< Авакум 1 >
1 Пророцтво, яке бачив пророк Аваку́м.
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 Аж до́ки я, Господи, кли́кати буду, а Ти не почуєш? До тебе я кли́чу: „Наси́льство!“та Ти не спаса́єш!
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Для чого непра́вість мені Ти показуєш та позира́єш на му́ку? А передо мною грабі́ж та наси́льство, і супере́чка стається, і но́ситься сва́рка.
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 Тому то Зако́н припиня́ється, і не виходить до чину наза́всіди право, бо несправедливий вигу́блює праведного, тому правосуддя вихо́дить покри́вленим.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 Пригля́ньтеся ви до наро́дів, і диві́ться, і ду́же здиву́йтесь, бо вчиню́ Я за ваших днів ді́ло, про яке не повірите ви, коли буде розка́зане.
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 Бо оце Я поставлю халде́їв, народ лютий та скорий, що ґрасу́є по широкій землі, щоб захопи́ти оселі, які не його.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 Страшни́й та грізни́й він, — від нього само́го вихо́дить і право його, і вели́кість його.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 І від панте́р його коні швидші, і від вовкі́в вечеро́вих люті́ші. І розлетя́ться його́ верхівці́, а їздці́ його зда́лека при́йдуть, — вони будуть леті́ти, нена́че орел, що на їжу поспіша́є.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 Він прихо́дить увесь на наси́льство, а ціль їх обличчя — вперед, і набере́ полоне́них, як то́го піску́.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 І він глузу́є з царів, а князі́ — сміх для нього. Він сміється з тверди́ні усякої, бо на вал насипа́є землі, і її здобува́є!
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Тоді він несеться, як вітер, і пере́йде, і згріши́ть, бо зро́бить за бога свого́ оцю силу свою́.
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 Хіба ж Ти не відда́вна, о Господи? Боже Ти мій, мій Святий, — не помре́мо! Господи, Ти для суду поставив його́, і, о Скеле, призначив його на кара́ння!
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 Твої очі зана́дто пречисті, щоб міг Ти дивитись на зло, і на наси́льство дивитись не можеш. Чому ж дивишся Ти на грабі́жників, мовчиш, коли несправедливий винищує справедливішого від се́бе?
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 Ти ж маєш людей, як у морі тих риб, немов ту черву́, що пана над нею нема.
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 Усе́ це грабіжник витя́гує ву́дкою, своїм не́водом тя́гне оце́, та збирає оце́ в свою сітку, тому ті́шиться він та радіє.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 Тому жертву прино́сить він не́водові, — і ка́дить для сітки своєї, бо від них ситий у́діл його та добі́рна пожи́ва його!
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Чи на це випоро́жнює він свого не́вода, і за́вжди гото́в убивати наро́ди без милости?
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?