< Псалми 98 >

1 Псалом.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 Спасі́ння Своє Господь ви́явив, перед очима наро́дів відкрив Свою правду.
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 Пам'ятає Він Якову милість Свою, й Свою вірність для дому Ізра́їля. Бачать всі кі́нці землі те спасі́ння, що чинить наш Бог.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 Уся зе́мле, викли́куйте Господу, покли́куйте радісно, і співайте та грайте!
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 Грайте Господе́ві на гу́слах, на гу́слах і піснопі́нням,
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 на су́рмах і голосом рогу викликуйте перед обличчям Царя Цього й Господа!
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Нехай шумить море й усе, що у ньому, вселе́нна й мешка́нці її,
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 ріки хай плещуть в долоні, ра́зом радіють хай го́ри
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 перед обличчям Господнім, бо Він землю судити гряде́: Він за справедливістю буде судити вселе́нну, і народи по правді!
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< Псалми 98 >