< Pǝnd-nǝsiⱨǝtlǝr 13 >
1 Dana oƣul atisining tǝrbiyisigǝ kɵngül ⱪoyar; Mǝshirǝ ⱪilƣuqi tǝnbiⱨkǝ ⱪulaⱪ salmas.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 Adǝm durus eƣizining mewisidin ⱨuzurlinar; Tuzkorlar zorawanliⱪⱪa ⱨǝwǝs ⱪilip zorawanliⱪⱪa uqrar.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 Sɵzdǝ eⱨtiyatqan kixi jenini saⱪlap ⱪalar; Aƣzi ittik ⱨalakǝtkǝ uqrar.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 Ⱨurunning arzu-tiliki bar, lekin erixǝlmǝs; Lekin tirixqan ǝtlinǝr.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 Ⱨǝⱪⱪaniy adǝm yalƣanqiliⱪtin yirginǝr; Ⱪǝbiⱨ bolsa sesip, xǝrmǝndǝ bolar.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 Yoli durusni ⱨǝⱪⱪaniyǝt ⱪoƣdar; Lekin gunaⱨkarni rǝzillik yiⱪitar.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 Bǝzilǝr ɵzini bay kɵrsǝtkini bilǝn ǝmǝliyǝttǝ ⱪuruⱪ sɵlǝttur; Bǝzilǝr ɵzini yoⱪsul kɵrsǝtkini bilǝn zor bayliⱪliri bardur.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 Ɵz bayliⱪi gɵrügǝ tutulƣan bayning jeniƣa ara turar; Biraⱪ yoⱪsullar ⱨeq wǝⱨimini anglimas.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 Ⱨǝⱪⱪaniy adǝmning nuri xadlinip parlar; Biraⱪ yaman adǝmning qiriƣi ɵqürülǝr.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 Kibirliktin pǝⱪǝt jedǝl-majirala qiⱪar; Danaliⱪ bolsa nǝsiⱨǝtni angliƣanlar bilǝn billidur.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Ixlimǝy tapⱪan ⱨaram bayliⱪ bǝrikǝtsizdur; Tǝr tɵküp ⱨalal tapⱪan güllinǝr.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 Tǝlmürginigǝ kütüp erixǝlmǝslik kɵngülni sunuⱪ ⱪilar, Lekin tǝxnaliⱪta erixkini «ⱨayatliⱪ dǝrihi»dur.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 [Hudaning] kalam-sɵzigǝ pisǝnt ⱪilmiƣan adǝm gunaⱨning tɵlimigǝ ⱪǝrzdar bolar; Lekin pǝrmanni ⱪǝdirligǝn adǝm yahxiliⱪ kɵrǝr.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 Aⱪilanining tǝlimi ⱨayatliⱪ bǝrgüqi bulaⱪtur, U seni ɵlüm tuzaⱪliridin ⱪutuldurar.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Aⱪilanilik adǝmni iltipatⱪa erixtürǝr; Biraⱪ tuzkorlarning yoli ǝgri-bügri, japaliⱪ bolar.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Pǝm-parasǝtlik adǝm bilimi bilǝn ix kɵrǝr; Ⱨamaⱪǝt ɵz nadanliⱪini axkarilar.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 Rǝzil alaⱪiqi bala-ⱪazaƣa uqrar; Sadiⱪ ǝlqi bolsa dǝrdkǝ dǝrmandur.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Tǝrbiyǝni rǝt ⱪilƣan adǝm namratlixip uyatⱪa ⱪalar; Əmma tǝnbiⱨni ⱪobul ⱪilƣan ⱨɵrmǝtkǝ erixǝr.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 Əmǝlgǝ axⱪan arzu kixigǝ xerin tuyular; Lekin ǝhmǝⱪlǝr yamanliⱪni taxlaxni yaman kɵrǝr.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 Aⱪilanilǝr bilǝn billǝ yürgǝn Dan. bolar; Biraⱪ ǝhmǝⱪlǝrgǝ ⱨǝmraⱨ bolƣan nalǝ-pǝryadta ⱪalar.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Bala-ⱪaza gunaⱨkarlarning kǝynidin besip mangar; Lekin ⱨǝⱪⱪaniylar yahxiliⱪning ǝjrini tapar.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 Yahxi adǝm pǝrzǝntlirining pǝrzǝntlirigǝ miras ⱪaldurar; Gunaⱨkarlarning yiƣⱪan mal-dunyaliri ⱨǝⱪⱪaniylar üqün toplinar.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 Yoⱪsulning taxlanduⱪ yeri mol ⱨosul berǝr, Lekin adalǝtsizliktin u wǝyran bolar.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 Tayaⱪni ayiƣan kixi oƣlini yahxi kɵrmǝs; Balini sɵygǝn kixi uni ǝstayidil tǝrbiyilǝp jazalar.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 Ⱨǝⱪⱪaniy adǝm kɵngli ⱪanaǝt tapⱪuqǝ ozuⱪ yǝr; Yamanning ⱪorsiⱪi aq ⱪalar.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.