< Михей 3 >

1 А я відказав: Послухайте ж, го́лови Якова та начальники дому Ізраїля, — чи ж не ва́м знати право?
Ndipo ine ndinati, “Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli. Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
2 Добро ви нена́видите та кохаєте зло, шкіру їхню здираєте з них, а їхнє тіло — з косте́й їхніх.
inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa; inu amene mumasenda khungu la anthu anga, ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
3 Ви оста́нок наро́ду Мого їсте та стягаєте з них їхню шкіру, а їхні кості ламаєте, і січе́те, немов до горня́ти, і мов м'ясо в котел.
inu amene mumadya anthu anga, mumasenda khungu lawo ndi kuphwanya mafupa awo; inu amene mumawadula nthulinthuli ngati nyama yokaphika?”
4 Вони тоді кли́кати будуть до Господа, та Він відповіді їм не дасть, і заховає обличчя Своє того ча́су від них, коли будуть робити лихі свої вчинки.
Pamenepo adzalira kwa Yehova, koma Iye sadzawayankha. Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
5 Так говорить Госпо́дь на пророків, що вводять наро́д Мій у блуд, що зубами своїми гризу́ть та покли́кують: „Мир!“А на то́го, хто їм не дає що до рота, на ньо́го святую війну оголо́шують.
Yehova akuti, “Aneneri amene amasocheretsa anthu anga, ngati munthu wina awapatsa chakudya amamufunira ‘mtendere;’ ngati munthu wina sawapatsa zakudya amamulosera zoyipa.
6 Тому буде вам ніч, щоб не стало видіння, і сте́мніє вам, щоб не чарува́ти. І над тими пророками сонце зако́титься, і над ними поте́мніє день.
Nʼchifukwa chake kudzakuderani, simudzaonanso masomphenya, mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso. Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
7 І посоро́млені будуть такі прозорли́вці, і будуть засти́джені чарівники́, і всі вони свої у́ста закриють, бо не буде їм Божої відповіді.
Alosi adzachita manyazi ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa. Onse adzaphimba nkhope zawo chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
8 А я́ повний сили й Госпо́днього Духа, і правди й відваги, щоб представити Якову про́гріх його, а Ізраїлеві — його гріх.
Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu, ndi Mzimu wa Yehova, ndi kulungama, ndi kulimba mtima, kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo, kwa Israeli za tchimo lake.
9 Почуйте ж це, го́лови дому Якового та начальники дому Ізраїля, які не́хтують справедливість, а все про́сте викри́влюють,
Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli, inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama; ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
10 вони кров'ю будують Сіо́на, а кривдою — Єрусали́ма.
inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi, ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
11 Його го́лови судять за хабара́, і навчають за плату його ті священики, і за срі́бло воро́жать пророки його́, хоч на Господа вони опира́ються, кажучи: „Хіба не Господь серед нас? Зло не при́йде на нас!“
Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze, ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire, ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama. Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti, “Kodi Yehova sali pakati pathu? Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
12 О так, — через вас Сіон буде на поле зао́раний, а Єрусалим на руїни обе́рнеться, а гора́ храмова́ стане взгі́р'ями лісу.
Choncho chifukwa cha inu, Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.

< Михей 3 >