< Псалми 118 >
1 Дякуйте Господу, добрий бо Він, бо навіки Його милосердя!
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Нехай скаже Ізраїль, бо навіки Його милосердя!
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Нехай скаже дім Ааро́нів, бо навіки Його милосердя!
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Нехай скажуть ті, хто бої́ться Господа, бо навіки Його милосердя!
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 У тісно́ті я кли́кав до Господа, — і просто́ром озвався до мене Госпо́дь!
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 Зо мною Господь — не боюся ніко́го, що зро́бить люди́на мені?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 Господь серед тих, що мені помагають, — і побачу загибіль своїх ненави́сників.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Краще вдаватись до Господа, ніж наді́ятися на люди́ну,
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 краще вдаватись до Господа, ніж наді́ятися на вельмо́жних!
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 Всі наро́ди мене оточи́ли, — я ж Господнім Ім'я́м їх понищив!
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Оточи́ли мене й обступили мене, — я ж Господнім Ім'я́м їх понищив!
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Оточили мене немов бджо́ли, та погасли вони, як терно́вий огонь, — я бо Господнім Ім'я́м їх понищив!
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Дошкульно попхну́в ти мене на паді́ння, — та Господь спас мене́!
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 Господь моя сила та пісня, і став Він спасі́нням мені!
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 Голос співу й спасі́ння в наметах між пра́ведників: „Госпо́дня прави́ця виконує чу́да!
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 Правиця Господня підно́ситься, прави́ця Господня вико́нує чу́да!“
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 Не помру́, але жи́тиму, і буду звіщати про чи́ни Господні!
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Покара́ти мене — покарав був Госпо́дь, та смерти мені не завдав.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Відчиніте мені брами правди, — я ними ввійду́, буду сла́вити Господа!
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 „Це брама Господня, — праведники в неї вхо́дять“.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Я буду хвалити Тебе, бо озвався до мене, і став Ти спасі́нням мені!
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 Камінь, що його будівни́чі відки́нули, той нарі́жним став каменем, —
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 від Господа ста́лося це, і дивне воно в очах наших!
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Це день, що його́ створи́в Господь, — радіймо та тішмося в нім!
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Про́симо, Господи, — спаси! Про́симо, Господи, — пощасти́!
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Благословен, хто гряде́ у Господнє Ім'я́! Благословляємо вас із Господнього дому!
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Господь — Бог, і зася́яв Він нам. Прив'яжі́те святковую жертву шнура́ми аж до нарі́жників же́ртівника!
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Ти мій Бог, і я бу́ду Тебе прославля́ти, мій Боже, я буду Тебе велича́ти!
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Дякуйте Господу, добрий бо Він, бо навіки Його милосердя!
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.