< Естер 1 >
1 І сталося за днів Ахашверо́ша, це той Ахашверо́ш, що царював від Індії аж до Етіопії, сто й двадцять і сім окру́г, —
Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
2 за тих днів, коли цар Ахашверош засів на троні свого царства, на замку Су́зи.
Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
3 Третього року свого царюва́ння справив він гости́ну для всіх своїх князі́в та для своїх слуг ві́йська перського та мідійського, старши́х та прави́телів округ,
ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
4 показуючи ба́гатство слави царства свого й пишну славу своєї вели́чности довгі дні, сто й вісімдесят день.
Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
5 А по скінченні цих днів справив цар для всього наро́ду, що знахо́дився в за́мку Су́зи, від великого й аж до мало́го, гости́ну на сім день на садко́вому подві́р'ї царсько́го пала́цу.
Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
6 Біла, зелена та блаки́тна ткани́на, три́мана віссо́новими та пурпу́ровими шну́рами, ви́сіла на срібних стовпця́х та мармуро́вих коло́нах. Золоті та срібні ло́жа стояли на підлозі з пли́ток з зеленого, білого, жовтого й чорного ма́рмуру.
Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
7 А напо́ї подавали в золотому по́суді, в посуді все різному, і царсько́го вина було ве́льми щедро, за великою спромо́жністю царя.
Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
8 А пиття було за встановленим порядком, — ніхто не приму́шував, бо цар так установи́в усім значни́м свого дому, щоб чинили за вподо́бою кожного.
Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
9 Також цариця Ва́шті спра́вила гости́ну для жіно́к в царсько́му домі царя Ахашверо́ша.
Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
10 Сьо́мого дня, коли цареві стало ве́село на серці від вина, він сказав Мегуманові, Біззеті, Харвоні, Біґті, і Аваґті, Зетарові та Каркасові, сімо́м е́внухам, які служили перед обличчям царя Ахашвероша,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
11 приве́сти царицю Вашті перед цареве обличчя в короні царські́й, щоб показати наро́дам та зверхникам її красу́, бо була вона вродли́вого ви́гляду.
kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
12 Та цариця Ва́шті відмо́вилася прийти за царськи́м словом, що було передане їй через е́внухів. І сильно загні́вався цар, і в ньому горіла його лю́тість!
Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
13 І сказав цар до мудреців, що знають часи́ (бо так царська́ справа йшла перед усіма́, що знали зако́на та право,
Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
14 а близьки́ми до нього були: Каршена, Шетар, Адмата, Паршіш, Мерес, Марсена, Мемухан, сім князів перськи́х та мідійських, які бачать царе́ве обличчя й сидять перші в царстві):
Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
15 „Як велить зако́н, щоб зробити з царицею Вашті за те, що не виконала сло́ва царя Ахашвероша, переданого їй через євнухів?“
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
16 І сказав Мемухан перед царем та князя́ми: „Не перед сами́м царе́м провини́лася цариця Вашті, але й перед усіма́ князя́ми та перед усіма́ народами, що по всіх окру́гах царя Ахашвероша.
Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
17 Бо цари́цин учи́нок ді́йде до всіх жіно́к, і спричи́ниться до пого́рдження їхніх чолові́ків в їхніх оча́х, бо бу́дуть говорити: Цар Ахашверо́ш сказав був приве́сти царицю перед обличчя своє, та вона не прийшла́!
Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
18 І цього дня казатимуть те саме княгині перські та мідійські, що почують про цари́цин учи́нок, до всіх царськи́х князі́в, — і бу́де багато пого́рди та гніву!
Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
19 Якщо цареві це добре, нехай ви́йде царськи́й нака́з від нього й нехай буде записане в зако́нах Персії та Мідії, і нехай не поминеться, щоб Вашті більш не прихо́дила перед обличчя царя Ахашвероша, а її царюва́ння цар дасть іншій, ліпшій від неї.
“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
20 А коли почується царськи́й нака́з, який цар зробить відо́мим у всім своїм царстві, хоч яке велике воно, то всі жінки́ віддадуть честь своїм чоловікам, від великого й аж до мало́го“.
Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
21 І була приємна ця рада в оча́х царя та князі́в, і цар зробив за Мемухановим словом.
Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
22 І порозсила́в він листи до всіх царськи́х окру́г, до кожної округи — письмо́м її, і до кожного наро́ду — мовою його́, щоб кожен чоловік був па́ном у домі своєму, і говорив про це мовою свого наро́ду.
Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.