< Wehiy 15 >
1 Asmanda zor hem karametlik yene bir alametni, yeni axirqi yette balayi’apetni tutup turghan yette perishtini kördüm (axirqi balayi’apet déyilishtiki seweb, Xudaning ghezipi bular bilen axirlishidu).
Kumwamba ndinaona chizindikiro china chachikulu ndi chodabwitsa: angelo asanu ndi awiri ali ndi miliri isanu ndi iwiri yomaliza chifukwa Mulungu anakwiya kotheratu.
2 Men yene ot arilash eynek déngizidek bir körünüshni hem eynek déngizning üstide turghan, diwe we uning but-heykili we namining reqimi üstidin ghalib kelgenlerni kördüm. Ularning qollirida Xuda bergen chiltarlar bolup,
Ndipo ndinaona chimene chinaoneka ngati nyanja yonyezimira yosakaniza ndi moto, ndipo pambali pa nyanjayo panayima amene anagonjetsa chirombo chija ndi fano lake, ndi nambala yotanthauza dzina lake. Anthuwo ananyamula azeze amene Mulungu anawapatsa.
3 ular Xudaning qul-xizmetkari bolghan Musaning küyini hem Qozining küyini éytishatti: — «Ulugh we karamet Séning qilghanliring, I Hemmige Qadir Perwerdigar Xuda, Yolliring adil we heqtur, I pütkül ellerning Padishahi!
Iwo ankayimba nyimbo ya Mose, mtumiki wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwana Wankhosa. Nyimbo yake inkati, “Zochita zanu ndi zazikulu ndi zodabwitsa, Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse Njira zanu ndi zachilungamo ndi zoona, Mfumu ya mitundu yonse.
4 I Perwerdigar, kim Sendin qorqmaydighan, Namingni ulughlimaydighan bolalisun? Chünki birdinbir muqeddes Özüngdursen; Barliq eller aldinggha kélidu, Sanga sejde qilidu; Chünki heqqaniy qilghanliring ashkare boldi».
Inu Ambuye, ndani angapande kukuopani, ndi kulemekeza dzina lanu? Pakuti Inu nokha ndiye woyera. Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzapembedza pamaso panu, pakuti ntchito zanu zolungama zaonekera poyera.”
5 Bu ishlardin kéyin, men kördümki, mana ershtiki ibadetxana, yeni höküm-guwahliq chédiri échildi!
Zitatha izi, ndinaona kumwamba Nyumba ya Mulungu imene ndi Tenti ya Umboni, atatsekula.
6 Yette balayi’apetni öz ilkide tutqan yette perishte pakiz, parqirap turidighan libas kiygen, köksige altun kemer baghlighan halda ibadetxanidin chiqti.
Mʼnyumbamo munatuluka angelo asanu ndi awiri ndi miliri isanu ndi iwiri. Angelowo anavala nsalu zoyera bwino zonyezimira ndi malamba agolide pa zifuwa zawo.
7 Töt hayat mexluqning biri yette perishtige ebedil’ebed yashaydighan Xudaning qehri bilen tolghan yette altun chinini berdi. (aiōn )
Ndipo kenaka chimodzi cha zamoyo zinayi zija chinapereka kwa angelo asanu ndi awiri mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi ukali wa Mulungu amene ali ndi moyo mpaka muyaya. (aiōn )
8 Ibadetxana Xudaning shan-sheripi we qudritidin tütün bilen liq toldi. Yette perishtining yette balayi’apiti ayaghlashmighuche, héchkim ibadetxanigha kirelmidi.
Ndipo Nyumba ya Mulungu inadzaza ndi utsi wochokera ku ulemerero wa Mulungu ndi ku mphamvu zake, ndipo panalibe yemwe akanalowa mʼNyumbayo mpaka miliri isanu ndi iwiri ya angelo asanu ndi awiri aja itatha.