< Осія 2 >

1 Скажіть своїм братам: „Народ Мій“, а своїм сестрам: „Помилувана“.
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 Судіться з вашою матір'ю, судіться, бо вона не жінка Моя, а Я не її чоловік, і нехай вона відкине від себе свій блуд, і з-поміж своїх перс свій пере́люб,
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 щоб Я не роздягну́в її до́ нага, і не поставив її такою, як у день її наро́дження, і щоб не зробив Я її пустинею, і не обернув її на суху зе́млю, і не забив її спра́гою.
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 Над синами ж її Я не змилуюся, бо вони сини блу́ду,
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 бо їхня мати блудли́ва була, та, що ними була вагітна́, сором чинила, бо казала вона: Я піду́ за своїми полюбо́вниками, що дають мені хліб мій та воду мою, мою вовну та льон мій, оливу мою та напо́ї мої.
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Тому́ то ось Я вкрию твою дорогу те́рнями, і обгороджу́ її огоро́жею, — і стежо́к своїх не зна́йде вона.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 І буде вона гнатися за своїми полюбо́вниками, але́ не дожене́ їх, і буде шукати їх, та не зна́йде. І скаже вона: Піду́ я, і вернуся до мого першого чолові́ка, бо краще було мені тоді, як тепер.
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 А вона не знає, що то Я давав їй збіжжя, і виноградний сік, і свіжу оливу, і примно́жив їй срі́бло та золото, яке вони звернули на Ваала.
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 Тому́ то заберу́ назад Своє збіжжя в його ча́сі, а Мій сік виноградний в його умо́вленому ча́сі, і заберу́ Свою вовну та Свій льон, що був на покриття́ її наготи́.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 А тепер відкрию її наготу́ на оча́х її коха́нців, і ніхто не врятує її від Моєї руки.
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 І зроблю́ кінець усякій радості її, свя́ту її, новомі́сяччю її, і суботі її, та всякому святко́вому ча́сові.
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 І спусто́шу її виноградинка та її фіґове дерево, про які вона говорила: „Це мені дар за блудоді́йство, що дали́ мені мої полюбо́вники“. А Я оберну́ їх на ліс, — і їх пожере́ польова́ звірина́!
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 І навіщу́ її за дні Ваалів, коли вона кадила. І приоздбо́лювалася ти своєю носово́ю сере́жкою та своїм наши́йником, і ходила за своїми полюбо́вниками, а Мене забувала, говорить Госпо́дь.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 Тому́ то ось Я намо́влю її, і попрова́джу її до пустині, і буду говорити до серця її.
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 І дам їй виноградники звідти та долину Ахор за двері надії, і вона буде там співати, як за днів своєї мо́лодости, як за дня ви́ходу її з єгипетського кра́ю.
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 І станеться, того дня — говорить Господь — ти кликатимеш: „Чолові́че мій“, і не будеш більше кликати Мене: „Мій ваа́ле“.
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 I усу́ну іме́на Ваа́лів з її уст, і вони не будуть більше зга́дувані своїм і́менем.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 І складу́ їм заповіта того дня з польово́ю звірино́ю, і з птаством небесним, та з плазу́ючим по землі, і лука й меча та війну зни́щу з землі, і покладу́ їх безпечно.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 І заручу́ся з тобою навіки, і заручуся з тобою справедливістю, і правосу́ддям, і милістю та любов'ю.
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 І заручуся з тобою вірністю, і ти пізна́єш Господа.
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 І станеться того дня, Я почую, — говорить Господь, — почую небо, а воно почує землю,
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 а земля задоволи́ть збіжжя, і виноградний сік, і оливу, а вони задовольня́ть Їзреела.
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 І обсію її Собі на землі́, і змилуюся над Ло-Рухамою, і скажу до Ло-Амі: Ти наро́д Мій, а він скаже: Мій Боже!“
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”

< Осія 2 >