< Псалми 96 >
1 Співайте для Господа пісню нову́, уся зе́мле, — співайте для Господа!
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Співайте для Господа, благословля́йте Ім'я́ Його, з дня на день сповіщайте спасі́ння Його!
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Розповідайте про славу Його між пога́нами, про чу́да Його — між усі́ми наро́дами,
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 бо великий Господь і просла́влений ве́льми, Він грізни́й понад богів усіх!
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Бо всі боги наро́дів — божки́, а Госпо́дь створив небеса́, —
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 перед лицем Його слава та велич, сила й краса — у святині Його!
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Дайте Господу, ро́ди наро́дів, дайте Господу славу та силу,
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 дайте Господу славу йме́ння Його, жертви прино́сьте і вхо́дьте в подві́р'я Його!
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Додолу впадіть ув оздо́бі святій перед Господом, тремтіть перед обличчям Його, уся зе́мле,
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 сповістіть між наро́дами: „Царю́є Госпо́дь! Він вселе́нну зміцни́в, щоб не захита́лась, Він бу́де судити людей справедли́во“!
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Хай небо радіє, і хай весели́ться земля, нехай гримить море й усе, що у нім,
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 нехай поле радіє та все, що на ньому! Нехай заспівають тоді всі дере́ва лісні́, —
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 перед Господнім лицем, бо гряде́ Він, бо зе́млю судити гряде́, е́ — Він за справедливістю буде судити вселе́нну, і наро́ди — по правді Своїй!
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.