< Єремія 33 >
1 І було Єремії Господнє слово вдру́ге, коли він ще за́мкнений був на подвір'ї в'язни́ці, говорячи:
Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
2 „Так говорить Господь, що чинить оце, Господь, що вформо́вує це, щоб поставити міцно оце, — Господь Його Йме́ння:
“Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
3 Покли́куй до Мене — і тобі відпові́м, і тобі розповім про велике та незрозуміле, чого ти не знаєш!
‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
4 Бо так промовляє Господь, Бог Ізраїлів, про доми́ цього міста й про доми́ царів Юди, що їх поруйновано на оборо́нні вали́, —
Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
5 приходять вони воювати з халдеями, щоб доми́ понапо́внювати лю́дськими тру́пами, що вра́зив Я гнівом Своїм та люттю Своєю, і сховав Я від міста оцього обличчя Своє за все їхнє зло:
Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
6 Ось Я йому ви́рощу шкурку на рані, й дам ліки, та їх уздоро́влю, і відкрию багатство споко́ю та правди для них!
“‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
7 І Я поверну́ долю Юди, і долю Ізраїля, і їх розбудую, немов напоча́тку.
Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
8 І очищу Я їх з їхньої провини всілякої, що нагріши́ли Мені, і проба́чу всі їхні провини, яки́ми нагрішили Мені, та відпа́ли від Мене.
Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
9 І Єрусалим Мені стане за радісне йме́ння, за хвалу́ та пишно́ту всім лю́дям землі, що почують про все те добро́, що зробив Я для них! І вони полякаються та затремтя́ть через все те добро та ввесь спо́кій, який Я для нього вчинив!
Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
10 Так говорить Господь: Ще буде почутий на місці оцьо́му, — про яке ви говорите: „Воно поруйноване, так що немає люди́ни й немає скотини“, — у містах Юди й на вулицях Єрусалиму, спусто́шених так, що немає люди́ни, й немає мешка́нця, й немає скотини, —
“Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
11 радісний голос та голос веселий, голос молодого та голос молодої, голос тих, що говорять: „Хваліть Господа Саваота, бо добрий Господь, бо навіки Його́ милосердя!“що жертву хвали́ до Господнього дому приносять, бо Я поверну́ долю Кра́ю цього, як було напоча́тку, говорить Господь!
mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
12 Так говорить Господь Саваот: Ще буде на місці оцьо́му спусто́шеному, що немає нічого воно від люди́ни та аж до скотини, та по містах його всіх — ще буде пасо́висько для пастухів, куди приведу́ть вони че́реду на відпочи́нок!
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
13 У містах у горі́шніх, у містах до́лішніх, і в півде́нних містах, і в Веніяминовому кра́ї, і в околицях Єрусалиму, і в містах Юдиних ще прохо́дитиме череда через руки рахуючого, говорить Господь!
Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
14 Ось дні настаю́ть, — говорить Господь, — і Я ви́повню добре те слово, що Я провіща́в про Ізраїлів дім і про дім Юдин:
“‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
15 тими дня́ми та ча́су того́ Я Давидові зрощу́ Пагінця́ справедливости, — Він буде чини́ти на землі правосуддя та правду!
“‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 Юда буде спасе́ний в тих днях, а Єрусалим буде жити безпечно, і його будуть кликати так: „Господь — наша правда!“
Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
17 Бо так промовляє Господь: Нема перево́ду Давидовим му́жам, що мають сидіти на троні дому Ізраїлевого,
Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
18 і нема перево́ду в Левитів — священиків перед обличчям Моїм тому му́жеві, що буде прино́сити цілопа́лення, і спалювати хлібну жертву, і прино́сити жертву всі дні!“
ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
19 І було слово Господа до Єремії таке:
Yehova anawuza Yeremiya kuti:
20 „Так говорить Господь: Якщо знищите ви заповіта Мого щодо дня та Мого заповіта щодо ночі, щоб не було́ дня та ночі в їхньому ча́сі,
Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
21 то знищений буде також заповіт Мій з Давидом, рабом Моїм, щоб він сина не мав, який не царював би на троні його, і з Левитами-священиками, слугами Моїми!
Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
22 І як незчисле́нні ті зо́рі небесні, а мо́рський пісок незміре́нний, так помно́жу насіння Давида, Мого раба, та Левитів, що служать Мені!“
Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
23 І було слово Господа до Єремії таке:
Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
24 „Хіба ж ти не завва́жив, як наро́д цей казав був, говорячи: „Оби́два ті ро́ди, яких Господь вибрав, відкинув Він їх?“І наро́дом Моїм вони не́хтують, наче б не був він уже перед ними наро́дом.
“Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
25 Так говорить Господь: Якщо заповіта Мого щодо дня та щодо ночі нема, якщо Я уставів для неба й землі не поклав,
‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
26 то відки́ну й насіння Якова та раба Мого Давида, щоб не брати володарі́в із насіння його для насіння Авраама, Ісака та Якова. Та не буде того, — бо верну́ їхню долю, й помилую їх!“
monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”