< Псалми 64 >

1 Для дириґента хору. Псалом Давидів. Вислухай, Боже, мій голос, як ска́ржуся я, від стра́ху ворожого душу мою хорони!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Заховай мене від потає́много збору злочинців, від крику сваві́льців,
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 які нагостри́ли свого язика́, як меча, натягнули стрілу́ свою словом гірки́м,
Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 щоб таємно стріляти в невинного, — вони нагло стріля́тимуть в нього, і не бу́дуть боятись!
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 У злій справі зміцня́ють себе, змовля́ються па́стки таємно розста́вити, кажуть: „Хто бу́де їх бачити?“
Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 Вони кривди ховають. Загинемо, як за́дум їхній спо́вниться, бо нутро́ чоловіка та серце — глибоке!
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 Але́ вчинить Бог, що стріла́ на них стрі́лить, — і на́гло пора́нені будуть,
Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 і вчинить, що їхній язик допаде́ться до них, — і будуть хита́ти головою усі, хто спогля́не на них!
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 І всі люди боятися будуть, і будуть розказувати про чин Бога, і ді́ло Його зрозуміють!
Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 І праведний Господом бу́де раді́ти, і буде вдава́тись до Нього, і бу́дуть похва́лені всі простосе́рді!
Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!

< Псалми 64 >