< Осія 14 >
1 Вернися, Ізраїлю, до Господа, Бога свого́, бо спіткну́вся ти через провину свою́!
Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 Візьміть із собою слова́, та й зверні́ться до Господа, до Нього промовте: „Прости́ нам усяку провину, та добре прийми, і ми принесе́мо у жертву плода́ своїх уст!
Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Ашшу́р не спасе нас, не бу́демо їздити ми на коні́, і не скажемо вже чи́нові рук наших: боже наш, бо тільки Тобою помилуваний сирота́“.
Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 „Ворохо́бність їхню вилікую, доброві́льно любитиму їх, бо Мій гнів відверну́вся від нього.
Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 Я буду Ізраїлеві, як роса́, розцвіте́ він, неначе ліле́я, і пустить корі́ння своє, мов Ліва́н.
Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 Розійду́ться його пагінці́, і буде його пишнота́, мов оли́вне те дерево, а па́хощ його — мов Ліва́н.
mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 Наве́рнуться ті, що сиділи під ті́нню його́, збіжжя ожи́влять вони й зацвіту́ть, немов той виногра́д, будуть згадки про нього, немов про ліва́нське вино́.
Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 Єфрем, — що йому до бовва́нів іще? Я вислухав вже та побачив його, Я для нього немов кипари́с той зелений: з Мене зна́йдений бу́де твій плід“.
Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Хто мудрий, то це зрозумі́є, розумний — і пізна́є, бо про́сті Господні доро́ги, і праведні ходять по них, а грішні спіткну́ться на них!
Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.