< Левит 22 >

1 І Господь промовляв до Мойсея, говорячи:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 „Промовляй до Аарона й до синів його, і нехай вони обере́жно поводяться зо святощами Ізраїлевих синів, які вони посвячують Мені, і нехай не безчестять Мого святого Ймення. Я — Господь!
“Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
3 Скажи їм: На ваші покоління кожен чоловік, що набли́зиться зо всякого вашого насіння до святощів, які Ізраїлеві сини посвятять Господе́ві, а нечистість його на нім, то буде винищена душа та з-перед лиця Мого. Я — Господь!
“Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
4 Кожен чоловік з Ааро́нового насіння, коли він прокаже́ний або течи́вий, не буде їсти зо святощів, аж поки очиститься. А хто доторкнеться всякого нечистого від мертвого тіла, або чоловік, що з нього вийде насіння лежа́ння,
“Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
5 або хто доторкнеться до всякого плазуна́, через якого він стане нечистий, або до людини́, через яку стане нечистий, через усяку нечистість її, —
kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
6 особа, що доторкнеться до того, то стане нечиста аж до вечора, і не буде їсти зо святощів, поки не обмиє свого тіла в воді.
Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
7 А коли за́йде сонце, то стане він чистий, а потім буде їсти зо святощів, бо це хліб його.
Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
8 Па́дла та розша́рпаного не буде він їсти, щоб не занечиститись ним. Я — Господь!
Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
9 І будуть вони стерегти́ Мої при́кази, — щоб не понести через те гріха́ на собі, і щоб не померти через нього, коли б збезче́стили їх. Я — Господь, що освячує їх!
“‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
10 А кожен чужий не буде їсти святощів; осілий у священика й на́ймит не будуть їсти святощів.
“‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
11 А коли священик купить чоловіка, — купівля срібла його це, — той буде їсти їх, також уро́джений дому його, — вони будуть їсти його хліб.
Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
12 А священикова дочка́, коли буде видана чужому чоловікові, вона не буде їсти принесених святощів.
Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
13 А священикова дочка́, коли буде вдова, або розве́дена, а дітей не має, і ве́рнеться до дому свого батька, — як за мо́лодости своєї, буде їсти з хліба ба́тька свого. А кожен чужий не буде їсти його.
Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
14 А чоловік, коли з'їсть святощі через по́милку, то докладе до неї п'яту частину її, і віддасть священикові ті святощі,
“‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
15 і священики не збезчестять святощів Ізра́їлевих синів, що вони приносять Господе́ві,
Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
16 і не стягнуть на себе вини за провину їдження своїх святощів. Бо Я — Господь, що освячує їх“.
ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
17 I промовляв Господь до Мойсея, говорячи:
Yehova anawuza Mose kuti,
18 „Промовляй до Ааро́на й до синів його, та до всіх Ізраїлевих синів, і скажеш їм: Кожен чоловік з Ізраїлевого дому та з прихо́дька між Ізраїлем, що принесе свою жертву за всякими своїми обі́тницями та за всякими дарува́ннями своїми, що принесе Господе́ві на цілопа́лення,
“Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
19 то нехай принесе на вподобання ваше безвадного самця́ з худоби великої, з овець і з кіз.
ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
20 Жодного, що в нім вада, не принесете, бо не буде воно на вподо́бання вас.
Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
21 А чоловік, коли принесе Господе́ві мирну жертву на виразно ви́словлену обі́тницю або на дарунок, із худоби великої чи з худоби дрібної, — безвадна буде на вподо́бання, жодна вада не буде в ній:
Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
22 сліпа, або зла́мана, або скалічена, або шолуди́ва, або коро́стява, або паршива, — не принесете тих Господеві, і жертви огняно́ї не дасте з них на жертівника для Господа.
Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
23 А вола та вівцю з занадто довгим чи занадто коротким яким членом добровільно принесеш у жертву, а на обі́тницю вони не вгодні Богові.
Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
24 А того, що має ядра розчавлені, чи збиті, чи відірвані, чи відрізані, — не піднесете Господе́ві, і в вашому Кра́ї не зробите того.
Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
25 І з руки чужи́нця не принесете хліба нашого Бога зо всіх таких, бо в них зіпсуття їх, вада в них, — вони не будуть вгодні для вас“.
Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
26 І Господь промовляв до Мойсея, говорячи:
Yehova anawuza Mose kuti,
27 „Віл, або вівця, або коза, коли вродиться, то буде сім день під своєю матір'ю, а від дня во́сьмого й далі буде вгодне на жертву огняну́ для Господа.
“Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
28 А корови та вівці, — її й маля́ її не заріжете одно́го дня.
Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
29 А коли будете прино́сити вдячну жертву для Господа, то приносьте так, щоб вона була вгодна.
“Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
30 Того дня буде вона з'їджена, — не зоставите з неї аж до ра́нку. Я — Господь!
Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
31 І заповіді Мої будете додержувати, і будете виконувати їх. Я — Господь!
“Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
32 І не будете безчестити Мого святого Ймення, і Я буду освячений серед Ізраїлевих синів. Я — Господь, що освячує вас,
Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
33 що вивів вас із єгипетського кра́ю, щоб бути вашим Богом. Я — Господь!“
ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”

< Левит 22 >