< Ісая 45 >

1 Так говорить Госпо́дь до Свого пома́занця Кіра: Я мі́цно тримаю тебе за прави́цю, щоб перед обличчям твоїм повали́ти наро́ди, і з сте́гон царів розв'яжу́ пояси́, щоб відчини́ти двері перед тобою, а брами не будуть зами́кані.
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 Я перед тобою піду́ й повирі́внюю ви́сунене, двері мідні злама́ю і порозбива́ю залізні засуви.
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 І дам тобі ска́рби, що в те́мряві, та бага́тства захо́вані, щоб пізнав ти, що Я — то Господь, Який кличе тебе за йме́нням твоїм, Бог Ізраїлів,
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 ради раба Мого Якова й ради вибра́нця Мого Ізраїля, і кличу тебе твоїм іме́нням, тебе називаю, хоч ти не знаєш Мене.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 Я — Господь, і нема вже ніко́го, нема іншого Бога, крім Ме́не. Я тебе підпері́зую, хоч ти не знаєш Мене,
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 щоб дізна́лися зо сходу сонця й з заходу, що крім Мене немає нічо́го; Я — Господь, і нема вже ніко́го,
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Я, що світло форму́ю та те́мність творю́, чиню мир і недолю творю́, Я — Господь, Який робить це все!
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Спустіть ро́су згори́, небеса́, а із хмар хай спливе́ справедливість! Хай земля відкрива́ється, і хай поро́дить спасі́ння та правду, хай ра́зом ростуть! Я, Господь, це вчинив!
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Горе тому́, хто з Творце́м своїм сва́риться, черепо́к із земни́х черепкі́в! Чи глина повість ганчаре́ві своєму: „Що робиш?“а ді́ло його: „Ти без рук!“
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Горе тому́, хто патя́кає ба́тькові: „Пощо ти пло́диш?“а жі́нці: „Пощо ти родиш?“
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Так говорить Господь, Святий Ізраїлів, і Той, Хто його вформува́в: „Питайте Мене про майбу́тнє, а долю синів Моїх й чин Моїх рук позоста́вте Мені!“
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 Я землю вчини́в і створи́в люди́ну на ній, небеса́ Я руками Своїми простя́г і про їхні зо́рі звелів.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 Я збуди́в його в правді, і зрівня́ю йому всі доро́ги. Він місто Моє побуду́є і відпу́стить вигна́нців Моїх не за ви́куп і не за дару́нка, — говорить Госпо́дь Савао́т.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Так говорить Господь: Пра́ця Єгипту й торгі́вля Етіопії та високі севаїтяни пере́йдуть до тебе та бу́дуть твої. Пі́дуть вони за тобою, у кайда́нах пере́йдуть, і будуть вклоня́тись тобі та блага́ти тебе́: „Тільки в те́бе є Бог, і нема більш, нема іншого Бога!“
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Справді Ти Бог таємни́чий, Бог Ізраїлів, Спаси́тель!
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 Всі вони засоро́мляться й зні́яковіють, майстрі і́долів пі́дуть у соромі ра́зом,
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 Ізраїль же буде спасе́ний від Господа вічним спасі́нням: не будете ви засоро́млені ані знесла́влені аж на вічні віки́!
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 Бо так промовляє Господь, Творець неба. Він той Бог, що землю вформува́в та її вчини́в, і міцно поставив її; не як порожне́чу її створи́в, — на прожива́ння на ній Він її вформува́в. Я — Господь, і нема більше іншого Бога!
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Я не говорив в укритті́, на темному місці землі. Я не говорив до насі́ння Якова: Шукаєте да́рмо Мене! Я — Господь, — говорю́ справедливість, звіщаю правдиве!
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Збері́ться й прийді́ть, набли́зьтеся ра́зом, урято́вані всі із поганів! Не знає нічо́го, хто дерево носить, боввана свого, та що мо́литься богові, який не поможе.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Розкажіть та набли́зьте, і хай ра́зом нара́дяться: Хто розповів це відда́вна, із давніх часі́в це звісти́в? Чи ж не Я, ваш Госпо́дь? Бож немає вже Бога, крім Ме́не, окрім Мене нема Бога праведного та Спасителя!
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Зверніться до Мене й спасе́тесь, всі кі́нці землі, бо Я — Бог, і нема більше іншого Бога!
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 Я Собою Самим присяга́в, справедливість із уст Моїх ви́йшла, те слово, яке не пове́рнеться: усяке колі́но вклоня́тися буде Мені, усякий язик присягне́
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 й Мені скаже: Тільки в Господі правда та сила! При́йдуть до Нього та засоро́мляться всі, що на Ньо́го запа́люються.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 Через Господа усправедли́вляться, і буде просла́влене всяке насіння Ізраїля!
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< Ісая 45 >