< Естер 6 >

1 Тієї ночі втік був сон від царя, і він сказав прине́сти Книгу пам'яток, Хроніки, — і вони читалися перед обличчям царськи́м.
Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
2 І зна́йдене було́ написане, що Мордехай доніс на Біґдана та Тереша, двох царськи́х е́внухів, зо сторо́жів поро́га, що заду́мували були простягнути руку на царя́ Ахашверо́ша.
Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
3 І сказав цар: „Яка честь та гі́дність зро́блена Мордеха́єві за це?“І сказали ца́реві о́троки, що прислуго́вували йому: „Нічо́го йому́ не зро́блено“...
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
4 І спита́в цар: „Хто́ на подві́р'ї?“А Га́ман прийшов на зо́внішнє подві́р'я царсько́го дому, щоб сказати цареві пові́сити Мордехая на тій ши́бениці, яку пригото́вив для нього.
Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
5 І сказали о́троки царя до нього: „Ось Га́ман стоїть на подві́р'ї“. І сказав цар: „Нехай уві́йде!“
Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
6 І Гаман увійшов, а цар йому сказав: „Що́ зробити з чоловіком, якому цар хоче чести?“І подумав Гаман у серці своїм: „Кому ж цар зажадає вчинити честь більше, як мені?“
Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
7 І відповів Гаман царе́ві: „Тому чоловікові, якому цар жадає чести,
Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
8 нехай принесу́ть цареву одежу, яку цар зодягав, та коня, що цар їздив на ньому, і щоб була да́на царська́ корона на його го́лову.
Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
9 І дати цю одежу та цього коня на руку котро́гось із старших князі́в царе́вих. І нехай зодя́гнуть того чоловіка, якому цар жадає чести, і нехай во́зять його на коні на міські́й площі, і нехай кличуть перед ним: „Так ро́биться му́жеві, якому цар жадає чести!“
Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
10 І сказав цар до Гамана: „Поспіши, візьми́ одежу та коня, як казав ти, і зроби так юдеєві Мордеха́єві, що сидить у царській брамі. Не пропусти нічого зо всього, що́ ти говорив!“
Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
11 І взяв Гаман одежу та коня, і зодягнув Мордехая, і возив його на міські́й площі, і кричав перед ним: „Так ро́биться му́жеві, якому цар жадає чести!“
Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
12 I вернувся Мордеха́й до царсько́ї брами, а Га́ман поспішив до дому свого сумни́й та закривши го́лову.
Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
13 І розповів Гаман жінці своїй Зереші та всім при́ятелям своїм усе, що спіткало його. І сказали йому мудреці його та жінка його Зе́реш: „Якщо з юдейського насіння Мордехай, перед яким зачав ти падати, то не переможеш його, бо дійсно впаде́ш перед ним!“
Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
14 Ще вони говорили з ним, а е́внухи царські́ прибули́ й поспішили відве́сти Гамана на гости́ну, яку зробила Есте́р.
Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.

< Естер 6 >