< Екклезіяст 1 >
1 Книга Пропові́дника, сина Давидового, царя в Єрусалимі.
Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2 Наймарні́ша марно́та, сказав Пропові́дник, наймарні́ша марно́та, — марно́та усе!
“Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
3 Яка ко́ристь люди́ні в усім її тру́ді, який вона робить під сонцем?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4 Поколі́ння відхо́дить, й поколі́ння приходить, а земля вікові́чно стоїть!
Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5 І со́нечко схо́дить, і сонце заходить, і поспішає до місця свого́, де схо́дить воно.
Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6 Віє вітер на пі́вдень, і на північ верта́ється, кру́титься, крутиться він та й іде, і на круг свій верта́ється вітер.
Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7 Всі пото́ки до моря пливуть, але море — воно не напо́внюється: до місця, ізві́дки пливуть, ті потоки вони поверта́ються, щоб зно́ву плисти́!
Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
8 Повні тру́ду всі ре́чі, — люди́на сказати всього́ не потра́пить! Не наси́титься ба́ченням око, і не напо́вниться слу́ханням ухо.
Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9 Що було́, воно й бу́де, і що робилося, бу́де робитись воно, — і немає нічо́го ново́го під сонцем!
Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10 Буває таке, що про нього говорять: „Дивись, — це нове́!“Та воно вже було́ від вікі́в, що були́ перед нами!
Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
11 Нема згадки про перше, а тако́ж про насту́пне, що бу́де, — про них згадки не бу́де між тими, що бу́дуть пото́му.
Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
12 Я, Проповідник, був царем над Ізраїлем в Єрусалимі.
Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
13 І поклав я на серце своє, щоб шукати й дослі́джувати мудрістю все, що робилось під небом. Це праця тяжка́, яку дав Бог для лю́дських синів, щоб мозо́литись нею.
Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
14 Я бачив усі справи, що чини́лись під сонцем: й ось усе це — марно́та та ло́влення вітру!
Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15 Покри́вленого не напра́виш, а неісну́ючого не полі́чиш!
Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16 Говорив я був з серцем своїм та казав: Ось я велику премудрість набув, Найбільшу за всіх, що до ме́не над Єрусалимом були́. І бачило серце моє всяку мудрість і знання.
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
17 І поклав я на серце своє, щоб пізнати премудрість, і пізнати безу́мство й глупо́ту, — і збагну́в я, що й це все — то ло́влення вітру!
Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18 Бо при мно́гості мудрости мно́житься й кло́піт, хто ж пізна́ння побільшує, той побільшує й біль!
Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.