< Єремія 49 >

1 На Аммонових синів. „Так говорить Господь: Чи немає синів у Ізраїля? Чи немає спадкоє́мця в нього? Чому Ґада Мілком одіди́чив й осівся наро́д його по містах його?
Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
2 Тому́ настаю́ть ось дні, — говорить Господь, — і Я розголошу́ крик військо́вий на Раббу Аммонових синів, — і вона стане за купу руїн, а підлеглі міста її спа́лені будуть огнем, і знов одіди́чить Ізраїль спа́док сві́й, говорить Господь.
Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
3 Ридай, о Хешбо́не, бо місто зруйноване! Кричіть, до́чки Рабби, опережі́ться вере́тою, лементу́йте й блукайте по обійстя́х, бо Мілком до поло́ну іде, його священики й його зверхники ра́зом!
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
4 Чого ти долинами хва́лишся? Долина твоя розпливається кров'ю, о до́чко невірна, що на скарби свої покладаєш надію та кажеш: „Хто при́йде до мене?“
Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
5 Ось Я страх припрова́джу на тебе, — говорить Господь, Бог Саваот, — із усього довкі́лля твого, і ви повтікаєте кожен напе́ред себе, — і не буде кому втікачів позбира́ти!
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
6 А потім верну́ Я долю Аммонових синів, говорить Господь“.
“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
7 На Едома. „Так говорить Господь Саваот: Чи в Темані немає вже мудрости? Чи згинула рада розумних? Хіба зіпсувалась їхня мудрість?
Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
8 Утікайте, оберні́ться плечи́ма, сядьте глибше, мешка́нці Дедану, бо привів Я нещастя Ісава на нього, — той час, коли покараю його!
Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
9 Якщо при́йдуть до тебе збирачі́ винограду, вони не полишать останків, якщо ж при́йдуть злоді́ї вночі, напсую́ть, скільки схо́чуть.
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Бо обнажи́в Я Ісава, повідкривав усі криївки його, і він сховатись не зможе, — спусто́шене буде насіння його, й його браття, і сусіди його, — і не буде його!
Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
11 Залиши́ свої си́роти, — Я утри́маю їх при житті, а вдови твої хай наді́ю на Мене кладу́ть!
‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
12 Бо так промовляє Господь: Ось і ті, що не мали б пити чаші ціє́ї, пити будуть напе́вне, а ти непока́раним будеш? Не будеш без кари, бо справді ти пи́тимеш чашу!
Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
13 Бо Собою присяг Я, — говорить Господь, — що Боцра́ за спусто́шення стане, за га́ньбу, пустиню й прокляття, і руїнами вічними стануть міста́ її всі!
Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
14 Я звістку від Господа чув, і відправлений ві́сник між люди: Зберіться й прийдіть проти неї, і встаньте на бій,
Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
15 бо тебе Я зробив ось мали́м між наро́дами, погордженим серед людей!
“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Страхіття твоє обманило тебе й гордість серця твого, тебе, що в розщі́линах скелі живеш, що високих підгі́рків тримаєшся. Та коли б ти кубло́ своє й ви́соко звив, мов орел, то й ізвідти Я скину тебе, промовляє Господь.
Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
17 І стане Едо́м за страхі́ття, — кожен, хто буде прохо́дити ним, остовпі́є й засвище, як пора́зи його всі побачить.
“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Як Содо́м та Гомо́рру й сусідів її поруйно́вано, каже Господь, — так ніхто там не буде сидіти, і не буде в нім ме́шкати чужи́нцем син лю́дський.
Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
19 Ось піді́йметься він, немов лев, із темного лісу Йорда́ну на во́дяні луки, і Я вмент зроблю́, що він побіжить геть від них, а хто ви́браний буде, того Я поставлю над ними. Бо хто є подібний Мені, і хто покличе Мене перед суд, і хто па́стир такий, що перед обличчям Моїм устоїть?
“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Тому то послухайте за́дум Господній, що Він на Едома заду́мав, і думки́ Його ті, які Він на мешка́нців Теману замислив: Направду, — найменших з отари потя́гнуть, і попусто́шать пасо́висько їхнє при них!
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Від гуку упадку їхнього буде тремтіти земля, буде зойк, аж на морі Червоному чути їхній голос.
Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Ось піді́йметься він, як орел, і літатиме, й крила свої над Боцро́ю розго́рне: і стане серце хоробрих едо́млян в той день, немов серце жони-породі́ллі“.
Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
23 На Дамаск. „Засоро́мивсь Хамаш та Арпал, бо злу звістку почули; в неспоко́ї тривожнім вони, як те море, що не може вспоко́їтись.
Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Дама́ск сторопі́в, обернувся втікати, і страх його міцно охопи́в, біль та му́ки його обгорну́ли, немов породі́ллю.
Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Як спорожні́ло славне це місто, місто вті́хи Моєї!
Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Тому́ юнаки́ його падати будуть на пло́щах його, і всі військо́ві погинуть того дня, говорить Господь Саваот.
Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 І під муром Дама́ску огонь запалю́, і він пожере Бен-Гада́дські пала́ци!“
“Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 На Кедар та на царства Хацору, що їх побив Навуходоносор, цар вавилонський. „Так говорить Господь: Уставайте, ідіть на Кеда́р, і нехай попусто́шать війська́ синів сходу!
Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Заберуть їхні наме́ти та їхню отару, їхні покро́ви та всі їхні речі, та їхніх верблю́дів собі заберуть, і над ними кричатимуть: Жах звідусі́ль!
Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 Утікайте, мандруйте скоріш, сховайтесь в глибоке, мешка́нці Хацору, — говорить Господь, — бо раду нарадив на вас Навуходоно́сор, цар вавилонський, і за́дум заду́мав на вас!
“Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 Уставайте, ідіть на наро́д, що спокійно, безпечно живе, — промовляє Господь, — немає воріт, і нема в нього за́сувів, самітно живуть.
“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 І стануть верблю́ди їхні здо́биччю, а їхні череда́ — грабеже́м, і на всі ві́три розвію Я їх, хто воло́сся довко́ла стриже, і зо всіх їхніх сторін припрова́джу на них їхню поги́біль, говорить Господь.
Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 І стане Хацо́р за мешка́ння шака́лів, за вічне спусто́шення, — не заме́шкає там люди́на, і син лю́дський не спи́ниться в ньо́му!“
“Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 Слово Господнє, що було пророкові Єремії на Елам на початку царюва́ння Седекії, Юдиного царя, таке:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 „Так говорить Госпо́дь Савао́т: Ось Я злама́ю ела́мського лука, головну́ їхню силу!
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 І з чотирьо́х кінців неба спрова́джу чотири вітри́ до Еламу, і їх розпоро́шу на всі ці вітри́, і не бу́де такого наро́ду, куди б не прийшли ці вигна́нці з Ела́му.
Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 І настра́шу Ела́м перед їхніми ворога́ми та перед всіма́, хто їхню душу шукає, і лихо на них наведу́, лютість гніву Мого, говорить Господь, — і пошлю́ Я за ними меча, аж поки не ви́гублю їх!
A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 І поставлю Престо́ла Свого в Еламі, і ви́гублю звідти царя й його зверхників, каже Господь.
Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 Але бу́де напри́кінці днів, поверну́ Я Ела́мові долю, говорить Господь“.
“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.

< Єремія 49 >