< Повторення Закону 4 >

1 А тепер, Ізра́їлю, послухай постанов та зако́нів, що я навчаю вас чинити, щоб жили́ ви, і ввійшли, й посіли цей край, що Господь, Бог батьків ваших, дає вам.
Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
2 Не додава́йте до того, що я вам наказую, і не зменша́йте з того, щоб виконувати заповіді Господа, Бога вашого, що я наказав вам.
Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
3 Очі ваші бачили те, що Господь зробив був з Ваалом пеорським, бо кожного чоловіка, що пішов за пеорським Ваалом, вигубив його Господь, Бог твій, з-посеред тебе.
Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
4 А ви, що ли́нули до Господа, Бога вашого, усі ви живі сьогодні.
Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
5 Дивіться, — навчив я вас постанов та зако́нів, як наказав мені Господь, Бог мій, чинити так серед того Кра́ю, куди ви входите, щоб посісти його.
Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
6 Бережіть, і виконуйте їх, бо це мудрість ваша та ваш розум на оча́х наро́дів, що ви́слухають усіх постанов тих та й скажуть: Тільки він мудрий та розумний наро́д, цей великий люд!
Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
7 Бо хто інший такий великий народ, що мав би богів, таких йому близьки́х, як Господь, Бог наш, кожного ра́зу, як ми кличемо до Нього?
Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
8 І хто і́нший такий великий народ, що має постанови й зако́ни такі справедливі, як увесь той Зако́н, що я даю перед вами сьогодні?
Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
9 Тільки стережися, і дуже пильнуй свою душу, щоб не забув ти тих речей, що бачили очі твої, і щоб вони не повихо́дили з серця твого по всі дні життя твого, а ти подаси їх до ві́дома синам твоїм та синам твоїх синів,
Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
10 про день, коли стояв ти перед лицем Господа, Бога твого, на Хори́ві, як Господь говорив був до мене: „Збери Мені той народ, і вони слухатимуть слів Моїх, із яких навчаться боятися Мене по всі дні, скільки вони житимуть на землі, та й синів своїх понавча́ють“.
Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
11 І поприхо́дили ви, та й поставали під горою, а гора та горіла огнем аж до самих небес, а при тому була темрява, хмара та мряка.
Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
12 І промовляв Господь до вас із сере́дини огню, — голос слів ви чули, та виду ви не бачили, окрім голосу.
Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
13 І Він оголосив перед вами заповіта Свого, що наказав вам чинити, — Десять Заповідей, і написав їх на двох камі́нних табли́цях.
Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
14 А мені Господь наказав того ча́су навчати вас постанов та зако́нів, щоб виконували ви їх у краю́, куди ви перехо́дите володіти ним.
Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
15 І бу́дете ви сильно стерегти свої душі, бо не бачили ви того дня жодної постаті, коли говорив Господь до вас на Хориві з сере́дини огню,
Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
16 щоб ви не зіпсулися, і не зробили собі ідола на подобу якогось бовва́на, зобра́ження самця́ чи самиці,
kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
17 зобра́ження всякої худобини, що на землі, зобра́ження всякого крилатого пта́ха, що літає під небом,
kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
18 зобра́ження всякого плазу́ючого по землі, зобра́ження всякої риби, що в воді під землею,
Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
19 і щоб ти, звівши очі свої до неба, і побачивши сонце, і місяць, і зорі, — усе військо небесне, щоб не був ти зве́дений і не вклонявся їм, і не служив їм; бо Господь, Бог твій, приділив їх усім наро́дам під усім небом.
Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
20 А вас Господь узяв та й вивів вас із залізної гутни́чої пе́чі, — з Єгипту, щоб ви стали для Нього наро́дом наді́лу, як сьогодні це ви́дко.
Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
21 А Господь був розгнівався на мене за ваші діла́, і поклявся, що не перейду́ я Йорда́ну, і не ввійду́ до того хорошого кра́ю, що Господь, Бог твій, дає тобі на спа́дщину.
Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
22 Бо я умру в цьому кра́ї, я не перейду́ Йорда́ну, а ви пере́йдете й посядете той хороший край.
Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
23 Стережіться, щоб не забули ви заповіту Господа, вашого Бога, якого склав з вами, щоб не зробили ви собі бовва́на на подобу всього, як наказав тобі Господь, Бог твій.
Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
24 Бо Господь, Бог твій, — Він палю́чий огонь, Бог за́здрісний.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
25 Коли ти породиш синів, і синів твоїх синів, і поста́рієте ви в краю́, і зіпсуєтеся, і зробите бовва́на на подобу чогось, і зробите зло в оча́х Господа, Бога свого, та Його розгнівите́,
Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
26 то беру Я сьогодні за свідків проти вас небо й землю, що незаба́ром конче погинете в краю́, на вспадкува́ння якого ви перехо́дите туди Йорда́н. Не будуть довгі ваші дні в ньому, бо конче ви будете ви́гублені.
ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
27 І розпоро́шить вас Господь посеред народів, і будете ви нечисле́нні поміж людами, куди попрова́дить вас Господь.
Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
28 І будете служити там богам, ділу рук лю́дських, дереву та каменеві, які не бачать, і не чують, і не їдять, і не нюхають.
Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
29 Та коли ви будете шукати звідти Господа, Бога свого, то зна́йдете, якщо будете шукати Його всім серцем своїм та всією душею своєю.
Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
30 Як будеш у біді своїй, і коли спіткають тебе в кінці днів усі оці речі, то ве́рнешся ти до Господа, Бога свого, і послухаєш Його голосу.
Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
31 Бо Господь, Бог твій — Бог милости́вий: Він не залишить тебе й не знищить тебе, і не забуде заповіту батьків твоїх, яким їм присягнув був.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
32 Бо питай но про перші дні, що були перше тебе, від того дня, коли Бог створив люди́ну на землі, і від кінця неба й аж до кінця неба, — чи бувало щось таке, як ця велика річ, або чи чуте було щось таке, як вона:
Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
33 чи чув народ голос Бога, що говорив із сере́дини огню, як чув ти і жив?
Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
34 Або чи намагався який бог піти взяти собі народ з-посеред іншого народу пробами, ознаками, і чудами, і війною, і сильною рукою, і раме́ном ви́тягненим, і стра́хами великими, як усе те, що зробив був вам Господь, Бог ваш, в Єгипті на оча́х твоїх?
Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
35 Тобі було показане це, щоб ти пізнав, що Господь — Він Бог, і нема іншого, окрім Нього.
Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
36 Він дав тобі з неба почути Його голос, щоб навчити тебе, а на землі показав тобі Свій великий огонь, і слова́ Його чув ти з сере́дини огню.
Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
37 І тому, що кохав Він батьків твоїх, то вибрав їхнє насіння по них, і Сам Він вивів тебе Своєю великою силою з Єгипту,
Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
38 щоб прогнати перед тобою народи, більші й сильніші за тебе, щоб ввести тебе, та дати тобі їхній край на спа́док, як сьогодні це ви́дко.
kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
39 І пізнаєш сьогодні, і ві́зьмеш до серця свого, що Господь — Він Бог на небі вгорі й на землі долі, — іншого нема.
Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
40 І будеш пильнувати постанов Його та заповідей Його, що я наказую тобі сьогодні, щоб було добре тобі та синам твоїм по тобі, і щоб ти продо́вжив дні на землі, що Господь, Бог твій, дає тобі на всі дні".
Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
41 Тоді виділив Мойсей три місті по той бік Йорда́ну на схід сонця,
Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
42 щоб утікав туди убійник, що замордує свого ближнього ненароком, а він не був йому ворогом ні вчора, ані позавчора. І втече він до одно́го з цих міст, і буде жити:
kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
43 Бецер у пустині, у кра́ї рівниннім, Рувимовому, і Рамот у Ґілеаді Ґадовому, і Ґолан у Башані Манасіїному.
Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
44 І оце Зако́н, що Мойсей поклав перед Ізраїлевими синами,
Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
45 оце свідо́цтва, і постанови, і зако́ни, що Мойсей говорив їх до Ізраїлевих синів при виході їх із Єгипту,
Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
46 по той бік Йорда́ну в долині навпроти Бет-Пеору в краю́ Сигона, царя аморейського, що сидів у Хешбоні, якого побив Мойсей та Ізраїлеві сини при виході їх із Єгипту.
Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
47 І вони оволоділи краєм його та краєм Оґа, башанського царя, обох аморейських царів, що по той бік Йорда́ну на схід сонця,
Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
48 від Ароеру, що над берегом арнонського потоку, і аж до гори Сіон, цебто Гермон,
Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
49 і ввесь степ по тім боці Йорда́ну на схід і аж до моря сте́пу під узбі́ччям Пісґі.
ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.

< Повторення Закону 4 >