< Псалми 97 >

1 Царю́є Господь: хай радіє земля, нехай веселя́ться числе́нні острови́!
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Хмара та мо́рок круг Нього, справедливість та право — підстава престолу Його.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Огонь іде перед лицем Його́, і ворогів Його па́лить навко́ло.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Освітили вселе́нну Його блискави́ці, — те бачить земля та тремти́ть!
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Гори, як віск, розтопи́лися перед обличчям Господнім, перед обличчям Господа всієї землі.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Небо розповідає про правду Його, й бачать славу Його всі наро́ди.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Нехай посоро́млені будуть усі, хто і́долам служить, хто божка́ми вихва́люється! Додо́лу впадіть перед Ним, усі бо́ги!
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Почув і звесели́вся Сіон, і поті́шились Юдині до́чки через Твої при́суди, Господи,
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 бо над усією землею Найви́щий Ти, Господи, над бога́ми всіма́ Ти піднесе́ний сильно!
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Хто Господа любить, — нена́видьте зло! Хто рятує душі святих Своїх, Той ви́зволить їх із руки несправедли́вих.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Світло сі́ється для справедливого, а для простосердих — розра́да.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Радійте, праведні, Господом, і славте Його святу па́м'ять!
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.

< Псалми 97 >