< Псалми 78 >
1 Пісня навча́льна Асафова.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 нехай я відкрию уста́ свої при́казкою, нехай старода́вні прислі́в'я я ви́словлю!
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Що́ ми чули й пізнали, і що́ розповідали батьки́ наші нам, —
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 того не сховаємо від їхніх сині́в, будемо розповіда́ти про славу Господню аж до покоління оста́ннього, і про силу Його та про чу́да Його, які Він учинив!
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Він поставив засві́дчення в Якові, а Зако́на поклав ув Ізраїлі, про які наказав був Він нашим батька́м завідо́мити про них синів їхніх,
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 щоб знало про це поколі́ння майбу́тнє, сини, що наро́джені будуть, — уста́нуть і будуть розповідати своїм дітям.
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 І положать на Бога надію свою, і не забудуть діл Божих, Його ж заповіді берегти́муть.
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 І не стануть вони, немов їхні батьки́, поколі́нням непокі́рливим та бунтівни́чим, поколінням, що серця свого́ не поста́вило міцно, і що дух його Богу невірний.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Сини Єфрема, озбро́єні лу́чники, повернулися взад у день бо́ю:
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 вони не берегли́ заповіту Божого, а ходити в Зако́ні Його відреклися,
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 і забули вони Його чи́ни та чу́да Його, які їм показав.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Він чудо вчинив був для їхніх батькі́в ув єгипетськім кра́ї, на полі Цоа́нськім:
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Він море розсік, і їх перепрова́див, а воду поставив, як вал;
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 і прова́див їх хмарою вдень, а ся́йвом огню́ цілу ніч;
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 на пустині Він скелі розсік, і щедро усіх напоїв, як з безо́дні.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Він витягнув із скелі пото́ки, і во́ди текли, немов ріки.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Та гріши́ли вони проти Нього ще да́лі, і в пустіші гніви́ли Всевишнього,
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 і Бога вони випробо́вували в своїм серці, для душ своїх ї́жі бажаючи.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 І вони говорили насу́проти Бога й казали: „Чи Бог зможе в пустині трапе́зу згото́вити?“
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Тож ударив у скелю — і во́ди лину́ли, і полили́ся пото́ки! „Чи Він зможе також дати хліба? Чи Він наготує м'яси́ва наро́дові Своє́му?“
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Тому́ то почув це Господь та й розгні́вався, — і огонь запалав проти Якова, і проти Ізраїля теж знявся гнів,
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 бо не ві́рували вони в Бога, і на спасі́ння Його не наді́ялись.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 А Він хмарам згори наказав, — і відчинив двері неба,
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 і спустив, немов дощ, на них ма́нну для їжі, — і збі́жжя небесне їм дав:
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Хліб а́нгольський їла люди́на, Він послав їм поживи до си́тости!
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Крім цього, Він схі́днього вітра пору́шив на небі, і міццю Своєю привів полудне́вого вітра, —
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 і дощем на них м'ясо пустив, немов по́рох, а птаство крила́те, як мо́рський пісо́к,
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 і спустив його серед табо́ру його́, коло наметів його.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 І їли вони та й наси́тились ду́же, — Він їм їхнє бажа́ння приніс!
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 Та ще не вдовольни́ли жада́ння свого́, ще їхня ї́жа була в їхніх уста́х,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 а гнів Божий підня́вся на них, та й побив їхніх ситих, і вибра́нців Ізраїлевих повали́в.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 Проте́ ще й далі грішили вони та не вірили в чу́да Його,
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 — і Він докінчи́в у марно́ті їхні дні, а їхні літа́ — у страху.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Як Він їх побива́в, то бажали Його, — і верта́лися, й Бога шукали,
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 і прига́дували, що Бог — їхня скеля, і Бог Всевишній — то їхній Викупите́ль.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 І своїми уста́ми вле́щували Його, а своїм язико́м лжу спліта́ли Йому́,
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 бо їхнє серце не міцно стояло при Нім, і не були́ вони вірні в Його заповіті.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Та він, Милосердний, гріх проща́в і їх не губив, і часто відве́ртав Свій гнів, і не буди́в усю Свою лютість,
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 і Він пам'ятав, що вони тільки тіло, вітер, який перехо́дить і не поверта́ється!
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Скільки вони прогнівля́ли Його на пустині, зневажа́ли Його на степу́!
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 І все знову та знов випробо́вували вони Бога, і зневажа́ли Святого Ізра́їлевого, —
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 вони не пам'ята́ли руки Його з дня, як Він ви́бавив їх із недолі,
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 як в Єгипті чинив Він знаме́на Свої, а на полі Цоа́нському чу́да Свої,
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 і в кров оберну́в річки їхні та їхні пото́ки, щоб вони не пили́.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Він послав був на них рої мух, — і їх же́рли вони, і жаб — і вони їх губили.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 А врожай їхній віддав був Він гу́сені, а їхню пра́цю — сарані́.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Виноград їхній Він гра́дом побив, а при́морозком — їхні шовко́виці.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 І Він градові віддав їхній скот, а бли́скавкам — че́реди їхні.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Він послав був на них Свій гнів запальни́й, і лютість, й обу́рення, й у́тиск, насла́ння злих анголі́в.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Він дорогу зрівня́в був для гніву Свого, їхні душі не стримав від смерти, життя ж їхнє віддав морови́ці.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 І побив Він усіх перворі́дних в Єгипті, пе́рвістків сили в наметах Ха́мових.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 І повів Він, немов ту отару, наро́д Свій, і їх попрова́див, як стадо, в пустині.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 І провадив безпечно Він їх, і вони не боялись, а море накри́ло було́ ворогів їхніх.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 І Він їх привів до границі святині Своєї, до тієї гори, що прави́ця Його набула́.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 І наро́ди Він повиганя́в перед їхнім обличчям, і кинув для них жеребка́ про спа́док, — і в їхніх наме́тах племе́на Ізраїлеві осели́в.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Та й далі вони випробо́вували та гніви́ли Всевишнього Бога, і Його постано́в не доде́ржували,
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 і відступали та зраджували, немов їхні батьки відверну́лись, як обма́нливий лук.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 І же́ртівниками своїми гніви́ли Його, і дрочи́ли Його своїми фіґу́рами.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Бог почув усе це — і розгні́вався, і сильно обри́дивсь Ізраїлем,
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 і покинув осе́лю в Шіло́, скинію ту, що вмістив був посеред людей,
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 і віддав до неволі Він силу Свою, а вели́чність Свою — в руку во́рога.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 І віддав для меча Свій наро́д, і розгнівався був на спа́дщину Свою:
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 його юнакі́в огонь пожира́в, а дівча́там його не співали весі́льних пісе́нь,
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 його священики від меча полягли́, — і не плакали вдови його.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Та небавом збудився Господь, немов зо́ сну, як той ве́лет, що ніби вином був підко́шений,
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 і вдарив Своїх ворогів по оза́дку, — вічну га́ньбу їм дав!
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Та Він погорди́в намет Йо́сипів, і племе́на Єфремового не обрав,
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 а вибрав Собі плем'я Юдине, го́ру Сіон, що її полюбив!
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 І святиню Свою збудував Він, як місце високе, як землю, що навіки її вґрунтува́в.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 І вибрав Давида, Свого раба, і від коша́р його взяв,
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 від кі́тних ове́чок його Він привів, щоб Якова пас він, народа Свого, та Ізраїля, спа́док Свій, —
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 і він пас їх у щирості серця свого́, і прова́див їх мудрістю рук своїх!
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.