange vilitwalua ku vukamiku iisi isinge, ni Yelusalemu jilikanyua na vaanhu va iisi kuhanga unsiki ghwa vaanhu va iisi pano ghuuva ghufikile.
Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
25 fili vineka ifivalilo ku lijuva, umwesi ni nhondue, neke pa iisi apa inyanja siliva na mavingo amavaha amanya mughindi, uluo lulipelela avaanhu ava fisina fyonikuuva nulupumuko nu ludwesi.
“Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
26 isi sooni siliva sikwisa mu iisi, avaanhu ghulifua umwoojovwimila kukwoghopa kyongo. vilisaghagha kuuti lukwisa ulutalamu ulukome, ulwakuva ifinu ifya kukyanya filisukanisivua,
Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
27 pepano vilikumwagha umwana ghwa muunhu ikwisa kuhuma mumafunde ku ngufu nu vwimike uvuvaha.
Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
28 neke isio sooni silava sitengula kuhumila, mwimaghe, inulagha amatu ghinu, ulwakuva uvupoki vwinu vuvelelile pavupipi.
Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
29 uYesu akavavula ku kihwanikisio akati, lolagha umpiki ghwa tini na mapiki ghoni.
Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
30 pano muvona amapiki ghatengwile kulemba, mukujilolela jumue na kukagula kuuti amasiki gha lufuke ghalipipi.
Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
31 vule vule pano muvona agha ghihumila umue kagulagha kuuti, uvutwa vwa Nguluve vulipipi.
Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
32 kyang'haani nikuvavula, ikisina iki nakilikila, kuhanga isi sooni sihumile.
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
33 uvulanga ni iisi silikila, neke amasio ghango looli naghilikila.
Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
34 neke mujilolelelaghe jumue, neke kuuti, amoojo ghinu naghangalemuaghe nu vuhojofu, uvughasi, nuvukaming'anilua vwa iisi iji. ulwakuva ikighono ikio kilavisila mu lwa ng'enyemukila hwene lutegho.
“Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
35 ulwakuva jiiva kwa muunhu ghweni juno ikukala pa maaso gha iisi jooni.
Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
36 lino muvisaghe maaso unsiki ghwoni, mun'sumaghe uNguluve kuuti muva lukangafu lwa kukwilana kukughaseghuka agha ghoni ghano kyale ghihumila, na kukwima pavulongolo pa mwana ghwa Muunhu”.
Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
37 mu fighono ifio pamwisi, uYesu alyale ivulanisia avaanhu mu luviika ulwa nyumba inyimike ja kufunyila. pakilo akalutagha kughona ku kidunda ikya Miseituni.
Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
38 neke jaatu avaanhu voni vakasisimukagha lulwakilo na kuluta mu nyumba inyimike ja kufunyila kuuti vampulikisie.
Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.

< Luuka 21 >