< Псалми 37 >

1 Давидів.
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 бо вони, як трава, будуть скоро поко́шені, і мов та зелена били́на — пов'я́нуть!
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Надійся на Господа й добре чини, землю заме́шкуй та правди дотримуй!
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Хай Господь буде розкіш твоя, — і Він спо́внить тобі твого серця бажа́ння!
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 На Господа здай доро́гу свою, і на Нього надію клади, і Він зробить,
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 і Він ви́провадить, немов світло, твою справедливість, а правду твою — немов пі́вдень.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Жди Господа мо́вчки й на Нього наді́йся, не розпалюйся гнівом на того, хто щасливою чинить дорогу свою, на люди́ну, що виконує за́думи злі.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Повстри́майсь від гніву й покинь пересе́рдя, не розпа́люйся лютістю, щоб чини́ти лиш зло,
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 бо ви́тяті будуть злочинці, а ті, хто вповає на Господа — землю вспадку́ють!
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 А ще тро́хи — й не буде безбожного, і будеш дивитись на місце його — і не буде його,
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 а покірні вспадку́ють землю, — і зарозкошу́ють ми́ром великим!
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Лихе замишляє безбожний на праведного, і скрего́че на нього своїми зубами,
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 та Господь посміється із нього, — бачить бо Він, що набли́жується його день!
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Безбожні меча добува́ють та лука свого натягають, щоб звали́ти нужде́нного й бідного, щоб порізати людей простої дороги, —
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 та вві́йде їхній меч до їхнього власного серця, і пола́мані будуть їхні лу́ки!
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Краще мале справедливого, ніж велике багатство безбожних, і то багатьох,
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 бо зла́мані будуть раме́на безбожних, а справедливих Господь підпира́є!
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 Знає Господь дні неви́нних, а їхня спадщина пробуде навіки,
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 за лихолі́ття не будуть вони посоро́млені, і за днів голоду ситими бу́дуть.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 Бо загинуть безбожні, і Господні вороги, як овечий той лій, зани́кнуть, у димі заникнуть вони!
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Позичає безбожний — і не віддає, а праведний милість висві́дчує та роздає,
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 бо благословенні від Нього вспадку́ють землю, а прокля́ті від Нього — пони́щені будуть!
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 Від Господа кроки люди́ни побожної ставляться міцно, і Він любить дорогу її;
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 коли ж упаде́, то не буде поки́нена, бо руку її підпирає Госпо́дь.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Я був молодий і поста́рівся, та не бачив я праведного, щоб опу́щений був, ні нащадків його, щоб хліба просили.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 Кожен день виявляє він милість та позичає, і над пото́мством його благословення.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Ухиляйся від злого та добре чини, та й навіки живи!
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 Бо любить Господь справедливість, і Він богобі́йних Своїх не покине, — вони будуть навіки бере́жені, а насіння безбожних загине!
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 Успадку́ють праведні землю, і повік будуть жити на ній.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 Уста праведного кажуть мудрість, язик же його промовляє про право,
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 Закон Бога його — в його серці, кроки його не спіткну́ться.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 А безбожний чату́є на праведного, і пильнує забити його́,
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 та Господь не зоставить його в руках того, і несправедливим не вчи́нить його, коли буде судити його.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Надійся на Господа, та держися дороги Його, — і піднесе Він тебе, щоб успадкува́ти землю, ти бачитимеш, як пони́жені будуть безбожні.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 Я бачив безбожного, що збуджував по́страх, що розкорени́вся, немов саморосле зелене те дерево,
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 та він промину́в, — й ось немає його, і шукав я його, — й не знайшов!
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Бережи непови́нного та дивися на праведного, бо люди́ні споко́ю належить майбу́тність,
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 переступники ж ра́зом понищені будуть, — майбутність безбожних загине!
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 А спасі́ння праведних — від Господа, Він їхня тверди́ня за ча́с лихолі́ття,
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 і Господь їм поможе та їх порятує, ви́зволить їх від безбожних і їх збереже, — бо вдавались до Нього вони!
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Псалми 37 >