< Псалми 6 >

1 Для дириґента хору. На струнних знаря́ддях. На октаву. Псалом Давидів. Не карай мене, Господи, в гніві Своїм, не завдава́й мені кари в Своїм пересе́рді!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Помилуй мене, Господи, я ж бо слаби́й, уздоро́в мене, Господи, бо тремтять мої кості,
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 і душа моя сильно стривожена, а ти, Господи, доки?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Вернися, о Господи, ви́зволи душу мою, ради ласки Своєї спаси Ти мене!
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 Бож у смерті нема пам'ята́ння про Тебе, у шео́лі ж хто буде хвалити Тебе? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 Зму́чився я від стогна́ння свого́, щоночі постелю свою обмиваю слізьми́, сльозами своїми окроплюю ложе своє!
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 Моє око зів'я́ло з печалі, поста́ріло через усіх ворогів моїх.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Відступіться від мене, усі беззако́нники, бо почув Господь голос мого плачу́!
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 Блага́ння моє Господь ви́слухає, молитву мою Господь при́йме, —
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 усі мої вороги посоро́млені бу́дуть, і будуть настра́шені дуже: хай ве́рнуться, — і будуть вони посоро́млені за́раз!
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Псалми 6 >