< Vaebrania 12 >

1 Pa uluo, ulwakuva litusyungutile ilifunde ilikome ilya valesi, pe tutaghe kila kiini kino kikutulema ni nyivi sino sikutwuvila kihugu. Tu tove uluvilo ku saburi mu masindano ghano ghavikilue pavulongolo palyusue.
Tsono popeza ifenso tazunguliridwa ndi gulu lalikulu la mboni, tiyeni titaye chilichonse chimene chimatitchinga, makamaka tchimo limene limatikola mosavuta, ndipo tithamange ndi khama mpikisano umene tayambawu.
2 Tusung'e amaso ghitu kwa Yesu, juno n'tengulisi nughwa ku ling'ania ulwitiko lwitu, juno vwimila lwa lukelo lwitu jino jika vikilue pavulongolo jikanoghile pa kikovekano, ibeda isooni ja mwene, akikala pasi pa paluvoko lwa ndiyo lwa kitengo kya vutua ikya Nguluve.
Tiyeni tiyangʼanitsitse Yesu, amene ndi woyamba ndi wotsiriza wa chikhulupiriro chathu. Chifukwa cha chimwemwe chimene chimamudikira anapirira zowawa zapamtanda. Iye ananyoza manyazi a imfa yotere ndipo tsopano akukhala ku dzanja lamanja la mpando waufumu wa Mulungu.
3 Msaghe kuuti umwene umwene juno alya gudile amasio amasio gha kukalasia kuhuma mu nyivi, vwimila umwene jujuo neke kuti mulakatala nambe kusilika amoojo ghinu.
Muzilingalira za Iye amene anapirira udani waukulu chotere wochokera kwa anthu ochimwa, kuti musafowoke ndi kutaya mtima.
4 Namupumuike nambe kupumuka kutovana ni nyivi kighelelo kya kusilua idanda.
Polimbana ndi uchimo, simunafike mpaka pokhetsa magazi.
5 Kange musyamilue kula ku kangasivua inumbula kuno kukuvolelela ndavule avaanha ava dimi: “Mwanango, Nulaghatolagha kuvuhugu amagomokelo gha Mutwa, nambe nula denyekagha inumbula pano ghunosevua nu mwene.”
Kodi mwayiwala mawu olimbitsa mtima aja, amene Mulungu anayankhula kwa inu ngati ana ake? Mawuwo ndi awa: “Mwana wanga, usapeputse kulanga kwa Ambuye ndipo usataye mtima pamene akukudzudzula.
6 Ulwakuva u Mutwa ikun'gomokela ghweghue juno amughanile, na pikumigha umwana ghwenibjuno ikumwupila.
Chifukwa Ambuye amadzudzula amene amawakonda ndipo amalanga aliyense amene amamulandira.”
7 Ghulilala ingelo kukugomokela. uNguluve ihangajika numue ndavule ikuvavombela avaana, ulwakuva ghwe mwana juliku juno u nhaataghake nangawesie kugomoka?
Pamene mukupirira masautso monga chilango, Mulungu achitira inu monga ana ake. Kodi ndi mwana wotani amene abambo ake samulanga?
8 Looli nave na kwekule kugomoka, kuno usue tweni tuhanga, looli umue ni haram namuli vaanha va mwene.
Ngati inu simulangidwa, komatu aliyense amalangidwa, ndiye kuti sindinu ana enieni koma amʼchigololo.
9 Kukila ghoni, tulyale nava nata vitu mu iisi vakutugomokela, kange tukavoghopagha. Vuli najitunoghile namba kukila kumwitika Nhaata wa kimhepo na na kukukala?
Komanso, tonsefe tinali ndi abambo athu otibala amene amatilanga ndipo timawapatsa ulemu. Nanga kodi sitidzagonjera Atate a mizimu yathu kuti tikhale ndi moyo?
10 Ku vwakyang'haani va naata vitu valyatuhighile ku maka madebe ndavule jikavonike sawa kuvanave, looli u Ngiluve ikutuhigha kuluvumbulilo lwitu neke tuhange uvwimika vwa mwene.
Abambo athu ankatilanga kwa kanthawi kochepa monga amaonera kufunika kwake, koma Mulungu amatilanga kuti tipindule, kuti tikhale oyera mtima.
11 Nakwelule uluhighilo luno luhovosia ku nsiki ughuo. Luva nuvuvafi. pauluo, pambele jikoma imeke ja lutengano lwa kuvabuda vala vano vano vavulanisivue nagho.
Palibe chilango chimene chimaoneka kuti ndi chabwino pa nthawiyo, komatu chowawa. Koma pambuyo pake, chimabweretsa chipatso chachilungamo ndi mtendere kwa iwo amene aleredwa mwa njira imeneyi.
12 Pa uluo mwinila amavoko ghinu ghano ghilegena na pivoma amafundo ghinu ghano mavotevote kuva manyangufu kange;
Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka.
13 mugholosie amakilo gha sajo sinu, neke kuuti ghweghwoni juno mulemale nailitemua muvuvusovi looli asosevue.
Muziyenda mʼnjira zowongoka, kuti iwo amene akukutsatirani ngakhale ndi olumala ndi ofowoka asapunthwe ndi kugwa koma adzilimbikitsidwa.
14 Mulondaghe ulutengano na vaanhu vooni, kange nu vwimike kisilanuvuo nakwale juno ilikum'bona umutwa.
Yesetsani kukhala pa mtendere ndi anthu onse ndi kukhala oyera mtima, pakuti popanda chiyero palibe ndi mmodzi yemwe adzaona Ambuye.
15 Muve valoleli neke kuti napweavisaghe ughwa kudagua kutali nuvumofu vwa Nguluve, nakuuti liilisa ilisikina lya lusungulino lilemba nakuhambusia imumuko na pikuvahambusia vinga.
Yangʼanitsitsani kuti wina aliyense asachiphonye chisomo cha Mulungu ndiponso kuti pasaphuke muzu wamkwiyo umene udzabweretsa mavuto ndi kudetsa ambiri.
16 Mulolaghe kuti nakwevule uvuvwafu nambe muunhu junono na mtauwa ndavule u Esau, juno vwimila vwa lulio lwa kamo alyaghusisie uvwakyang'haani vwa mwene uvwa kuholua.
Yangʼanitsitsani kuti pasakhale wina wachigololo. Kapena wosapembedza ngati Esau, amene chifukwa cha chakudya cha kamodzi kokha anagulitsa ukulu wake.
17 Ulwakuva mukagula kuti pambele, alya kanilue, ulwakuva nalyapelilue inafasi ja kulata palikimo nu naata ghwa mwene, nambe kuuti alyalondile kyongo ku masosi.
Monga inu mukudziwa, pambuyo pake pamene anafuna kuti adalitsidwe anakanidwa. Sanapezenso mpata woti asinthe maganizo, ngakhale anafuna madalitsowo ndi misozi.
18 Ulwakuva namukisile mu kidunda kino ndapunu ghugusa, Kidunda kno kivika umwoto, ng'isi, pidenya inumbula ni dhoruba.
Inu simunafike ku phiri limene mungathe kulikhudza, loyaka moto wa mdima bii, la mphepo yamkuntho;
19 Namulisile namukisile kulisio lya lukelema, nambe kumasio ghano ghahumilanile ni lisio ghanogha kavombole kuuti vanI'll vipilika valekaghe pikufunya ilisio lyolyoni kujovua kuvanave.
limene pali kulira kwa lipenga, ndiponso kumveka kwa mawu. Anthu amene amamva mawuwo anapempha kuti asawayankhulenso mawu ena.
20 Ulwakuva navakaghwesisie kuguda kila kinokilamulilue: “Nave nakikikanu kino kigusa ikidunda, lasima kitovue na mavue.”
Iwo anachita mantha ndi lamulo lija lakuti, “Ngakhale nyama ikangokhudza phirilo, iphedwe ndi miyala.”
21 Lwakuti kukila ghano aghaghile uMusa akajova, Noghuipe kyongo kivalilo kya kuhilila”.
Maonekedwenso a Mose anali woopsa kwambiri, ngakhale Mose yemwe anati, “Ine ndinachita mantha ndi kunjenjemera.”
22 Pauluo, musilebmukidunda kya Sayuni na mulikaja lya Nguluve juno mwumi, Yerusalemu ja kukyanya, na vanyamola filundo kumi vano vishelekela.
Koma inu mwafika ku Phiri la Ziyoni, ku mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wakumwamba. Mwafika mu msonkhano wa angelo osangalala osawerengeka.
23 Mwisile mulipugha lya vaholua va kwasia vooni vano vasajilivue kukyanya, kwa Nguluve umighi ghwa vooni nku mhepo sa vitike vano vakwilanile.
Mwafika mu mpingo wa ana oyamba kubadwa, amene mayina awo analembedwa kumwamba. Inu mwafika kwa Mulungu, woweruza anthu onse, ndiponso kwa mizimu ya anthu olungama ndi osandutsidwa kukhala angwiro.
24 Mwisile gha Yesu unsambanisi wa agano imia, dakudanda jino vamisile jino jijova amanono kyongo kukila idanda ja Haili.
Kwa Yesu mʼkhalapakati wa pangano latsopano, ndiponso mwafika ku magazi owazidwa amene amayankhula mawu abwino kuposa magazi a Abele.
25 Lolagha alan'kolagha jumo juno ijova. Ulwakuva hwene navakapungile vano van'kolile jumo juno akavavungile, sa kyang'haani na tulipunga isi nave tusyetuka kuvutali kuhuma kwajula juno ikutuvunga kuhuma kukyanya.
Chenjerani kuti musakane kumvera amene akuyankhula nanu. Anthu amene anakana kumvera iye amene anawachenjeza uja pa dziko lapansi pano, sanapulumuke ku chilango ayi, nanga tsono ife tidzapulumuka bwanji ngati tikufulatira wotichenjeza wochokera kumwamba?
26 Ku nsiki ughuo ilisio lya mwene likasukanisie i iisi. Looli lino atufingile kujova, “Bado kakinga kange nanisukania ji iisi jene, looli navuvulanga kange.”
Pa nthawiyo mawu ake anagwedeza dziko lapansi, koma tsopano Iye walonjeza kuti, “Kamodzi kenanso ndidzagwedeza osati dziko lapansi lokha komanso thambo.”
27 Amasio agha, “Lwakamo kange,”jisona kubusivua ku finu fila fino fisukanisivua, ifi fye, finu fila fino fipelilue, neke kuti ifinu fila fino nafisukanisivua visighale.
Mawu akuti, “Kamodzi kenanso,” akuonetsa kuchotsedwa kwa zimene zitha kugwedezeka, zonse zolengedwa, kotero kuti zimene sizingatheke kugwedezeka zitsale.
28 Pa uluo twupile uvutwa vuno navusukanisivua, tukele mu mu hali ja kumfunya u Nguluve kukwitika palikimo na kuvumofu mu kicho,
Popeza tikulandira ufumu umene sungagwedezeke, tiyeni tikhale oyamika ndi kupembedza Mulungu movomerezeka ndi mwaulemu ndi mantha.
29 Ulwakuva uNguluvevghwitu ghwe mwoto ghuno ghulia.
Pakuti Mulungu wathu ndi moto wonyeketsa.

< Vaebrania 12 >