< Waefeso 4 >

1 Pauluo, heene n'kunguavwimila u Mutwa, nikuvasuma mughendelelaghe ndavule ng'emelo jino u Nguluve alya vakemelile.
Ine monga wamʼndende chifukwa chotumikira Ambuye, ndikukulimbikitsani kuti mukhale moyo woyenera mayitanidwe amene munalandira.
2 Mukulaghe nu vwoghofi mu vuhugu nulugudo. Kupindilanila n'kate mulughano.
Mukhale odzichepetsa kwathunthu ndi ofatsa; mukhale oleza mtima, ololerana wina ndi mnzake mwachikondi.
3 Mulolelanilaghe ni ngufu kulolela uvumo vwa Mhepo muvukungua uvwa lutengano.
Muyesetse kusunga umodzi wa Mzimu; umodzi umene umatimangirira pamodzi mu mtendere.
4 Kuli m'bili ghumo ku Mhepo jumo, ndavule mulyale mukemelilue muvwa kyang'haani uvwa lughulilo lumo ulwa ulwa ng'emelelo jinu.
Pali thupi limodzi ndiponso Mzimu mmodzi, monganso pali chiyembekezo chimodzi chimene anakuyitanirani.
5 Kange kwale u Ntua jumo, ulwofugho lumo,
Pali Ambuye mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi;
6 nu Nguluve jumo ghwe Nhaata ghwa vooni. Umwene alipakyanya pa sooni iisi, na kusooni isi na mun'kate mu ku sooni.
Mulungu mmodzi ndi Atate a onse, ndipo ali mwa onse.
7 Kwa muunhu ghweni mulyusue apelilue ikipelua kuling'ana nikighelelo ikya kipelua ikya Kilisite.
Koma aliyense wa ife wapatsidwa chisomo molingana ndi muyeso wa mphatso ya Khristu.
8 Ndavule amalembe ghijova: “Pano alyatoghile ku kyanya kyongo, alyalongwisie ava galulu muvukami. Akahumia ifipelua ku vaanhu.”
Nʼchifukwa chake akunena kuti, “Iye atakwera kumwamba, anatenga chigulu cha a mʼndende ndipo anapereka mphatso kwa anthu.”
9 Kwekuuti kiki iisi, “Alyatoghile,” neke looli alikile kange pasi pa iisi?
Kodi mawu akuti, “Iye anakwera” akutanthauza chiyani, ngati Iyeyo sanatsikire kunsi kwa dziko lapansi?
10 Umwene juno alikile ghwe mwene julajula juno kange alyatoghile kuvutali kukyanya kuvulanga vwooni. Alyavombile n'diki ulwakuuti uvuvaha vwa mweene vuvisaghe mu finu fyooni.
Iye amene anatsika ndi yemweyo anakwera koposa mʼmayiko a kumwamba onse, ndi cholinga choti zinthu zonse zikhale zodzaza ndi Iye.
11 U Kilisite alya humisie ifipelua ndavule ifi: avasung'ua, avaviili, avainjilisiti, avadiimi nava vulanisi.
Iye ndiye amene anapereka mphatso kwa ena kuti akhale atumwi ndi ena aneneri, ena alaliki, ndi ena abusa ndi aphunzitsi.
12 Alyavombile vulevule kukuvatanga avitiki vwimila vwa mbombo ija vuvombi, vwimila vwa kuvuvujenga um'biili ghwa Kilisite.
Ntchito yawo ndi kukonza oyera mtima kuti agwire ntchito ya utumiki kuti thupi la Khristu lilimbikitsidwe.
13 Ivomba n'diki kuhanga usue tweeni tufikile uvumo vwa lwitiko nhuvu mang'anyi vwa mwana ghwa Nguluve. Ivomba vulevule mpaaka tukangale ndavule vaala vano valyafikile ikyimo kino kikwiline ikya Kilisite.
Izi zidzatifikitsa tonse ku umodzi wachikhulupiriro, kumudziwa Mwana wa Mulungu, kukhwima msinkhu ndi kufika pa muyeso wangwiro weniweni wopezeka mwa Khristu.
14 Ulu kwekuuti tulekaghe kuuva heene vaana, natungapululusivwaghe kuno nakula. Ulwakuuti tuleke pitolua ni mhepo sisino sivisaghe sa mbulanisio, nigiilabsa vaanhu mumanjughulu gha vudesi vuno vusoveleng'ine.
Motero sitidzakhalanso makanda, ogwedezekagwedezeka ndi mafunde, otengekatengeka ndi mphepo iliyonse ya chiphunzitso ndi kuchenjera kwa anthu achinyengo amene amasocheretsa anthu ndi kuchenjera kwawo.
15 Palwene uluo tujovaghe uvwakyang'haani mulughano na kukula kyoongo mu siila sooni n'kate mwa mweene juno ghwe muutu, u Kilisite.
Mʼmalo mwake, poyankhula choonadi mwachikondi, tidzakula mu zinthu zonse ndi kukhala thupi la Khristu, amene ndi Mutu, omwe ndi mpingo.
16 U Kilisite adumining'inie, palikimo u m'biili ghwooni ughwa vitiki. Ghulunginisivue palikimo nifipelua fyooni ulwakuuti um'biili ghwoni ghukule napikujenga gwene mulughano.
Mwa Iye thupi lonse lalumikizidwa ndi kugwirana pamodzi ndi mitsempha yothandizira. Likukula ndi kudzilimbitsa lokha mwachikondi, pomwe chiwalo chilichonse chikugwira ntchito yake.
17 Pauluo, nijova iili, nikuvasuma mwa Mutwa: Namulaghendagha kange heene vaanhu vapanji fino vighenda muvugalusi vwa luhala luvanave.
Tsono ine ndikukuwuzani izi, ndipo ndikunenetsa mwa Ambuye, kuti musayendenso monga amachitira anthu a mitundu ina potsata maganizo awo opanda pake.
18 Vakapikilue ni ng'iisi mumasaghe gha vanave. Vadaghilue vwumi vwa Nguluve muvuyasu vuno vulin'kate muvanave ulwakuva vwimila uvwumi vwa moojo ghavanave.
Maganizo awo ndi odetsedwa, ndi osiyanitsidwa ndi moyo wa Mulungu chifukwa cha umbuli umene uli mwa iwo chifukwa cha kuwuma mtima kwawo.
19 Navikupulika isooni. Vitavwile veene kuvunyali mu mbombo inyali, mulwa vugheji vwooni.
Popeza sazindikiranso kanthu kalikonse, adzipereka okha kuti akhumbe zonyansa, kuti achite mtundu uliwonse wa zoyipa ndi zilakolako zosatha.
20 Looli, nafyelulivuo ndavule mulumanyile vwimila u Kilisite.
Koma inu simunadziwe Khristu mʼnjira yotere.
21 Nakuva kuuti mupulike umwene. Nakuva kuuti mukale mumanyila mwa mweene, ndavule uvwa kyang'ani vulivuo vwimila u Yesu.
Zoonadi munamva za Iye ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye molingana ndi choonadi chimene chili mwa Yesu.
22 Luvanoghile mufunyaghe sooni sino silutana nulughendo lwiinu ulwa pakali, uvumuunhu uvwa pakali, uvumuunhu vwa pakali vuno vuvola vwimila vwa vunoghelua vwa vudesi.
Inu munaphunzitsidwa molingana ndi moyo wanu wakale, kuchotsa umunthu wakale, umene ukupitirira kuwonongeka ndi zilakolako zachinyengo;
23 Mufulaghe uvumuunhu uvwa pakali ulwakuuti muvombeke vupia munumbula sa luhala lwinu.
kuti mukonzedwe mwatsopano mʼmitima mwanu;
24 Muvombaghe vulevule ulwa kuuti mukagule kufwala uvumuunhu uvupia, vuno vulutana nu nguluve vupelilue muvwakyang'aani nu vwimike vwa kyang'ani.
ndi kuti muvale umunthu watsopano, wolengedwa kuti ufanane ndi Mulungu mu chilungamo chenicheni ndi chiyero.
25 Pa uluo, vikagha kutali nuvudesi. “Jovagha uvwa kyang'aani umuunhu ghweni nhu m'bading'ani ghwa mwene,” ulwakuva tulivahangilanisi umuunhu ghweni kwa junge.
Chifukwa chake, aliyense wa inu aleke kunama ndipo ayankhule zoona kwa mʼbale wake, pakuti ife tonse ndife ziwalo za thupi limodzi.
26 Muvisaghe ni ng'alasi, looli na mungavombaghe inyivi,” Ilijuva nalingasemaghe mujighe ni ng'alasi siinu.
Kwiyani koma musachimwe. Dzuwa lisalowe mukanali chikwiyire.
27 Namungam'pelaghe uvwelefu u setano.
Musamupatse mpata Satana.
28 Ghweni juno ihija anoghile kuhija kange. Pa uluo anoghile avombaghe imbombo. Avombaghe imbombo inyaluvumbulilo na mavoko gha mwene, ulwakuuti akagule pikun'tanga umuunhu juno aghilue.
Iye amene wakhala akuba asabenso, koma agwire ntchito ndi kuchita kenakake kaphindu ndi manja ake, kuti akhale ndi kenakake kogawana ndi amene akusowa.
29 Injovele imbiivi najingajighaghe mumulomo ghwinu. Pa uluo amasio ghanoghile pihuma mumalomo ghiinu ghano ghanoghile kusino silondeka, kukuvapela uluvumbulilo vala vano vipulikisia.
Mʼkamwa mwanu musatuluke mawu aliwonse onyansa, koma okhawo amene ndi othandiza kulimbikitsa ena molingana ndi zosowa zawo, kuti athandize amene akawamve.
30 Mulampelelagha kusukunala u Mhepo Mwimike ghwa Nguluve kwa mwene kuuti mukanyilue umuhuri vwila vwa kighono ikya vupoki
Ndipo musamvetse chisoni Mzimu Woyera wa Mulungu amene mwasindikizidwa naye chizindikiro cha tsiku la kuwomboledwa.
31 Lunoghile pikuluvika patali uvuvafi vwooni, ing'alasi, ilyoojo, amabatu, namaligho, palikimo nuvuhosi vuno vuli pa pinga.
Chotsani kuzondana, ukali ndi kupsa mtima, chiwawa ndi kuyankhula zachipongwe, pamodzi ndi choyipa chilichonse.
32 Muvisaghe nulusungu. Musaghilanilaghe jumue kwa jumue, ndavule u Nguluve mwa Kilisite avasaghile umue.
Mukomerane mtima ndi kuchitirana chifundo wina ndi mnzake. Khululukiranani wina ndi mnzake, monga momwe Mulungu anakukhululukirani mwa Khristu.

< Waefeso 4 >