< Неемія 3 >

1 І встав Еліяші́в, первосвященик, та брати його священики, і збудували Овечу браму. Вони освятили її, і повставля́ли її двері, й аж до башти Меа освятили її, аж до башти Ханан'їла.
Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
2 А поруч нього будували єрихо́няни, а поруч них будував Заккур, син Імріїв.
Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
3 А браму Рибну збудували сини Сенаїні, і вони покрили її бру́ссями, і повставляли двері її, замки́ її та за́суви її.
Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
4 А поруч них направляв Меремот, син Урії, Коцового сина, а поруч них направляв Мешуллам, син Берехії, Мешав'їлового сина, а поруч них направляв Садок, Баанин син.
Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
5 А поруч них направляли текояни, але́ їхні вельмо́жі не схилили своєї шиї в службу свого Господа.
Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
6 А браму Стару направляли Йояда, син Пасеахів, та Мешуллам, син Бесодеїн, — вони покрива́ли бру́ссями, і вставляли двері її, і замки́ її та за́суви її.
Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
7 А поруч них направляв ґів'онеянин Мелатія та меронотеянин Ядон, люди Ґів'ону та Міцпи, що належали до володі́ння намісника Заріччя.
Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
8 Поруч нього направляв Уззіїл, син Хархаїн, з золотарів, а поруч нього направляв Хананія, син Раккахімів, — і вони віднови́ли Єрусалима аж до Широкого муру.
Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
9 А поруч нього направляв Рефая, син Хурів, зверхник половини єрусалимської округи.
Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
10 А поруч нього направляв Єдая, син Харумафів, а то навпроти дому свого, а при його руці направляв Хаттуш, син Хашавнеїн.
Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
11 Другу міру направляв Малкійя, син Харімів, та Хашшув, син Пахат-Моавів, та башту Печей.
Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
12 А поруч нього направляв Шаллум, син Лохеша, зверхник половини єрусалимської окру́ги, він та дочка́ його.
Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
13 Браму Долинну направляв Ханун та ме́шканці Заноаху, — вони збудували її, і повставляли двері її, замки́ її та за́суви її, і тисячу ліктів у мурі аж до Смітнико́вої брами.
Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
14 А Смітнико́ву браму направив Малкійя, син Рехавів, зверхник бет-керемської округи, — він збудував її, і повставля́в її двері, замки́ її та за́суви її.
Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
15 А Джерельну браму направив Шаллум, син Кол-Хезеїв, зверхник округи Міцпи, — він збудував її, і покри́в її, і повставля́в її двері, замки́ її та за́суви її, і направив мура ставу Шелах до царсько́го садка́, і аж до ступені́в, що спускаються з Давидового Міста.
Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
16 За ним направляв Неемія, син Азбуків, зверхник половини бетцурської окру́ги аж до місця навпроти Давидових гробі́в і аж до зробленого ста́ву, і аж до дому Лицарів.
Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
17 За ним направляли Левити: Рехум, син Баніїв, поруч нього направляв зверхник половини округи Кеїла, для своєї окру́ги.
Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
18 За ним направляли їхні брати: Баввай, син Хенададів, зверхник половини окру́ги Кеїла.
Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
19 І направляв поруч нього Езер, син Єшуїн, зверхник округи, міру другу, від місця навпроти виходу до зброя́рні наріжника.
Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
20 За ним ревно направляв Барух, Заббаїв син, міру другу, від наріжника аж до входу до дому первосвященика Еліяшіва.
Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
21 За ним направляв Меремот, син Урійї, сина Коцового, міру другу, від входу до Еліяшівового дому й аж до кінця Еліяшівового дому.
Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
22 А за ним направляли священики, люди йорданської окру́ги.
Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
23 За ним направляв Веніямин, син Хашшувів, навпроти свого дому; за ним направляв Азарія, син Маасеї, сина Ананіїного, при своєму домі.
Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
24 За ним направляв Біннуй, син Хенададів, міру другу, від Азаріїного дому аж до нарі́жника й аж до ро́гу.
Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
25 Палал, син Узаїв, — від місця навпроти наріжника та в горі́шній башті, що вихо́дить із царсько́го дому, що при в'язни́чному подві́р'ї. За ним Педая, син Пар'ошів.
Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
26 А підда́нці храму сиділи в Офелі аж до місця навпроти Водної брами на схід та навпро́ти виступа́ючої башти.
ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
27 За ним направляли техояни, міру другу, від місця навпроти великої виступаючої башти й аж до офельського му́ру.
Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
28 З-над Кінської брами направляли священики, кожен навпроти дому свого́.
Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
29 За ним и направляв Садо́к, син Іммерів, навпроти свого дому, а за ним направляв Шемая, син Шеханіїн, сторож Схі́дньої брами.
Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
30 За ним направляв Хананія, син Шелеміїн, та Ханун, шо́стий син Цалафів, міру другу; за ним направляв Мешуллам, син Берехіїн, навпроти своєї кімна́ти.
Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
31 За ним направляв Малкійя, син золотаря́, аж до дому храмови́х підда́нців та крамарі́в, навпроти брами Міфкад і аж до наріжної го́рниці.
Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
32 А між наріжною го́рницею до Овечої брами направляли золотарі́ та крамарі́.
Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.

< Неемія 3 >