< Амос 4 >
1 Послухайте сло́ва оцього, коро́ви баша́нські, які на горі самарі́йській, що тиснете бідних, торо́щите вбогих, що своїм хазяя́м ви говорите: „Принеси, і ми бу́демо пити!“
Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
2 Присягав Господь Бог Своєю святістю, що ось дні настаю́ть на вас, і будуть тягти вас гака́ми, а ваших наща́дків — гачка́ми для ло́влення риби!
Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
3 І ви повихо́дите ви́ломами, кожна окремо собі, і ки́нетеся до Хермо́ну, говорить Госпо́дь.
Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
4 Прийдіть до Бет-Елу й грішіть, до Ґілґа́лу — примно́жте грішити. І свої жертви прино́сьте щора́нку, на три дні — ваші десятини.
“Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
5 І з димом пустіть жертву вдячну квасну́, і сповістіть добровільні дару́нки, розголосі́ть, бо ви любите так, сино́ве Ізраїлеві, говорить Господь Бог.
Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
6 І тому́ Я вам дав чистоту́ зубів по всіх ваших міста́х, і брак хліба по всіх ваших місця́х, та ви не верну́лись до Мене, говорить Госпо́дь.
“Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
7 І Я стримав вам дощ за три місяці перед жнива́ми, і дощ посилав на одне місто, а на друге місто не посилав; одна діля́нка була побита дощем, а ділянка, на яку не пустив Я дощу, висиха́ла.
“Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
8 І два-три мі́ста рушали до міста одно́го напитись води, але́ не наси́чувались, — та ви не вернулись до Мене, говорить Госпо́дь.
Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
9 Я бив вас посу́хою та зеленя́чкою, сарана́ жерла бе́зліч ваших садків й виноградників ваших, і ваших фіґо́вниць та ваших олив, — та ви не верну́лись до Мене, говорить Госпо́дь.
“Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
10 Я на вас посилав морови́цю, немов на Єгипет, мечем побивав ваших хло́пців, поло́нячи ра́зом і ко́ней у вас, підіймав до нізде́р сморід ваших табо́рів, — та ви не вернулись до Мене, говорить Господь.
“Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
11 Я ви́нищив вас, як Содо́м та Гомо́рру Бог винищив, і ви стали, немов голове́шка, з пожа́ру врято́вана, — та ви не вернулись до Мене, говорить Господь.
“Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
12 Тому́ то зроблю́ тобі так, о Ізраїлю, а що Я зроблю́ тобі це, приготуйся, Ізраїлю, до зу́стрічі Бога свого́!
“Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
13 Бо це Той, що вформо́вує гори, і що ство́рює вітра, що люди́ні показує за́дум її, що робить зірни́цю темно́тою, і ступає по згі́р'ях землі, — Господь Бог Савао́т Йому Йме́ння!
Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.