< Вихід 32 >
1 І побачив наро́д, що загаявся Мойсей зійти з гори. І зібрався наро́д проти Аарона, та й сказали до нього: „Устань, зроби нам богі́в, що бу́дуть ходити перед нами, бо той Мойсей, муж, що вивів був нас із єгипетського кра́ю, — ми не знаємо, що сталось йому“.
Anthu ataona kuti Mose akuchedwa kutsika mʼphiri, anasonkhana kwa Aaroni ndipo anati, “Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.”
2 І сказав їм Аарон „Поздіймайте золоті сере́жки, що в ушах ваших жінок, ваших синів та дочо́к ваших, і поприносьте до мене“.
Aaroni anawayankha kuti, “Vulani ndolo zagolide zimene avala akazi anu, ana anu aamuna ndi aakazi ndipo muzibweretse kwa ine.”
3 І ввесь наро́д поздіймав з себе золоті сережки, що в їхніх ушах, та й позно́сили до Аарона.
Kotero anthu onse anavula ndolo zagolide ndi kubwera nazo kwa Aaroni.
4 І взяв він це з їхньої руки, і вформував його в глині, і зробив із нього лите теля. А вони сказали: „Оце твої боги, Ізраїлю, що вивели тебе з єгипетського кра́ю!“
Choncho Aaroni analandira golideyo ndipo anamuwumba ndi chikombole ndi kupanga fano la mwana wangʼombe. Kenaka anthu aja anati, “Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.”
5 І побачив це Аарон, і збудував жертівника перед ним. І кликнув Аарон та й сказав: „Завтра свято для Господа!“
Aaroni ataona izi, anamanga guwa lansembe patsogolo pa mwana wangʼombeyo ndipo analengeza kuti, “Mawa kudzakhala chikondwerero cha Yehova.”
6 І повставали вони взавтра ра́но вранці, і принесли цілопа́лення, і привели́ мирну жертву. І засів наро́д до їди́ та до пиття́, і встали ба́витися.
Kotero tsiku linalo anthu anadzuka mmamawa ndithu ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Atatha kupereka nsembezo, anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.
7 А Господь промовляв до Мойсея: „Іди, зійди, бо зіпсувся наро́д твій, якого ти вивів із єгипетського краю.
Pamenepo Yehova anati kwa Mose, “Tsika msanga, chifukwa anthu ako amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto aja adziyipitsa kwambiri.
8 Зійшли вони скоро з дороги, що наказав був Я їм, — зробили собі лите теля, і поклонились йому, і склали йому́ жертви, та й сказали: Оце твої боги, Ізраїлю, що вивели тебе з єгипетського краю!“
Iwo apatuka mwamsanga kuleka kutsatira zimene ndinawalamula. Ndiye adzipangira fano la mwana wangʼombe. Aligwadira ndi kuliperekera nsembe nʼkumati, ‘Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
9 І промовив Господь до Мойсея: „Я бачив наро́д той, і ось наро́д — твердошиїй він!
Yehova anati kwa Mose, “Ine ndikuwadziwa anthu amenewa. Iwowa ndi ankhutukumve.
10 А тепер залиши Мене, — і розпа́литься гнів Мій на них, і Я ви́нищу їх, а тебе зроблю́ великим наро́дом“.
Chifukwa chake undileke kuti mkwiyo wanga uyake pa iwo ndi kuwawononga. Ndipo Ine ndidzakusandutsa kuti ukhale mtundu waukulu.”
11 І Мойсей став благати лице Господа, Бога свого, та й сказав: „На́що, Господи, розпа́люється гнів Твій на народ Твій, якого Ти випровадив з єгипетського кра́ю силою великою та міцно́ю рукою?
Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
12 На́що будуть казати єги́птяни, говорячи: На зле ти їх вивів, щоб їх повбивати в гора́х, та щоб винищити їх з пове́рхні землі?. Вернися з ро́зпалу гніву Свого, та й відверни́ зло від Свого́ наро́ду!
Kodi mukufuna kuti Aigupto azinena kuti, ‘Munali ndi cholinga choyipa chofuna kuwaphera ku mapiri kuno ndi kuwawonongeratu pa dziko lapansi pamene munkawatulutsa ku Igupto kuja?’ Ayi, chonde mkwiyo wanu woyaka ngati motowu ubwezeni ndipo sinthani maganizo ofunira zoyipa anthu anu.
13 Згадай про Авраама, Ісака та Ізраїля, рабів Своїх, що Ти їм присягався був Собою, та говорив їм: „Помно́жу ваших наща́дків, немов зорі небесні, і всю оту землю, що про неї казав, дам вашим наща́дкам, — і вони пося́дуть навіки“.
Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isake, Israeli ndi zija munawalonjeza polumbira pa dzina lanu kuti, ‘Ine ndidzachulukitsa zidzukulu zanu ndipo zidzakhala zambiri ngati nyenyezi zakumwamba. Zidzukulu zanuzo ndidzazipatsa dziko lonseli limene ndinalonjeza. Dziko limeneli lidzakhala lawo nthawi zonse.’”
14 І відверну́в Господь зло, про яке говорив, щоб зробити Своєму народо́ві.
Choncho Yehova analeka ndipo sanawachitire choyipa anthu ake monga anaopsezera.
15 І повернувся, і зійшов Мойсей із гори, — а в руці його дві табли́ці свідо́цтва, писані з обох їхніх сторін, — звідси й звідти вони були́ писані.
Mose anatembenuka ndi kutsika phiri miyala iwiri ya pangano ili mʼmanja mwake. Miyalayi inalembedwa mbali zonse, kutsogolo ndi kumbuyo komwe.
16 А табли́ці — Божа робота вони, а письмо — Боже письмо воно, ви́різьблене на табли́цях.
Miyalayi anayikonza ndi Mulungu. Malembawo analemba ndi Mulungu mozokota pa miyalapo.
17 І почув Ісус голос наро́ду, як кричав він, та й сказав до Мойсея: „Крик бо́ю в табо́рі!“
Pamene Yoswa anamva phokoso la anthu anati kwa Mose, “Ku msasa kuli phokoso la nkhondo.”
18 А той відказав: „Це не крик сили перемо́жців і не крик слабости переможених, — я чую голос співу!“
Mose anayankha kuti, “Phokoso limeneli sindikulimva ngati phokoso la opambana nkhondo, kapena kulira kwa ongonjetsedwa pa nkhondo. Koma ndikulimva ngati phokoso la anthu amene akuyimba.”
19 І сталося, коли він набли́зився до табо́ру, то побачив теля те та та́нці... І розпали́вся гнів Мойсеїв, і він кинув табли́ці із рук свої́х, — та й розторо́щив їх під горою!.
Mose atayandikira msasa ndi kuona mwana wangʼombe ndiponso kuvina, anakwiya kwambiri ndipo anaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwake, ndi kuyiphwanya pa tsinde la phiri.
20 І схопи́в він теля, що зробили вони, та й спалив на огні, та змолов, аж став порох І розси́пав на поверхні води, і напоїв тим синів Ізра́їлевих.
Ndipo iye anatenga mwana wangʼombe amene anthu anapanga uja ndi kumuwotcha pa moto ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi. Kenaka anawaza fumbilo mʼmadzi ndi kuwamwetsa Aisraeli madziwo.
21 І сказав Мойсей Ааронові: „Що́ вчинив тобі наро́д цей, що ти гріх великий навів на нього?“
Tsono Mose anafunsa Aaroni kuti, “Kodi anthu awa anakuchita chiyani kuti uwachimwitse koopsa chotere?”
22 А Аарон відказав: „Нехай не запа́литься гнів мого пана! Ти знаєш наро́д цей, що він у злому.
Aaroni anayankha kuti, “Musakwiye mbuye wanga. Inu mukudziwa kuti anthu awa ndi ovuta.
23 І вони сказали мені: Зроби нам богів, що будуть ходити перед нами, бо той Мойсей, муж, що вивів нас із єгипетського кра́ю, — ми не знаємо, що сталось йому.
Iwo anati kwa ine, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa ife mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.’
24 І сказав я до них: Хто має золото, — поздіймайте з себе. І дали вони мені, а я кинув його в огонь, — і вийшло те теля“.
Choncho ine ndinawawuza kuti, ‘Aliyense amene ali ndi zokometsera zagolide azivule.’ Choncho iwo anandipatsa golide, ndipo ndinamuponya pa moto ndi kupanga fano la mwana wangʼombeyu.”
25 І побачив Мойсей народ, що незагну́зданий він, бо Аарон розгнузда́в його на га́ньбу поміж їхніми ворогами.
Mose anaona kuti anthuwo anali osokonezekadi chifukwa Aaroni anawalekerera mpaka kusanduka anthu osekedwa pakati pa adani awo.
26 І став Мойсей у брамі табо́ру й сказав: „Хто за Господа — до мене!“І зібралися до нього всі Левіїні сини.
Choncho iye anayima pa chipata cholowera mu msasa ndipo anati, “Aliyense amene ali mbali ya Yehova abwere kwa ine.” Ndipo Alevi onse anapita mbali yake.
27 І сказав він до них: „Так сказав Господь, Бог Ізраїлів: Припаші́ть кожен меча свого́ на стегно́ своє, перейдіть, і верніться від брами до брами в табо́рі, — і повбивайте кожен брата свого, і кожен приятеля свого, і кожен бли́жнього свого́“.
Ndipo iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena, ‘Pitani ku misasa konse, mulowe ku zipata zonse ndipo aliyense akaphe mʼbale wake, kapena mnzake kapena mnansi wake.’”
28 І зробили Левіїні сини за словом Мойсеєвим. І впало з наро́ду того дня близько трьох тисяч чоловіка.
Alevi anachita zomwe Mose analamula, ndipo tsiku limenelo panafa anthu pafupifupi 3,000.
29 І сказав Мойсей: „Освятіть сьогодні себе для Господа, бо кожен мстився на сині своїм та на браті своїм, і щоб сьогодні Він дав вам благослове́ння“.
Kenaka Mose anati, “Lero mwadzipatula nokha kukhala ansembe otumikira Yehova. Mwachita izi popeza aliyense wa inu wapha mwana wake kapena mʼbale wake. Tsono lero Yehova wakudalitsani.”
30 І сталося назавтра, і сказав Мойсей до народу: „Ви згрішили великим гріхом, а тепер зійду́ я до Господа, — може складу́ оку́плення за ваш гріх“.
Mmawa mwake Mose anati kwa anthu onse, “Inu mwachita tchimo lalikulu. Koma tsopano ine ndipita ku phiri kwa Yehova mwina ndikatha kukupepeserani chifukwa cha tchimo lanu.”
31 І вернувся Мойсей до Господа та й сказав: „О, згрішив цей наро́д великим гріхом, — вони зробили собі золотих богі́в!
Kotero Mose anabwereranso kwa Yehova ndipo anati, “Aa! Anthu awa achita tchimo lalikulu! Iwo adzipangira milungu yagolide.
32 А тепер, коли б Ти пробачив їм їхній гріх! А як ні, — витри мене з книги Своєї, яку Ти написав“.
Koma tsopano, chonde akhululukireni tchimo lawo. Ngati simutero, ndiye mundifute ine mʼbuku limene mwalemba.”
33 І промовив Господь до Мойсея: „Хто згрішив Мені, того витру із книги Своєї.
Yehova anamuyankha Mose kuti, “Ndidzafuta mʼbuku aliyense amene wandichimwira.
34 А тепер іди, провадь цей народ туди, куди казав Я тобі. Ось Мій Ангол піде перед лицем твоїм. А в день кари Моєї — покараю їх за їхній гріх!
Tsopano pita ukawatsogolere anthu kumalo kumene ine ndinanena, ndipo mngelo wanga adzakutsogolerani. Komabe, nthawi yanga ikadzafika kuti ndiwalange, ndidzawalanga chifukwa cha tchimo lawo.”
35 І Господь ударив той народ за те, що вони зробили теля, яке Аарон учинив був.
Ndipo Yehova anawakantha anthuwo ndi mliri chifukwa anawumiriza Aaroni kuti awapangire fano la mwana wangʼombe.