< Pǝnd-nǝsiⱨǝtlǝr 23 >
1 Katta ǝrbab bilǝn ⱨǝmdastihan bolsang, Aldingdiki kim ikǝnlikini obdan oylan.
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 Ixtiying yaman bolsa, Gelingƣa piqaⱪ tǝnglǝp turƣandǝk ɵzüngni tart.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Uning nazunemǝtlirini tama ⱪilma, Ular adǝm aldaydiƣan tamaⱪlardur.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Bay bolimǝn dǝp ɵzüngni upratma; Ɵzüngning zeⱨningni bu ixⱪa ⱪaratma.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 [Bayliⱪlarƣa] kɵz tikixing bilǝnla, ular yoⱪ bolidu; Pul-mal dǝrwǝⱪǝ ɵzigǝ ⱪanat yasap, Huddi bürküttǝk asmanƣa uqup ketǝr.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Aq kɵzning nenini yemǝ, Uning esil nazunemǝtlirini tama ⱪilma;
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 Qünki uning kɵngli ⱪandaⱪ bolƣandǝk, ɵzimu xundaⱪ. U aƣzida: — Ⱪeni, alsila, iqsilǝ! — desimu, Biraⱪ kɵnglidǝ seni oyliƣini yoⱪ.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Yegǝn bir yutum taamnimu ⱪusuwetisǝn, Uningƣa ⱪilƣan qirayliⱪ sɵzliringmu bikarƣa kǝtkǝn bolidu.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Əhmǝⱪⱪǝ yol kɵrsitip salma, Qünki u ǝⱪil sɵzliringni kɵzgǝ ilmas.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Ⱪǝdimdǝ bekitkǝn yǝrning pasil taxlirini yɵtkimǝ, Yetimlarning etizliriƣimu ayaƣ basma;
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 Qünki ularning Ⱨǝmjǝmǝt-Ⱪutⱪuzƣuqisi intayin küqlüktur; U Ɵzi ular üqün üstüngdin dǝwa ⱪilar.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Nǝsiⱨǝtkǝ kɵngül ⱪoy, Ilim-bilimlǝrgǝ ⱪulaⱪ sal.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Balangƣa tǝrbiyǝ berixtin erinmǝ; Əgǝr tayaⱪ bilǝn ursang, u ɵlüp kǝtmǝydu;
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Sǝn uni tayaⱪ bilǝn ursang, Bǝlkim uni tǝⱨtisaradin ⱪutⱪuziwalisǝn. (Sheol )
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
15 I oƣlum, dana bolsang, Mening ⱪǝlbim ⱪanqǝ hux bolar idi!
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 Aƣzingda orunluⱪ sɵzlǝr bolsa, iq-iqimdin xadlinimǝn.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Gunaⱨ sadir ⱪilƣuqilarƣa rǝxk ⱪilma, Ⱨǝrdaim Pǝrwǝrdigardin ǝyminixtǝ turƣin;
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Xundaⱪ ⱪilƣiningda jǝzmǝn kɵridiƣan yahxi kününg bolidu, Arzu-ümiding bikarƣa kǝtmǝs.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 I oƣlum, sɵzümgǝ ⱪulaⱪ selip dana bol, Ⱪǝlbingni [Hudaning] yoliƣa baxliƣin.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Mǝyhorlarƣa arilaxma, Nǝpsi yaman gɵxhorlar bilǝn bardi-kǝldi ⱪilma;
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Qünki ⱨaraⱪkǝx bilǝn nǝpsi yaman ahirida yoⱪsulluⱪta ⱪalar, Ƣǝplǝt uyⱪusiƣa patⱪanlarƣa jǝndǝ kiyimni kiygüzǝr.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Seni tapⱪan atangning sɵzini angla, Anang ⱪeriƣanda uningƣa ⱨɵrmǝtsizlik ⱪilma.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Ⱨǝⱪiⱪǝtni setiwal, Uni ⱨǝrgiz setiwǝtmǝ. Danaliⱪ, tǝrbiyǝ wǝ yorutuluxnimu al.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Ⱨǝⱪⱪaniy balining atisi qong huxalliⱪ tapar; Dana oƣulni tapⱪan atisi uningdin hursǝn bolar.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Ata-anangni sɵyündürüp, Seni tuƣⱪan anangni hux ⱪil.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 I oƣlum, ⱪǝlbingni manga tapxur; Kɵzliringmu ⱨayatliⱪ yollirimƣa tikilsun!
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Qünki paⱨixǝ ayal qongⱪur oridur, Buzuⱪ yat ayal tar zindandur;
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Ular ⱪaraⱪqidǝk mɵküwelip, Insaniyǝt arisidiki wapasizlarni kɵpǝytǝr.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Kimdǝ azab bar? Kimdǝ dǝrd-ǝlǝm? Kim jedǝl iqidǝ ⱪalar? Kim nalǝ-pǝryad kɵtürǝr? Kim sǝwǝbsiz yarilinar? Kimning kɵzi ⱪizirip ketǝr?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Dǝl xarab üstidǝ uzun olturƣan, Əbjǝx xarabtin tetixⱪa aldiriƣan mǝyhorlar!
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Xarabning ajayib ⱪizilliⱪiƣa, uning jamdiki julaliⱪiƣa, Kixining gelidin xundaⱪ siliⱪ ɵtkǝnlikigǝ mǝptun bolup ⱪalma!
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 Ahirida u zǝⱨǝrlik yilandǝk qeⱪiwalidu, Oⱪ yilandǝk nǝxtirini sanjiydu.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Kɵz aldingda ƣǝlitǝ mǝnzirilǝr kɵrünidu, Aƣzingdin ⱪalaymiⱪan sɵzlǝr qiⱪidu.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Huddi dengiz-okyanlarda lǝylǝp ⱪalƣandǝk, Yǝlkǝnlik kemining moma yaƣiqi üstidǝ yatⱪandǝk bolisǝn.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 Sǝn qoⱪum: — Birsi meni urdi, lekin mǝn yarilanmidim! Birsi meni tayaⱪ bilǝn urdi, biraⱪ aƣriⱪini sǝzmidim!» — dǝysǝn. Biraⱪ sǝn yǝnǝ: «Ⱨoxumƣa kǝlsǝmla, mǝn yǝnila xarabni izdǝymǝn! — dǝysǝn.
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”