< Йоїл 2 >

1 Засурмі́ть на Сіоні в сурму́, здійміть крик на святій горі Моїй! Затремтіть, всі мешка́нці землі, бо прийшов день Госпо́дній, бо бли́зько вже він,
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 день темно́ти та те́мряви, день хмари й імли́! Як несеться досві́тня зоря́ по гора́х, так наро́д цей великий й міцни́й. Такого, як він, не бувало відві́ку, і по ньому не бу́де вже більш аж до літ з роду в рід!
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Перед ним пожира́є огонь, і палахкоти́ть за ним по́лум'я! Земля перед ним, як еде́нський садо́к, а за ним — опусті́ла пустиня, і ряту́нку від нього нема!
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Його ви́гляд — ніби коні, гарцю́ють вони, наче ті верхівці́!
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Як гу́ркіт військо́вих возі́в, вони ска́чуть гірськи́ми верхі́в'ями, як ве́реск огни́стого по́лум'я, що солому жере́, наче поту́жний наро́д, що до бо́ю поста́влений.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Наро́ди тремтять перед ним, всі обличчя поблі́дли.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Як ли́царі, мчаться вони, немов вояки́ вибігають на мур, і кожен своєю доро́гою йдуть, і з стежо́к своїх не позбива́ються, —
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 не пхають вони один о́дного, ходять своєю дорогою битою, а коли на списа́ упаду́ть, то не зра́няться.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 По місті хурча́ть, по мурі біжать, увіхо́дять в доми́, через ві́кна прола́зять, як зло́дій.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 Трясеться земля перед ним, тремтить небо, сонце та місяць темні́ють, а зорі загу́блюють ся́йво своє.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 I голос Свій видасть Госпо́дь перед ві́йськом Своїм, бо та́бір Його величе́зний, бо міцни́й викона́вець сло́ва Його, бо великий день Господа й ве́льми страшни́й, і хто зможе його перене́сти?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 Тому́ то тепер промовляє Госпо́дь: Верніться до Мене всім серцем своїм, і по́стом святим, і плаче́м та рида́нням!
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 І деріть своє серце, а не свою одіж, і наверні́ться до Господа, вашого Бога, бо ласка́вий Він та милосе́рдний, довготерпели́вий та многомилости́вий, і жалку́є за зло!
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Хто знає, чи Він не пове́рнеться та не пожа́лує, і по Собі не зали́шить благослове́ння, жертву хлі́бну та жертву ту литу для Господа, вашого Бога.
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Засурмі́ть на Сіоні в сурму́, оголосіть святий піст, скличте зібра́ння!
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Зберіте наро́д, оголосіть святі збо́ри, ста́рців згрома́дьте, позбирайте дітей та грудни́х немовля́т, нехай вийде з кімна́ти своєї тако́ж молодий, молода́ ж з-під свого накриття́!
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Між притво́ром та же́ртівником нехай плачуть священики, слу́ги Господні, хай мо́лять вони: Змилуйся, Господи, над наро́дом Своїм, і не видай на га́ньбу спадку Свого, щоб над ним панували пога́ни. Нащо будуть казати між наро́дами: Де́ їхній Бог?
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 І за́здрісним стане Госпо́дь за Свій край, і зми́лується над наро́дом Своїм“.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 І Господь відповів і сказав до наро́ду Свого: „Ось Я посилаю вам збіжжя й вино молоде та оливу, і наси́титесь нею, і більше не дам вас на нару́гу наро́дам.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 А цьо́го півні́чного ворога віддалю́ Я від вас, і його в край сухий та спусто́шений ви́жену, — його пе́ред до схі́днього моря, його ж край — до того́ моря за́днього. І вийде злий за́пах його, і піді́йметься смо́рід його, бо він лихо велике чинив.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Не бійся ти, зе́мле, а тішся й радій, — бо велике Господь учинив!
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Не бійтеся, ти пі́льна худо́бо, бо пустинні пасо́виська зазелені́ють, бо дерево видасть свій плід, фіґо́вниця та виноград свою силу дадуть.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 А ви, сіонські сини, радійте та тіштеся Го́сподом, Богом своїм, бо вам ї́жі Він дасть на спасі́ння, і найперше зішле вам дощу́, дощу ра́ннього й пі́знього.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 І то́ки напо́вняться збіжжям, чави́льні ж кадки́ будуть перелива́тись вином молодим та оливою.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 І надолу́жу Я вам за ті роки, що поже́рла була сарана́, коник і черва́ та гусінь, Моє ві́йсько велике, що Я посилав проти вас.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 А їсти — ви будете їсти й наси́чуватись, і хвалитимете Ім'я́ Господа, вашого Бога, що з вами на по́див зробив, і посоро́млений більше не буде наро́д Мій навіки!
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 І пізна́єте ви, що Я серед Ізраїля, і що Я — Господь, Бог ваш, і немає вже іншого, — і посоро́млений більше не буде наро́д Мій навіки!
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 І бу́де потому, — виллю Я Духа Свого на кожне тіло, і пророкува́тимуть ваші сини́ й ваші до́чки, а вашим стари́м будуть сни́тися сни, юнаки́ ваші бачити будуть виді́ння.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 І також на рабів та невільниць за тих днів виллю Духа Свого́.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 І дам Я озна́ки на небі й землі, — кров та огонь, та стовпи́ диму.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Замі́ниться сонце на те́мність, а місяць — на кров перед прихо́дом Господнього дня, великого та страшно́го!
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 І станеться, — кожен, хто кли́кати буде Господнє Ім'я́, той спасеться, бо на Сіонській горі та в Єрусалимі буде спасі́ння, як Госпо́дь говорив, та для тих позоста́лих, що Господь їх покличе.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< Йоїл 2 >