< Ісая 49 >

1 Почуйте Мене, острови́, і наро́ди здале́ка, і вважайте: Господь із утро́би покликав Мене, Моє Йме́ння згадав з нутра не́ньки Моєї.
Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
2 І Мої у́ста вчинив Він, як той гострий меч, заховав Мене в ті́ні Своєї руки, і Мене вчинив за добі́рну стрілу́, в Своїм сагайдаці́ заховав Він Мене.
Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
3 І до Мене прорік: Ти раб Мій, Ізраїлю, Яким Я просла́влюсь!
Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
4 І Я відповів: Надаре́мно трудивсь Я, на порожне́чу й марно́ту зужив Свою силу: Справді ж з Господом право Моє, і нагоро́да Моя з Моїм Богом.
Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
5 Тепер же промовив Господь, що Мене вформува́в Собі від живота́ за раба́, щоб наверну́ти Собі Якова, і щоб Ізраїль для Нього був зі́браний. І був Я шано́ваний в о́чах Господніх, а Мій Бог стався міццю Моєю.
Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
6 І Він сказав: Того мало, щоб був Ти Мені за раба́, щоб віднови́ти племе́на Якова, щоб вернути врято́ваних Ізраїля, але́ Я вчиню́ Тебе світлом наро́дів, щоб був Ти спасі́нням Моїм аж до кра́ю землі!
Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
7 Так говорить Господь, Відкупи́тель Ізраїлів, Святий його, до пого́рдженого на душі, до обри́дженого від людей, до раба тих воло́дарів: Побачать царі, і князі́ повстають, — і покло́няться ради Господа, що вірний, ради Святого Ізраїлевого, що ви́брав Тебе.
Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
8 Так говорить Господь: За ча́су вподо́бання Я відповів Тобі, в день спасі́ння Тобі допоміг, і стерегти́му Тебе, і дам Я Тебе заповітом наро́дові, щоб край обнови́ти, щоб поділити спа́дки спусто́шені,
Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
9 щоб в'я́зням сказати: „Вихо́дьте“, а тим, хто в темно́ті: „З'яві́ться!“При дорогах вони будуть па́стися, і по всіх ли́сих горбо́винах їхні пасови́ська.
Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
10 Не будуть голодні вони, ані спра́гнені, і не вдарить їх спе́ка, ні сонце, — бо Той, Хто їх милує, їх попрова́дить і до во́дних джере́л поведе́ їх.
Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
11 І вчиню Я всі го́ри Свої за доро́гу, і піді́ймуться биті шляхи́ Мої.
Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
12 Ось ці зда́лека при́йдуть, а ці ось із пі́вночі й з за́ходу, а ці з кра́ю Сіні́м.
Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
13 Раді́йте, небеса́, звесели́ся ти, земле, ви ж, го́ри, втіша́йтеся співом, бо Госпо́дь звесели́в Свій наро́д, і змилувався над Своїми убогими!
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
14 І сказав був Сіон: Господь кинув мене́, і Господь мій про ме́не забув.
Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
15 Чи ж жінка забу́де своє немовля́, щоб не пожаліти їй сина утроби своєї? Та коли б вони позабува́ли, то Я не забу́ду про тебе!
“Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
16 Отож на долонях Свої́х тебе ви́різьбив Я, твої мури поза́всіди передо Мною.
Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
17 Сино́ве твої поспіша́ться до тебе, а ті, хто руйнує тебе й ті, хто нищить тебе, повідхо́дять від тебе.
Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
18 Здійми свої очі навко́ло й побач: всі вони позбиралися й йдуть ось до те́бе! Як живий Я, говорить Господь: усіх їх, як оздо́бу, зодя́гнеш, та підв'я́жешся ними, немов нарече́на.
Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
19 Бо руїни твої та пустині твої, і зруйно́ваний край твій тепер справді стануть тісни́ми для ме́шканців, і будуть відда́лені ті, хто тебе руйнував.
“Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
20 Іще до вух твоїх скажуть сино́ве сирі́тства твого: Тісне́ мені місце оце, посунься для мене, й я сяду!
Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
21 І ти скажеш у серці своїм: Хто мені їх зродив, як була осиро́чена я та самі́тна, була ви́гнана та заблуди́ла? І хто ви́ховав їх? Я зоста́лась сама, а ці, — зві́дки вони?
Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
22 Так сказав Господь Бог: Ось Я підійму́ Свою руку до лю́дів, і піднесу́ до наро́дів прапора Свого́, — і позно́сять синів твоїх в па́зусі, а до́чок твоїх поприно́сять на пле́чах.
Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
23 І будуть царі за твоїх вихова́телів, а їхні цариці — за ня́ньок твоїх. Лицем до землі вони будуть вклоня́тись тобі та лиза́тимуть пил твоїх ніг, і ти пізна́єш, що Я — то Господь, що не посоро́мляться ті, хто на Мене наді́ється!
Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
24 Чи ж від сильного буде відня́та здобич, і чи награ́боване ґвалтівнико́м урято́ване буде?
Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
25 Бо Господь каже так: Полонені віді́брані будуть від сильного, і врято́вана буде здобич наси́льника, і Я стану на прю із твоїми супере́чниками, синів же твоїх Я спасу́.
Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
26 І Я зму́шу твоїх гноби́телів їсти тіло своє, і вони повпива́ються власною кров'ю, немов би вином молоди́м. І пізнає тоді кожне тіло, що Я — то Госпо́дь, твій Спаситель та твій Відкупи́тель, Поту́жний Яковів!
Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”

< Ісая 49 >