< Єремія 12 >
1 Справедливий Ти, Господи, будеш, коли б я судився з Тобою, проте правува́тися буду з Тобою: чому́ то дорога безбожним щасти́ться, чому́ то спокійні всі зра́дники?
Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
2 Ти їх посадив — і вони вкорени́лись, ростуть і прино́сять плоди́. Ти близьки́й в устах їхніх, та далекий від їхніх серде́ць.
Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
3 А Ти, Господи, знаєш мене, Ти бачив мене й дослідив моє серце, що з Тобою воно. Відлучи́ їх, немов на зарі́з ту отару, і признач їх на день побиття́!
Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
4 Аж доки в жало́бі земля пробува́тиме, і со́хнути буде трава всього поля за зло її ме́шканців? Гине худо́ба та пта́ство, бо сказали вони: кінця нашого Він не побачить!
Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
5 Як ти з пі́шими бігав, і вони тебе зму́чили, то як будеш змагатися з кі́ньми? Ти в спокі́йному кра́ї безпечний, та що будеш робити в пові́дді Йорда́ну?
Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
6 Бо також твої бра́ття та дім твого ба́тька — і вони тебе зраджують, і криком кричать за тобою, — не вір їм, коли й добре тобі говори́тимуть!
Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
7 Поки́нув Я Свій дім, залиши́в спа́док Свій; миле Моєї душі Я віддав у долоню її ворогів.
“Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
8 Спа́док Мій Мені став, мов лев той у лісі, — свій голос дав проти Мене, тому́ то його Я знена́видив.
Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
9 Чи для Мене спа́док Мій, — хижий птах різноба́рвний, що хижі птахи́ позліта́лись круг нього? Ідіть, позбирайте усю польову́ звірину́, спрова́дьте, щоб же́рли!
Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
10 Числе́нні па́стирі попсува́ли Мого виноградника, потопта́ли Мій у́діл, Мій улю́блений уділ вони обернули на голу пустиню!
Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
11 Обернули його на спусто́шення, він при Мені у жало́бі, спусто́шений, увесь Край опусті́лий, — бо ніко́го нема, хто б поклав це на серце собі!
Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
12 Поприхо́дять на всі лисі гори в пустині руїнники, бо меч Господа все позжира́є від кра́ю землі й аж до кра́ю землі, миру не буде для всякого тіла!
Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
13 Пшеницю посіяли, те́рня ж пожали, наму́чилися, та не мали кори́сти. І буде вам сором за ваші плоди́ через лю́тість Господнього гніву!
Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
14 Так говорить Господь про лихих усіх сусідів моїх, що вони дотика́ються того спа́дку, що Я дав на спа́дщину наро́ду Моєму Ізраїлеві: Ось Я повирива́ю їх з їхньої землі, і вирву дім Юдин з сере́дини їхньої.
“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
15 І станеться, як Я їх повирива́ю, то верну́ся й помилую їх, і кожного з них приверну́ до спа́дщини його, і кожного до кра́ю його.
Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
16 І буде, якщо вони справді навча́ться доріг наро́ду Мого, щоб присягатися Йме́нням Моїм: „ Як живий Господь“, — як вони присягати навчили наро́д Мій Ваалом, то збудуються серед наро́ду Мого!
Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
17 А якщо не послухають, то ви́рву наро́д цей, вирива́ючи та вигубля́ючи, каже Господь!“
Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.