< Екклезіяст 4 >
1 І знов я побачив всі у́тиски, що чинились під сонцем, — і сльоза́ ось ути́скуваних, та немає для них потіши́теля, і наси́лля з руки, що їх гно́блять, і немає для них потіши́теля.
Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano: ndinaona misozi ya anthu opsinjika, ndipo iwo alibe owatonthoza; mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo ndipo iwonso analibe owatonthoza.
2 І я похвалив тих померлих, що давно повмирали, більш від живих, що живуть дотепе́р.
Ndipo ndinanena kuti akufa, amene anafa kale, ndi osangalala kuposa amoyo, amene akanalibe ndi moyo.
3 А краще від них від обох тій люди́ні, що досі іще не була́, що не бачила чину лихого, що робився під сонцем!
Koma wopambana onsewa ndi amene sanabadwe, amene sanaone zoyipa zimene chimachitika pansi pano.
4 І я бачив ввесь труд та ввесь у́спіх учи́нку, виклика́є заздрість одно́го до о́дного, — і це все марно́та та ло́влення вітру!.
Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
5 Нерозумний сидить, склавши руки свої, та жере́ своє тіло, —
Chitsiru chimangoti manja ake lobodo ndi kudzipha chokha ndi njala.
6 краща повна долоня споко́ю за повні дві жмені кло́поту та за ло́влення вітру!
Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere, kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto, ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.
7 І зно́ву я бачив марно́ту під сонцем:
Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:
8 Буває само́тній, і не має ніко́го він іншого, сина чи брата у ньо́го нема, та немає кінця всьому зуси́ллю його, і не наси́титься око багатством його, і він не пові́сть: „Та для кого дба́ю і позбавляю добра свою душу?“Марно́та й оце, і даремна робота воно.
Panali munthu amene anali yekhayekha; analibe mwana kapena mʼbale. Ntchito yake yolemetsa sinkatha, ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake. Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?” Izinso ndi zopandapake, zosasangalatsa!
9 Краще двом, як одному, бо мають хорошу заплату за труд свій,
Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha, chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:
10 і якби вони впали, піді́йме одне́ свого друга! Та горе одно́му, як він упаде́, й нема дру́гого, щоб підве́сти його.
Ngati winayo agwa, mnzakeyo adzamudzutsa. Koma tsoka kwa munthu amene agwa ndipo alibe wina woti amudzutse!
11 Також коли вдвох покладу́ться, то тепло їм буде, а я́к же зогрі́тись одно́му?
Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana. Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?
12 А коли б хто напав на одно́го, то вдвох вони стануть на нього, — і нитка потрійна не скоро пірве́ться!
Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa, koma anthu awiri akhoza kudziteteza. Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.
13 Ліпший убогий та мудрий юна́к, аніж цар стари́й та нерозумний, що вже осторо́г не приймає,
Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo.
14 бо виходить юнак і з в'язни́ці, щоб зацарюва́ти, хоч у царстві своїм народивсь він убогим!
Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo.
15 Я бачив усіх живих, що ходять під сонцем, на боці цього́ юнака́, — цього дру́гого, що став він на місце його.
Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu.
16 Немає кінця всьому лю́дові, всьо́му, що був перед ним, та й насту́пні не втішаться ним, — бо й це теж марно́та та ло́влення вітру!
Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.