< Псалми 52 >
1 Для дириґента хору. Псалом навча́льний Давидів, як прийшов був ідуме́янин Доеґ та й Саулові був оповів, і до нього сказав: „Давид увійшов до дому Ахіме́леха“. Чого хва́лишся злом, о могу́тній? Цілий де́нь Божа милість зо мною.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.” Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu? Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse, iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
2 Замишляє лукавство язик твій, як та бритва наго́стрена ти, що чиниш обману!
Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena; lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nʼkunyenga.
3 Ти зло полюбив над добро, а неправду — більш, як правду казати, (Се́ла)
Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi. Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona. (Sela)
4 ти любиш усякі шкідливі слова́, ти язи́ку обманний!
Umakonda mawu onse opweteka, iwe lilime lachinyengo!
5 Отож, Бог зруйнує наза́вжди тебе, тебе викине й вирве з намету тебе, й тебе викоренить із країни життя. (Се́ла)
Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya: iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako; iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
6 І побачать це пра́ведні, й будуть боятись, і будуть сміятися з нього:
Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha; adzamuseka nʼkumanena kuti,
7 „Ось муж, що Бога не чинить своєю тверди́нею, та на великість багатства свого покладає надію, втікає до злого свого“.
“Pano tsopano pali munthu amene sanayese Mulungu linga lake, koma anakhulupirira chuma chake chambiri nalimbika kuchita zoyipa!”
8 А я — як зелена оли́вка у Божому домі, наді́юсь на Божую милість на вічні віки́!
Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu; ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu kwa nthawi za nthawi.
9 Буду сла́вити вічно Тебе, що вчинив Ти оце, і про йме́ння Твоє буду звіщати побожним Твоїм, що добре воно!
Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita; chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.