< Псалми 102 >

1 Молитва вбогого, коли він слабне та перед Господнім лицем виливає мову свою. Господи, ви́слухай молитву мою, і блага́ння моє нехай ді́йде до Тебе!
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Не ховай від мене обличчя Свого́, в день недолі моєї — схили Своє ухо до ме́не, в день блага́ння озвися неба́вом до мене!
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 Бо минають, як дим, мої дні, а кості мої — немов ви́сохли в о́гнищі.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Як трава та — поби́те та ви́сохло серце моє, так що я забував їсти хліб свій.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 Від зо́йку стогна́ння мого прили́пли до тіла мого мої кості.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Уподо́бився я пелика́нові пустині, я став, як той пу́гач руїн!
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 Я безсонний, і став, немов пташка само́тня на да́сі.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Увесь день ображають мене вороги́ мої, ті, хто з мене кепку́є, заприсяглись проти мене!
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 І по́піл я їм, немов хліб, а напо́ї свої із плаче́м перемі́шую, —
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 через гнів Твій та лютість Твою, бо підняв був мене Ти та й кинув мене́.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Мої дні — як похи́лена тінь, а я сохну, немов та трава!
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 А Ти, Господи, бу́деш повік пробува́ти, а пам'ять Твоя — з роду в рід.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Ти встанеш та змилуєшся над Сіо́ном, бо час учини́ти йому милосердя, бо прийшов речене́ць,
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 бо раби Твої покоха́ли й камі́ння його́, і порох його полюбили!
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 І будуть боятись наро́ди Господнього Йме́ння, а всі зе́мні царі — слави Твоєї.
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Бо Господь побудує Сіона, поя́виться в славі Своїй.
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 До молитви забутих зве́рнеться Він, і моли́тви їхньої не осоро́мить.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Запишеться це поколі́нню майбу́тньому, і наро́д, який ство́рений буде, хвали́тиме Господа,
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 бо споглянув Він із високо́сти святої Своєї, Господь зо́рив на землю з небе́с,
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 щоб почути зідха́ння ув'я́зненого, щоб на смерть прироко́ваних ви́зволити,
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 щоб розповіда́ти про Йме́ння Господнє в Сіоні, а в Єрусалимі — про славу Його,
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 коли ра́зом зберу́ться наро́ди й держа́ви служи́ти Господе́ві.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Мою силу в дорозі Він ви́снажив, дні мої скороти́в.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Я кажу́: „Боже мій, — не бери Ти мене в половині днів моїх! Твої ро́ки — на вічні віки.
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Колись землю Ти був закла́в, а небо — то чин Твоїх рук, —
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 позникають вони, а Ти бу́деш стояти. І всі вони, як оде́жа, загинуть, Ти їх зміниш, немов те вбрання́, — і мину́ться вони.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 Ти ж — Той Самий, а роки Твої не закі́нчаться!
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Сини Твоїх рабів будуть жити, а їхнє насіння стоя́тиме міцно перед обличчям Твоїм!“
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Псалми 102 >