< Захарія 2 >

1 І звів я очі свої та й побачив, аж ось муж, а в його руці мірни́чий шнур.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
2 І сказав я: „Куди ти йдеш?“А він відказав мені: „Щоб змі́ряти Єрусалим, щоб побачити, яка ширина́ його та яка довжина́ його“.
Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
3 Аж ось ангол, що говорив зо мною, виходить, а навпроти нього виходить Ангол інший.
Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
4 І сказав він до нього: „Біжи, говори цьому юнако́ві, кажучи: Невкрі́плений буде Єрусалим через многість людей та худоби в сере́дині його.
ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
5 А Я стану для нього, — говорить Господь, — огняни́м муром навко́ло, і стану славою в сере́дині його.
Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
6 „Горе, горе, — втікайте з північного кра́ю, — говорить Госпо́дь, — бо на чотири небесні вітри́ розпоро́шу Я вас, промовляє Господь.
“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
7 Горе, — втікай до Сіону, мешка́нко дочки́ Вавило́ну!
“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
8 Бо так промовляє Госпо́дь Савао́т: Для слави послав Він мене до наро́дів, що вас грабува́ли, бо хто вас дото́ркується, той дото́ркується до зірця́ Його ока.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
9 Бо ось тільки махну́ Я своєю рукою на них, — і для їхніх рабів вони здо́биччю стануть, і пізнаєте ви, що Господь Саваот мене вислав.
Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
10 Співай же та ті́шся, о до́чко Сіону, бо ось Я прихо́джу та перебува́тиму посеред те́бе, говорить Госпо́дь!
“Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
11 І дня то́го прилу́чаться люди числе́нні до Господа, „і стануть наро́дом Мені, а Я перебува́тиму посеред те́бе“, і довідаєшся, що Господь Саваот мене вислав до тебе.
“Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
12 І Юду, спа́док Свій, пося́де Господь на святій землі, і вибере Єрусалима Він ще!
Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
13 Замовчи ж, всяке тіло, перед Господнім лицем, бо Він пробуди́вся з мешка́ння святого Свого́!“
Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”

< Захарія 2 >