< Ісая 25 >
1 Господи, — Ти мій Бог! Я буду Тебе велича́ти, хвали́тиму Йме́ння Твоє, бо Ти чудо вчинив, виконав давні прире́чення, певную правду!
Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
2 Бо Ти купою каменя місто вчинив, укріплене місто — руїною, чужине́цький пала́ц перестав бути містом, навіки не буде воно відбудо́ване!
Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
3 Тому буде хвалити Тебе наро́д сильний, місто лю́дів наси́льників буде боятись Тебе,
Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 бо твердинею став Ти нужде́нному, твердинею став для убогого в час його у́тиску, охороною від хуртови́ни, тінню від спе́ки, — і дух тих наси́льників був немов хуртови́на на сті́ну!
Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 Як спеко́ту в пустині, Ти крики чужи́нців прибо́ркав; як тінню від хмари спеко́ту, спів наси́льників так Він приглу́шить.
ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 І вчи́нить Господь Саваот на горі цій гости́ну з страв ситих, гостину із вин молодих, із шпіко́вого то́вщу, із очи́щених вин молодих.
Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 І Він на горі цій пони́щить засло́ну, заслону над усіма наро́дами, та покриття́, що розтягнене над усіма лю́дами.
Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 Смерть знищена буде наза́вжди, і витре сльозу́ Господь Бог із обличчя усякого, і га́ньбу народу Свого він усуне з усієї землі, бо Господь це сказав.
Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
9 І скажуть в той день: Це наш Бог, що на Нього ми мали надію — і Він спас нас! Це Господь, що на Нього ми мали надію, — тішмося ж ми та радіймо спасі́нням Його!
Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 Бо Господня рука на горі цій спочи́не, Моав же на місці своєму пото́птаний буде, як солома вито́птується у гної́вці,
Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 і простя́гне він руки свої серед неї, немов той плива́к простягає, щоб пли́вати, і прини́зить пиху́ його Він разом з пі́дступами його рук.
Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
12 А високу твердиню цих мурів твоїх Він розва́лить, пони́зить, на землю їх кине, у по́рох!
Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.