< Ісая 54 >
1 Веселися ж, неплі́дна, яка не родила, співа́нням утішайся й радій, що мук породі́льних не мала, бо в покиненої буде більше синів від синів заміжньо́ї, говорить Господь!
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 Пошир місце наме́ту свого́, а заві́си наме́тні поме́шкань твоїх повитяга́й, не затри́муй! Свої шнури продо́вж, а кіло́чки свої позміцня́й!
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 Бо право́руч і ліво́руч поши́ришся ти, а насіння твоє одіди́чать наро́ди, і заселять міста́ опусто́шені.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 Не бійся, бо со́рому ти не зазнаєш, і не соро́мся, бо не будеш засти́джена, бо про сором свого юна́цтва забудеш, а га́ньби уді́вства свого́ ти не будеш уже пам'ятати!
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 Бо Муж твій, Творе́ць твій, — Господь Саваот йому Йме́ння, а твій Викупи́тель — Святий Ізраїлів, — Він Богом усієї землі буде зва́ний!
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 Бо Господь був покликав тебе, як поки́нуту жінку й засму́чену духом, й як жінку юна́цтва Свого, як була ти відки́нена, каже твій Бог.
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 На хвильку малу́ Я тебе був покинув, але з милосердям великим тебе позбира́ю.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 У за́палі гніву Я сховав був обличчя Своє на хвилину від тебе, та вічною милістю зми́луюся над тобою, каже твій Викупи́тель, Госпо́дь.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 Бо для Мене оце — мов ті Но́єві во́ди: як Я присягнув був, що Но́єві во́ди не при́йдуть уже над землею, так Я присягну́в, щоб на тебе не гні́ватися й не карта́ти тебе!
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 Бо зру́шаться го́ри й холми́ захита́ються, та милість Моя не віді́йде від тебе, і заповіт Мого миру не захита́ється, каже твій милости́вець, Господь.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 Моя до́чко убога та бурею гнана, невті́шна, — ось камі́ння твої покладу́ в малахі́ті, основи ж твої закладу́ із сапфі́рів!
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 І пороблю́ із рубі́ну карні́зи твої, твої ж брами — з каміння карбу́нкула, а всю горо́жу твою — з дорогого камі́ння.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 Всі сини твої стануть за у́чнів Господніх, і спо́кій глибокий настане синам твоїм!
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Будеш міцно поста́влена праведністю, стань дале́ко від у́тиску, бо не боя́тимешся, і від стра́ху, бо до тебе не збли́зиться він.
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Коли́ хто чіпля́тися буде до тебе, то це не від Мене, хто чіпля́тися буде до те́бе, той перед тобою впаде́.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 Отож, Я створив коваля́, який дме на огонь із вугі́лля, і виро́блює збро́ю свого ремесла́; і вигу́бника теж Я створив, який нищить ту збро́ю.
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 Жодна збро́я, що зро́блена буде на тебе, не матиме у́спіху, і кожні́сінького язика́, який стане з тобою до су́ду, осудиш. Це спа́дщина Господніх рабів, а їхнє оправда́ння від Мене, говорить Госпо́дь!
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.