< Книга Суддів 21 >
1 І присягнув Ізра́їльтянин в Міцпі, говорячи: „Жоден із нас не дасть своєї дочки́ Веніяминові за жінку!“
Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
2 І посхо́дився народ до Бет-Елу, та й сидів там аж до вечора перед Божим лицем. І підне́сли вони го́лос свій, та й плакали плаче́м великим.
Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
3 I сказали вони: „Чому, Господи, Боже Ізраїлів, сталося це між Ізраїлем, щоб сьогодні бракувало з Ізраїля одне пле́м'я?“
Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
4 І сталося назавтра, і встав рано наро́д, та й збудували же́ртівника, і прине́сли цілопа́лення та мирні жертви.
Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
5 І сказали Ізраїлеві сини: „Хто зо всіх Ізраїлевих племен не ввійшов до зборів до Господа? Бо та прися́га була велика на того, хто не прийшов до Господа, до Міцпи, говорячи: „ Такий буде конче забитий“.
Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
6 І жалували Ізраїлеві сини за Веніямином, своїм братом, та й сказали: „Сьогодні відру́бане з Ізраїля одне пле́м'я!
Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
7 Що́ ми зробимо їм, позосталим, щодо жіно́к? А ми присягнули Господом, що не дамо їм із дочо́к наших за жіно́к“.
Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
8 І сказали вони: „Яке́ одне́ з Ізраїлевих племен не прийшло́ до Господа до Міцпи?“Аж ось ви́явилось, що з Явешу ґілеадського ніхто не прихо́див до табо́ру на збори.
Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
9 І був переглянений народ, а оце — не було там нікого з ме́шканців Явешу ґілеадського!
Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
10 І послала громада туди дванадцять тисяч чоловіка хоробрих людей, і наказали їм, говорячи: „Ідіть, і повбиваєте ме́шканців ґілеадського Явешу вістрям меча, — і жінок і дітей.
Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
11 А це та річ, що ви зробите: Кожного чоловіка та кожну ланку, що пізна́ла чолові́ка, зробите закляттям“.
Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
12 І знайшли вони з ме́шканців ґілеадського Явешу чотири сотні дівчат паннів, що не пізна́ли чолові́ка, і спровадили їх до табо́ру в Шіло́, що в ханаанському Кра́ї.
Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
13 І послала вся та громада, а ті говорили до Веніяминових синів, що в Села-Ріммоні, та й кликнули їм: „Мир!“
Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
14 І вернувся Веніямин того ча́су, і дали́ їм тих жінок, яких позоставили при житті, із жінок ґілеадського Явешу. Та не знайшли їм до́сить.
Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
15 А народ той жалував за Веніямином, бо Господь зробив проло́ма в Ізраїлевих племенах.
Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
16 І сказали старші́ громади: „Що́ ми зробимо позосталим щодо жінок? Бо вигублена жінка з Веніямина“.
Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
17 І сказали вони: „Останки насліддя — для Веніямина, і не буде витерте пле́м'я з Ізраїля.
Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
18 А ми не можемо дати їм жінок із наших дочо́к, бо Ізраїлеві сини присягли́, говорячи: „Прокля́тий, хто дає жінку Веніяминові!“
Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
19 І сказали вони: „Ось буває рік-у-рік свято Господнє в Шіло́, що на північ від Бет-Елу, на схід сонця від дороги, що провадить з Бет-Елу до Сихему, і з пі́вдня від Левони“.
Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
20 І наказали вони Веніяминовим синам, говорячи: „Ідіть, і будете чатува́ти в виноградниках.
Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
21 І побачите, аж ось до́чки Шіла́ вийдуть танцювати та́нці, то ви вийдете з виноградників, та й схо́пите собі кожен свою жінку з дочо́к Шіла́, і пі́дете в Веніяминів край.
ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
22 І буде, коли їхні батьки або їхні брати при́йдуть до нас сваритися, то ми скажемо їм: Змилуйтеся над ними, бо не взяли́ ми для кожного з них жінку на війні, і ви не дали́ їм, тому цього ча́су ви винні“.
Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
23 І зробили так Веніяминові сини, і взяли жінок за числом своїм із тих, що танцювали, що їх вони викрали. І пішли вони, і вернулися до наді́лу свого, і побудували міста́, та й осілися в них.
Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
24 І порозхо́дилися звідти Ізраїлеві сини того ча́су кожен до племени свого та до роду свого, і пішли звідти кожен до спа́дку свого.
Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
25 Того ча́су не було царя в Ізраїлі, — кожен робив, що здавалося правдивим в його оча́х!
Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.