< Єремія 3 >
1 І було мені слово Господнє, гово́рячи: „Як відпу́стить хто жінку свою, й вона пі́де від нього, та стане за жінку для іншого чоловіка, — чи ве́рнеться ще він до неї? Чи ж не стане зовсі́м обезче́щеною оця жінка? Ти ж пере́люб чинила з коха́нцями багатьома́, і тобі поверта́тись до Мене? говорить Господь.
“Ngati munthu asudzula mkazi wake ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina, kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo? Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri? Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri. Komabe bwerera kwa ine,” akutero Yehova.
2 Зведи́ свої очі на го́ри порожні й дивися, — де пере́любу ти не чинила? Ти для них по доро́гах сиділа, немов той араб на пустині, — і збезче́стився край твоїм блу́дом та лихом твоїм!
“Tayangʼana ku zitunda zowuma. Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama? Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu. Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu ndi ntchito zanu zoyipa.
3 І дощі були стри́мувані, і не було́ дощу пі́знього, проте мала ти чо́ло блудни́ці, і стратила сором,
Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula, ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe. Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere; ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.
4 Чи ж кли́кати відни́ні не бу́деш до Мене: „Отче мій, Ти юна́цтва мого Провідни́к!
Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,
5 Чи Він пам'ята́тиме вічно про гнів, чи наза́вжди його стерегти́ме?“Таке ти говориш, і безме́жно зло чиниш.
kodi mudzandikwiyira nthawi zonse? Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’ Umu ndimo mmene umayankhulira, koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”
6 І сказав до мене Господь за днів царя Йосії: „Чи ти бачив, що зробила невірна дочка́ Ізраїлева? Вона ходила на кожну високу го́ру, і під кожне зелене дерево, — і блудоді́яла там.
Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko.
7 Я думав: Як зро́бить вона все оце, то до Мене пове́рнеться; та вона не верну́лась, і бачила це сестра її зра́дниця, Юдея.
Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi.
8 І побачила Юдея, що за все те, що пере́люб чинила невірна дочка Ізраїлева, відпустив Я її, і дав їй листа розводо́вого. Та зрадли́ва сестра її, дочка Юдина, не побоялася й пішла, і блудли́вою стала й вона.
Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo.
9 І сталось від ро́зголосу про пере́люб її, збезче́стила вона землю, і пере́люб чинила з камі́нням та з деревом.
Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo.
10 І також при всьому цьому не вернулась до Мене зрадли́ва сестра її, дочка Юди, усім своїм серцем, а тільки вдава́ла, говорить Господь“.
Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.
11 І промовив до мене Господь: „Невірна дочка́ Ізраїлева всправедли́вила душу свою більш від зрадли́вої дочки Юди.
Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda.
12 Піди, і проголо́сиш слова ці на пі́вніч та й скажеш: Вернися, відсту́пна дочко Ізраїлева! говорить Госпо́дь. Не зверну́ Я Свого обличчя у гніві на вас, бо Я милости́вий, — говорить Госпо́дь, і не бу́ду повік стерегти́ Свого гніву.
Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti, “‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale, pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.
13 Тільки пізнай же прови́ну свою́, бо ти проти Господа, Бога свого повстала, і грішила з чужими під деревом кожним зеленим, і Мого голосу ви не почули, говорить Господь.
Ungovomera kulakwa kwako kuti unawukira Yehova Mulungu wako. Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo pansi pa mtengo uliwonse wogudira, ndiponso kuti sunandimvere,’” akutero Yehova.
14 Верніться, діти невірні, говорить Господь, бо Я вам Госпо́дар, та візьму́ вас по о́дному з міста, а з роду по два, і вас поведу́ до Сіону!
“Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse.
15 І дам па́стирів вам згідно з серцем Своїм, і вони будуть па́сти вас умі́нням та ро́зумом.
Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha.
16 І буде, коли ви розмно́житеся та розпло́дитеся на землі за цих днів, — говорить Госпо́дь, — не скажуть уже: „ковче́г заповіту Господнього“, і він вже не при́йде на серце, і його пам'ятати не бу́дуть, і більше не буде він зро́блений.
Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,” akutero Yehova.
17 Того ча́су назвуть Єрусалима: Господній престо́л, і до нього, до Єрусалиму згрома́джені будуть наро́ди усі ради Йме́ння Господнього, і більше не пі́дуть вони за впертістю серця лихого свого́,
Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa.
18 Тими днями дім Юдин із домом Ізраїля пі́дуть і ра́зом прибу́дуть з півні́чного кра́ю до кра́ю, що вашим батькам на спа́док Я дав.
Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.
19 І Я був поду́мав: як поставлю тебе Я посе́ред синів і дам тобі край пожада́ний, найкращу спа́дщину народів? І Я ду́мав: ви будете звати Мене: „Мій Отче“, і не відве́рнетеся ви від Мене.
“Ine mwini ndinati, “‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga ndikukupatsani dziko labwino kwambiri, cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’ Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’ ndi kuti simudzaleka kunditsata.
20 Справді, як зраджує жінка свого чоловіка, так ви Мене зра́дили, доме Ізраїлів! каже Господь.
Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake, momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,” akutero Yehova.
21 Чути голос на ли́сих гора́х, плач блага́льний синів Ізраїлевих, вони бо скривили доро́гу свою, забули про Господа, Бога свого́:
Mawu akumveka pa magomo, Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo chifukwa anatsata njira zoyipa ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.
22 „Верніться, невірні сини, усі ваші відсту́пства Я ви́лікую!“„Ось прийшли ми до Тебе, бо Ти Господь, Бог наш!
Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika; ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.” “Inde, tidzabwerera kwa Inu pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
23 Справді, неправда ті па́гірки, той го́мін на го́рах, — справді, в Господі, Богові нашім, спасі́ння Ізраїлеве!
Ndithu kupembedza pa magomo komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu. Zoonadi chipulumutso cha Israeli chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
24 А той сором пожер працю наших батьків від нашої мо́лодости, їхню худобу дрібну́ й їхню худобу велику, синів їхніх та їхніх дочо́к.
Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu la ntchito za makolo athu, nkhosa ndi ngʼombe zawo, ana awo aamuna ndi aakazi.
25 Лежимо́ ми у со́ромі нашому, і нас покриває ця наша неслава, бо ми прогріши́лися Господу, Богові нашому, ми й батьки наші, від нашої мо́лодости й до сьогодні, і не слухали голосу Господа, нашого Бога!“
Tilekeni tigone pansi mwa manyazi, ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe. Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu, ife pamodzi ndi makolo athu kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”