< Ісая 46 >
1 Бел упав на коліна, зігнувся Нево́, — стали і́доли їхні для звіри́ни й худоби. Те, що колись ви носили, накладене, мов той тяга́р на худобу пому́чену.
Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
2 Зігнулися й ра́зом упали вони на коліна; не могли врятува́ти тягара́, і самі до поло́ну пішли.
Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
3 Почуйте Мене, доме Яковів, та ввесь за́лишку дому Ізраїлевого, яких від живота Я підняв, носив від утро́би,
Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
4 і Я буду Той Самий до ста́рости вашої, і до сивини вас носи́тиму, Я вчинив, і Я буду носити, й Я дви́гатиму й поряту́ю!
Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
5 До ко́го Мене ви вподо́бите та прирівня́єте, до кого подібним Мене́ ви учините, щоб схожому бути?
“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
6 Ті, що золото сиплють з киси́, срібло ж важать вагою, вина́ймлюють золотаря́, щоб із того їм бога зробив, і перед ним вони падають та поклоня́ються,
Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
7 носять його на плечі́, підіймають його, і ставлять його на місці його. І стоїть, і з місця свого́ він не рухається; коли ж хто до нього кричить, то він не відпові́сть, і не врятує його від недолі.
Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
8 Пам'ятайте про це та змужні́йте, візьміть це на розум, прови́нники!
“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
9 Пам'ятайте про давнє, відвічне, бо Я Бог, і немає більш Бога, й ніко́го, як Я,
Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
10 що звіщаю кінець від поча́тку, і напере́д — що не сталося ще, і що говорю́: „Мій за́мір відбу́деться, і всяке жада́ння Своє Я вчиню́“,
Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 що хижого пта́ха зо схо́ду прикли́кую, з кра́ю далекого мужа Своєї поради! Так, Я сказав — те й спрова́джу, що Я задумав був — теє зроблю́!
Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Почуйте Мене, твердосе́рді, далекі від справедливости!
Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 Я Свою справедливість набли́зив, — вона недале́ко, а спасі́ння Моє не припі́зниться, і дам на Сіоні спасі́ння, дам Ізраїлеві Свою ве́лич!
Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.